< Jeremiasza 31 >

1 Czasu onego, mówi Pan, będę Bogiem wszystkim rodzajom Izraelskim, a oni będą ludem moim.
“Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
2 Tak mówi Pan: Znalazł łaskę na puszczy lud, który uszedł miecza, gdym chodził przed nim, abym odpocznienie uczynił Izraelowi.
Yehova akuti, “Anthu amene anapulumuka ku nkhondo ndinawakomera mtima mʼchipululu; pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”
3 Rzeczeszli: Zdawna mi się Pan ukazywał. I owszem, miłością wieczną umiłowałem cię, dlategoć ustawicznie miłosierdzie pokazuję;
Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati, “Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire. Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
4 Jeszcze cię zbuduję, a zbudowana będziesz, panno Izraelska! jeszcze się weselić będziesz przy bębnach swoich, a wychodzić z hufem pląsających;
Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli; mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu, ndipo mudzapita kukavina nawo anthu ovina mwachimwemwe.
5 Jeszcze będziesz sadziła winnice na górach Samaryjskich; a szczepiący szczepić będą i jeść będą.
Mudzalimanso minda ya mpesa pa mapiri a Samariya; alimi adzadzala mphesa ndipo adzadya zipatso zake.
6 Bo nastanie dzień, którego stróżowie wołać będą na górze Efraimowej: Wstańcie a wstąpmy na Syon do Pana, Boga swego.
Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula pa mapiri a Efereimu nati, ‘Tiyeni tipite ku Ziyoni, kwa Yehova Mulungu wathu.’”
7 Tak zaiste mówi Pan: Śpiewajcie Jakóbowi o rzeczach wesołych, a wykrzykajcie jawnie przed tymi narodami; wydawajcie głos, chwałę oddawajcie a mówcie: Panie! wybaw ostatek ludu twego Izraelskiego.
Yehova akuti, “Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo, fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse. Matamando anu amveke, ndipo munene kuti, ‘Yehova wapulumutsa anthu ake otsala a Israeli.’
8 Oto Ja przywiodę ich z ziemi północnej, a zbiorę ich ze wszystkich stron ziemi; z nimi pospołu ślepego i chromego, brzemienną i rodzącą: tu się gromadą wielką nawrócą.
Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto, ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi. Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
9 Przywiodę ich zasię z płaczem i z modlitwami idących, a powiodę ich podle potoków wód drogą prostą, na którejby się nie potknęli; bom się stał Izraelowi ojcem, a Efraim jest pierworodnym moim.
Adzabwera akulira; koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza. Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo. Chifukwa ndine abambo ake a Israeli, ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
10 Słuchajcie słowa Pańskiego, o narody! a opowiadajcie je na wyspach dalekich, i mówcie: Ten, który rozproszył Izraela, zgromadzi go, a strzedz go będzie, jako pasterz trzody swojej.
“Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
11 Bo wykupił Pan Jakóba; przeto wybawi go z ręki tego, który jest mocniejszy nadeń.
Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
12 I przyjdą a śpiewać będą na wysokości Syonu, i zbieżą się do dobrotliwości Pańskiej ze zbożem i z winem, i z oliwą i z jagniętami, i z cielętami, a dusza ich podobna będzie ogrodowi wilgotnemu, a nie będzie się więcej smuciła.
Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni; adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova. Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta, ana ankhosa ndi ana angʼombe. Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino, ndipo sadzamvanso chisoni.
13 Tedy się weselić będzie panna z pląsaniem, także młodzieńcy i starcy społem; albowiem kwilenie ich obrócę w radość, a pocieszę ich, i rozweselę ich po smutku ich;
Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala. Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala. Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo; ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
14 I opoję duszę kapłanów tłustością, a lud mój dobrocią moją nasyci się, mówi Pan.
Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,” akutero Yehova.
15 Tak mówi Pan: Głos w Rama słyszany jest, narzekanie i płacz bardzo gorzki; Rachel płacząca synów swoich nie dała się pocieszyć po synach swoich, przeto, że ich niemasz.
Yehova akuti, “Kulira kukumveka ku Rama, kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake. Sakutonthozeka chifukwa ana akewo palibe.”
16 Tak mówi Pan: Zawściągnij głos swój od płaczu, a oczy swe od łez; bo będziesz miała zapłatę za pracę swoję, mówi Pan, że się nawrócą z ziemi nieprzyjacielskiej.
Yehova akuti, “Leka kulira ndi kukhetsa misozi pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,” akutero Yehova. “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
17 Jest mówię nadzieja, że się potem nawrócą, mówi Pan, synowie twoi do krainy swojej.
Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,” akutero Yehova. “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.
18 Wprawdzie słyszę Efraima, że sobie utyskuje, mówiąc: Pokarałeś mię, abym był pokarany jako cielec nieokrócony. Nawróć mię abym był nawrócony; tyś zaiste Panie! Bóg mój.
“Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti, ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva. Koma inu mwatiphunzitsa kumvera. Mutibweze kuti tithe kubwerera, chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
19 Bo po nawróceniu mojem pokutować będą; a gdy samego siebie poznam, uderzę się w biodro; wstydzę się, owszem i zapałam się, że odnoszę hańbę dzieciństwa swego.
