< Jeremiasza 3 >

1 Pan mówi: Opuściłliby mąż żonę swoję, a ona odszedłszy od niego szłaby za innego męża, izali się więcej do niej wróci? Izaliby nie była wielce splugawiona ona ziemia? Ale ty, chociażeś nierząd płodziła z wielą zalotników, wszakże nawróć się d o mnie, mówi Pan.
“Ngati munthu asudzula mkazi wake ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina, kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo? Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri? Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri. Komabe bwerera kwa ine,” akutero Yehova.
2 Podnieś oczu swych na miejsca wysokie, a obacz, jeźliś gdzie nierządu nie płodziła. Na drogach siadałaś kwoli nim, jako Arabczyk na puszczy, a splugawiłaś ziemię wszeteczeństwem twem, i złością twoją.
“Tayangʼana ku zitunda zowuma. Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama? Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu. Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu ndi ntchito zanu zoyipa.
3 A chociaż zawściągnione są dżdże jesienne, a deszczu na wiosnę nie bywało, przecieżeś czoło niewiasty wszetecznej mając, nie chciałaś się wstydzić.
Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula, ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe. Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere; ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.
4 Azaż od tego czasu wołać będziesz na mnie: Ojcze mój! Tyś wodzem młodości mojej?
Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,
5 Izali Bóg zatrzyma gniew na wieczność? Izali go zachowa na wieki? Oto mówisz i czynisz złe, ile możesz.
kodi mudzandikwiyira nthawi zonse? Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’ Umu ndimo mmene umayankhulira, koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”
6 Tedy Pan rzekł do mnie za dni Jozyjasza króla: Widziałżeś, co uczyniła odporna córka Izraelska? jako chodziła na każdą górę wysoką, i pod każde drzewo zielone, i tam nierząd płodziła.
Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko.
7 A chociażem rzekł, gdy to wszystko uczyniła: Nawróć się do mnie! przecie się nie nawróciła; a na to patrzyła przestępnica siostra jej, córka Judzka.
Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi.
8 A tak zdało mi się dla tych wszystkich przyczyn, ponieważ nierząd płodziła uporna córka Izraelska, opuścić ją, i dać jej list rozwodny; a przecież się nie ulękła przestępnica siostra jej, córka Judzka, ale szedłszy i sama nierząd płodziła.
Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo.
9 I stało się, że haniebnym nierządem swoim splugawiła ziemię; bo cudzołożyła z kamieniem i z drewnem.
Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo.
10 A wszakże w tem wszystkiem nie nawróciła się do mnie przestępnica siostra jej, córka Judzka, z wszystkiego serca swego; ale obłudnie, mówi Pan.
Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.
11 Przetoż rzekł Pan do mnie: Usprawiedliwiła duszę swą odporna córka Izraelska więcej, niżeli przestępnica Judzka.
Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda.
12 Idźże, a wołaj temi słowy ku północy a mów: Nawróć się, odporna córko Izraelska! mówi Pan, a nie obórzy się twarz moja surowa na was, bom Ja dobrotliwy, mówi Pan, a nie chowam gniewu na wieki.
Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti, “‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale, pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.
13 Tylko uznaj nieprawość twoję, żeś od Pana, Boga swego, odstąpiła, a tam i sam biegała drogami swemi do obcych bogów pod każde drzewo zielone, a głosu mojego nie słuchaliście, mówi Pan.
Ungovomera kulakwa kwako kuti unawukira Yehova Mulungu wako. Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo pansi pa mtengo uliwonse wogudira, ndiponso kuti sunandimvere,’” akutero Yehova.
14 Nawróćcież się, synowie uporni! mówi Pan; bom Ja jest małżonkiem waszym, a przyjmę was jednego z miasta, a dwóch z rodzaju, abym was wprowadził do Syonu,
“Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse.
15 Gdzie wam dam pasterzy według serca mego, i będą was paść umiejętnie i rozumnie.
Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha.
16 I stanie się, gdy się rozmnożycie a rozrodzicie się w tej ziemi w oneż dni, mówi Pan, nie będą więcej mówić: "Skrzynia przymierza Pańskiego", ani wstąpi na serce, ani wspomną na nią, ani jej nawiedzać, ani jej więcej poważać będą.
Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,” akutero Yehova.
17 Czasu onego nazwane będzie Jeruzalem stolicą Pańską, a zgromadzą się do niego wszystkie narody, do imienia Pańskiego, do Jeruzalemu, i nie będą więcej chodzić za uporem serca swego złośliwego.
Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa.
18 W one dni pójdą dom Judzki z domem Izraelskim, i przyjdą pospołu z ziemi północnej do ziemi, którąm dał w dziedzictwo ojcom waszym.
Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.
19 Chociażem Ja rzekł: Jakożbym cię położył między synami, a dał ci ziemię pożądaną, dziedzictwo zacne zastępów pogańskich? chyba żebyś mię wzywał, mówiąc: Ojcze mój! a od naśladowania mnie nie odwrócił się.
“Ine mwini ndinati, “‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga ndikukupatsani dziko labwino kwambiri, cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’ Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’ ndi kuti simudzaleka kunditsata.
20 Ponieważ jako żona przeniewierza się mężowi swemu, takeście mi się przeniewierzyli, o domie Izraelski! mówi Pan.
Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake, momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,” akutero Yehova.
21 Głos na wysokich miejscach niech będzie słyszany, płacz modlitw synów Izraelskich; bo przewrotne uczyniwszy drogi swe zapamiętali na Pana, Boga swego,
Mawu akumveka pa magomo, Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo chifukwa anatsata njira zoyipa ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.
22 Mówiącego: Nawróćcie się, synowie odporni! a uleczę odwrócenia wasze; mówcie: Oto my idziemy do ciebie, boś ty jest Pan, Bóg nasz.
Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika; ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.” “Inde, tidzabwerera kwa Inu pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
23 Zaiste próżna jest nadzieja w pagórkach i w mnóstwie gór; zaiste w Panu, Bogu naszym, jest zbawienie Izraelskie.
Ndithu kupembedza pa magomo komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu. Zoonadi chipulumutso cha Israeli chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
24 Bo ta hańba pożarła pracę ojców naszych od młodości naszej, trzody ich, i stada ich, syny ich, i córki ich.
Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu la ntchito za makolo athu, nkhosa ndi ngʼombe zawo, ana awo aamuna ndi aakazi.
25 Leżymy w pohańbieniu swem, a przykrywa nas zelżywość nasza; albowiemśmy przeciwko Panu, Bogu naszemu, zgrzeszyli, my i ojcowie nasi, od młodości naszej aż do dnia tego, a nie usłuchaliśmu głosu Pana, Boga naszego.
Tilekeni tigone pansi mwa manyazi, ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe. Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu, ife pamodzi ndi makolo athu kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”

< Jeremiasza 3 >