< Jeremiasza 29 >

1 A teć są słowa listu, który posłał Jeremijasz prorok z Jeruzalemu do ostatków starszych, którzy byli w pojmaniu, i do kapłanów, i do proroków, i do wszystkiego ludu, których był przeniósł Nabuchodonozor z Jeruzalemu do Babilonu,
Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
2 Gdy wyszedł Jechonijasz król i królowa, i komornicy, książęta Judzcy, i Jeruzalemscy, także cieśle i kowale z Jeruzalemu;
Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
3 Przez Elhasa, syna Safanowego, i Giemaryjasza, syna Helkijaszowego, (których był posłał Sedekijasz, król Judzki, do Nabuchodonozora, króla Babilońskiego, do Babilonu) mówiąc:
Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
4 Tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski, do wszystkich pojmanych, którychem przeniósł z Jeruzalemu do Babilonu:
Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
5 Budujcie domy, i osadzajcie się; szczepcie też sady, a jedzcie owoc ich;
“Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
6 Pojmujcie żony, a płodźcie synów i córki, i dawajcie synom waszym żony, a córki wasze wydawajcie za mąż, aby rodziły synów i córki; rozmnażajcie się tam, i niech was nie ubywa.
Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
7 Szukajcie też pokoju miastu temu, do któregom was przeniósł, a módlcie się za nie Panu; bo w pokoju jego będziecie mieli pokój.
Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
8 Tak zaiste mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Niech was nie zwodzą prorocy wasi, którzy są między wami, i wieszczkowie wasi, a nie sprawujcie się snami waszemi, które się wam śnią.
Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
9 Bo wam oni kłamliwie prorokują w imieniu mojem; nie posłałem ich, mówi Pan.
Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
10 Tak zaiste mówi Pan: Jako się jedno wypełnią siedmdziesiąt lat Babilonowi, nawiedzę was, a potwierdzę wam słowa swego wybornego o przywróceniu was na to miejsce.
Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
11 Bo Ja najlepiej wiem myśli, które myślę o was, mówi Pan: myśli o pokoju, a nie o utrapieniu, abym uczynił koniec pożądany biedom waszym.
Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
12 Gdy mię wzywać będziecie, a pójdziecie, i modlić mi się będziecie, tedy was wysłucham;
Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
13 A szukając mię, znajdziecie; gdy mię szukać będziecie ze wszystkiego serca swego,
Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
14 Dam się wam zaiste znaleść, mówi Pan: a przywrócę więźniów waszych, i zgromadzę was ze wszystkich narodów, i ze wszystkich miejsc, gdziemkolwiek was zagnał, mówi Pan; i przyprowadzę was na to miejsce, skądem was wyprowadził.
mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
15 Gdy rzeczecie: Wzbudzał nam Pan proroków prorokujących o zaprowadzeniu do Babilonu.
Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
16 Bo tak mówi Pan o królu, który siedzi na stolicy Dawidowej, i o wszystkim ludu, który mieszka w tem mieście, braciach waszych, którzy nie wyszli z wami w tę niewolę;
koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
17 Tak mówi Pan zastępów: Oto Ja poślę na nich miecz, głód, i mór, a uczynię ich jako złe figi, których nie jadają, przeto, że są złe.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
18 Albowiem prześladować ich będę mieczem, głodem i morem, i dam ich na potłukanie po wszystkich królestwach ziemi, na przeklęstwo, i na zdumienie, owszem, na poświstanie, i na urąganie między wszystkimi narodami, tam, gdzie ich zapędzę,
Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
19 Przeto, iż nie słuchają słów moich, mówi Pan, gdy posyłam do nich sług swoich, proroków, rano wstawając i posyłając; a nie słuchaliście, mówi Pan.
Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
20 Przetoż słuchajcie słowa Pańskiego wy wszyscy pojmani, którychem wysłał z Jeruzalemu do Babilonu.
Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
21 Tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski, o Achabie, synu Kolajaszowym, i o Sedekijaszu, synu Maazejaszowym, którzy wam prorokują w imieniu mojem kłamstwo: Oto Ja podam ich w rękę Nabuchodonozora, króla Babilońskiego, aby ich pobił przed oczyma wasze mi.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
22 I będzie wzięte z nich przeklinanie między wszystkich pojmanych z Judy, którzy są w Babilonie, aby mówili: Niech cię uczyni Pan jako Sedekijasza, i jako Achaba, których upiekł król Babiloński na ogniu,
Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
23 Przeto, że popełniali złość w Izraelu, cudzołożąc z żonami bliźnich swoich, a kłamliwie mówiąc słowo w imieniu mojem, czegom im nie przykazał; a Ja o tem wiem, i jestem tego świadkiem, mówi Pan.
Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
24 A do Semejasza Nechalamity rzecz, mówiąc:
Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
25 Tak powiada Pan zastępów, Bóg Izraelski, mówiąc: Przeto żeś ty posłał imieniem swojem listy do wszystkiego ludu, który jest w Jeruzalemie, i do Sofonijasza, syna Maazejaszowego, kapłana, i do wszystkich kapłanów, mówiąc:
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
26 Pan cię dał za kapłana miasto Jojady kapłana, abyście mieli dozór w domu Pańskim na każdego męża w rozum zaszłego a prorokującego, abyś dał takowego do więzienia i do kłody.
‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
27 Przeczżeś tedy teraz nie zgromił Jeremijasza Anatotczyka, który wam prorokuje?
Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
28 Bo posłał do nas do Babilonu, mówiąc: Jeszczeć długo czekać; budujcie domy, a osadzajcie się, szczepcie sady, a jedzcie owoce ich.
Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
29 Bo Sofonijasz kapłan czytał ten list przed Jeremijaszem prorokiem.
Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
30 I stało się słowo Pańsie do Jeremijasza mówiąc:
Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
31 Poślij do wszystkich zabranych w niewolę, mówiąc: Tak mówi Pan o Semejaszu Nechalamitczyku: Przeto, że wam prorokował Semejasz, chociażem go Ja nie posłał, a przywodzi was do tego, abyście mieli nad zieję w kłamstwie;
“Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
32 Przetoż tak mówi Pan: Oto Ja nawiedzę Semejasza Nechalamitczyka i nasienie jego; nie będzie miał nikogo, ktoby mieszkał w pośrodku ludu tego, ani ogląda tego dobra, które Ja uczynię ludowi swemu, mówi Pan; bo radził, aby odstąpił lud od Pana.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.

< Jeremiasza 29 >