< Jeremiasza 26 >

1 Na początku królowania Joakima, syna Jozyjasza, króla Judzkiego, stało się to słowo od Pana, mówiąc:
Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Tak mówi Pan: Stań w sieni domu Pańskiego, a mów do wszystkich miast Judzkich, do przychodzących kłaniać się w domu Pańskim, wszystkie słowa, któreć rozkazuję mówić do nich; nie ujmuj i słowa.
“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
3 Owa snać usłuchają, a nawrócą się każdy od złej drogi swej, abym pożałował złego, którem im umyślił uczynić dla złości spraw ich.
Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
4 I rzecz do nich: Tak mówi Pan: Jeźli mię nie usłuchacie, żebyście chodzili w zakonie moim, którym wam przedłożył.
Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
5 Słuchając słów sług moich proroków, których Ja posyłam do was, jakoście, gdym ich rano wstawając posyłał, nie usłuchali:
ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
6 Tedy uczynię temu domowi jako Sylo, a to miasto dam na przeklęstwo wszystkim narodom ziemi.
ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
7 A kapłani i prorocy i wszystek lud słyszeli Jeremijasza mówiącego te słowa w domu Pańskim.
Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
8 A skoro przestał Jeremijasz mówić wszystko, co mu był rozkazał Pan mówić wszystkiemu ludowi, pojmali go oni kapłani i prorocy, i wszystek on lud mówiąc: Śmiercią umrzesz.
Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
9 Czemuś prorokował w imię Pańskie, mówiąc: Stanie się temu domowi jako Sylo, a to miasto tak spustoszeje, że w niem nie będzie obywatela? I zgromadzał się wszystek lud przeciwko Jeremijaszowi do domu Pańskiego.
Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
10 Tedy usłyszawszy te rzeczy książęta Judzcy, przyszli z domu królewskiego do domu Pańskiego, i usiedli w wejściu nowej bramy Pańskiej.
Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
11 I rzekli kapłani i prorocy do onych książąt, i do wszystkiego ludu, mówiąc: Ten mąż godzien jest śmierci; bo prorokował przeciwko miastu temu, jakoście to słyszeli w uszy swoje.
Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
12 Tedy rzekł Jeremijasz do wszystkich książąt, i do wszystkiego ludu, mówiąc: Pan mię posłał, abym prorokował o tym domu i o tem mieście wszystko to, coście słyszeli.
Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
13 Przetoż teraz poprawcie drogi swoje i sprawy swe, a usłuchajcie głosu Pana, Boga swego, a pożałuje Pan tego złego, które wyrzekł przeciwko wam.
Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
14 A ja otom jest w rękach waszych; czyńcie zemną, co dobrego i sprawiedliwego jest w oczach waszych.
Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
15 A wszakże zapewne wiedzcie, jeźliż mię zabijecie, że krew niewinną zwalicie na się i na to miasto, i na obywateli jego; bo mię zaprawdę Pan do was posłał, abym mówił te wszystkie słowa w uszy wasze.
Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
16 I rzekli książęta i wszystek lud do kapłanów i do onych proroków: Niema być żadnym sposobem ten mąż osądzony na śmierć, ponieważ w imieniu Pana, Boga naszego, mówił do nas.
Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
17 Tedy powstali niektórzy z starszych onej ziemi, i uczynili rzecz do wszystkiego zgromadzenia ludu, mówiąc:
Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
18 Micheasz Morastytczyk prorokował za dni Ezechijasza, króla Judzkiego, i rzekł do wszystkiego ludu Judzkiego, mówiąc: Tak mówi Pan zastępów: Syon jako pole poorany będzie, a Jeruzalem jako gromady rumu będzie, a góra domu tego jako wysokie lasy.
“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
19 Izali go zaraz dlatego zabili Ezechijasz, król Judzki, i wszystek Juda? izali się nie ulękł Pana, a nie modlił się Panu? I żałował Pan onego złego, które był wyrzekł przeciwko nim: przetoż my złą rzecz czynimy przeciwko duszom naszym.
Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
20 Także też był mąż prorokujący w imieniu Pańskiem, Uryjasz, syn Semejaszowy, z Karyjatyjarym, który prorokował o tem mieście i o tej ziemi według wszystkich słów Jeremijaszowych.
(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
21 A gdy usłyszał król Joakim, i wszystko rycerstwo jego, i wszyscy książęta słowa jego, zaraz go chciał król zabić, co usłyszawszy Uryjasz uląkł się, a uciekłszy przyszedł do Egiptu.
Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
22 Ale król Joakim posłał niektórych do Egiptu, Elnatana, syna Achborowego, i innych z nim do Egiptu;
Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
23 Którzy wywiódłszy Uryjasza z Egiptu, przywiedli go do króla Joakima; i zabił go mieczem, i wrzucił trupa jego do grobów ludu pospolitego.
Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
24 Wszakże ręka Achikama, syna Safanowego, była przy Jeremijaszu, aby nie był wydan w ręce ludu, i nie był zabity.
Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.

< Jeremiasza 26 >