Popeza tatembenuka mtima, ndiye tikumva chisoni; popeza tazindikira ndiye tikudziguguda pachifukwa. Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
20 Izali synem moim miłym nie jest Efraim? Izali nie jest dziecięciem rozkosznem? Bo od onego czasu, jakom mówił przeciwko niemu, przecież nań ustawicznie wspominam; dlatego poruszają się wnętrzności moje nad nim, zaiste zlituję się nad nim, mówi Pan.
Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa, mwana amene Ine ndimakondwera naye? Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukumbukirabe. Kotero mtima wanga ukumufunabe; ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,” akutero Yehova.
21 Wystaw sobie pamiątki; nakładź sobie gromad kamieni; pamiętaj na ten gościniec, i na drogę, którąś chodziła: nawróć się, panno Izraelska! nawróć się do tych miast swoich.
“Muyike zizindikiro za mu msewu; muyimike zikwangwani. Yangʼanitsitsani msewuwo, njira imene mukuyendamo. Bwerera, iwe namwali wa Israeli, bwerera ku mizinda yako ija.
22 Dokądże się tułać będziesz, córko odporna? Bo uczyni Pan rzecz nową na ziemi: niewiasta ogarnie męża.
Udzakhala jenkha mpaka liti, iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika? Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”
23 Tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Jeszcze mówić będę słowo to w ziemi Judzkiej, i w miastach jej, gdy przywiodę więźniów ich: Niech cię błogosławi Pan, o mieszkanie sprawiedliwości! o góro świętobliwości!
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
24 Albowiem osadzać się będą w ziemi Judzkiej we wszystkich miastach jego społem oracze, i ci, którzy chodzą za stadem.
Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
25 Napoję zaiste duszę spracowaną, a wszelką duszę smutną nasycę.
Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
26 Wtemem ocucił i spojrzałem, a sen mój był mi wdzięczny.
Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
27 Oto dni idą, mówi Pan, w których posieję dom Izraelski i dom Judzki nasieniem człowieczem i nasieniem bydlęcem;
“Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
28 A jakom się starał, abym ich wykorzenił, i burzył, i kaził, i gubił, i trapił: tak się starać będę, abym ich pobudował i rozsadził, mówi Pan.
Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
29 Za onych dni nie będą więcej mówić: Ojcowie jedli grona cierpkie, a synów zęby ścierpnęły;
“Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti, “Makolo adya mphesa zosapsa, koma mano a ana ndiye achita dziru.
30 Owszem, raczej rzeką: każdy dla nieprawości swojej umrze; każdego człowieka, któryby jadł grona cierpkie, ścierpną zęby jego.
Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
31 Oto dni idą, mówi Pan, których uczynię z domem Izraelskim i z domem Judzkim przymierze nowe;
“Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
32 Nie takie przymierze, jakiem uczynił z ojcami ich w on dzień, któregom ich ujął za rękę ich, abym ich przywiódł z ziemi Egipskiej; albowiem oni przymierze moje wzruszyli, chociażem Ja był małżonkiem ich, mówi Pan.
Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto; chifukwa anaphwanya pangano langa, ngakhale ndinali mwamuna wawo,” akutero Yehova.
33 Ale to jest przymierze, które postanowię z domem Izraelskim po tych dniach, mówi Pan: Dam zakon mój do wnętrzności ich, a na sercu ich napiszę go, i będę Bogiem ich, a oni będą ludem moim.
“Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.
34 I nie będzie więcej uczył żaden bliźniego swego, i żaden brata swego, mówiąc: Poznajcie Pana; bo mię oni wszyscy poznają, od najmniejszego z nich aż do największego z nich, mówi Pan; bo miłościw będę nieprawościom ich, a grzechów ich nie wspomnę więcej.
Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake, kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’ chifukwa onse adzandidziwa Ine, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,” akutero Yehova. “Ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
35 Tak mówi Pan, który daje słońce na światłość we dnie, postanowienie miesiąca i gwiazd na światłość w nocy; który rozdziela morze, a huczą nawałności jego; Pan zastępów imię jego.
Yehova akuti, Iye amene amakhazikitsa dzuwa kuti liziwala masana, amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku, amene amavundula nyanja kuti mafunde akokome, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
36 Jeźli odstąpią te ustawy od oblicza mego, mówi Pan, tedyć i nasienie Izraelskie przestanie być narodem przed obliczem mojem po wszystkie dni.
Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
37 Tak mówi Pan: Jeźli mogą być rozmierzone niebiosa z góry, a doścignione grunty ziemi na dole, tedyć i Ja cale odrzucę nasienie Izraelskie dla tego wszystkiego, co uczynili, mówi Pan.
Yehova akuti, “Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo. Ngati patapezeka munthu amene angathe kupima zakuthambo nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”
38 Oto idą dni (mówi Pan, ) których będzie zbudowane to miasto Panu od wieży Chananeel aż do bramy narożnej;
“Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
39 A pójdzie jeszcze sznur pomiaru na przeciwko niej ku pagórkowi Gareb, a uda się ku Goa.
Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
40 I wszystka dolina trupów i popiołu, i to wszystko pole aż do potoku Cedron, aż do węgła bramy końskiej wschodniej, poświęcone będą Panu; nie będzie wykorzenione ani zepsute więcej na wieki.
Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”

< Jeremiasza 31 >