< Jeremiasza 25 >

1 Słowo, które się stało do Jeremijasza przeciwko wszystkiemu ludowi Judzkiemu roku czwartego Joakima, syna Jozyjaszowego, króla Judzkiego, (który jest rok pierwszy Nabuchodonozora, króla Babilońskiego; )
Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
2 Które mówił Jeremijasz prorok do wszystkiego ludu Judzkiego, i do wszystkich obywateli Jeruzalemskich mówiąc;
Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
3 Od trzynastego roku Jozyjasza, syna Amonowego, króla Judzkiego, aż do dnia tego, już to przez dwadzieścia i trzy lata bywało słowo Pańskie do mnie, którem do was mawiał, rano wstawając i opowiadając; aleście nie słuchali.
Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
4 Posyłał też Pan do was wszystkich sług swoich proroków, rano wstawając, i posyłając, (którycheście nie usłuchali, aniście nakłonili ucha swego, abyście słyszeli; )
Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
5 Którzy mówili: Nawróćcie się teraz każdy od złej drogi swojej, i od złości spraw waszych; a tak będziecie mieszkali w tej ziemi, którą wam dał Pan, i ojcom waszym od wieku aż na wieki.
Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
6 A nie chodźcie za bogami cudzymi, abyście im służyli, i kłaniali się im, ani mię gniewajcie sprawą rąk waszych, a Ja wam źle nie uczynię.
Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
7 Aleście mię nie usłuchali, mówi Pan, abyście mię pobudzali do gniewu sprawą rąk swioch na swe złe.
“Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
8 Przetoż tak mówi Pan zastępów: Dlatego, iżeście nie usłuchali słów moich,
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
9 Oto Ja poślę i pobiorę wszystkie narody północne, mówi Pan, i do Nabuchodonozora króla Babilońskiego, sługi mego, i przywiodę je na tę ziemię, i na obywateli jej, i na te wszystkie narody okoliczne, które do szczętu wygładzę, i położę je na podziw, i na poświstanie, i na spustoszenie wieczne.
ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
10 I sprawię to, aby im zginął głos wesela, i głos radości, głos oblubieńca, i głos oblubienicy, głos żarn, i światłość pochodni,
Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
11 I będzie ta wszystka ziemia spustoszeniem, i zdumieniem, a służyć będą te narody królowi Babilońskiemu siedmdziesiąt lat.
Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
12 Ale potem, gdy się wypełni siedmdzisiśąt lat, nawiedzę na królu Babilońskim i na tym narodzie, mówi Pan, nieprawość ich, i na ziemi Chaldejskiej, tak, że ją obrócę w pustynie wieczne.
“Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
13 A przywiodę na tę ziemię wszystkie słowa moje, którem mówił o niej, mianowicie to wszystko, co napisano w tych księgach, cokolwiek prorokował Jaremijasz o wszystkich narodach.
Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
14 Gdyż w niewolę podbici będą od narodów, także jako i oni możnych, i od królów wielkich, tedy im oddam według spraw ich i według uczynków rąk ich.
Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
15 Bo tak rzekł Pan, Bóg Izraelski, do mnie: Weźmij kubek wina tej popędliwości z ręki mojej, a napawaj nim wszystkie narody, do których Ja ciebie poślę;
Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
16 Aby pili i potaczli się, owszem, aby szaleli od ostrza miecza, który Ja poślę między nich.
Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
17 Wziąłem tedy kubek z ręki Pańskiej, i napoiłem wszystkie one narody, do których mię Pan posłał:
Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
18 Jeruzalem, i miasta ziemi Judzkiej, i królów jej, i książąt jej, abym ich podał na spustoszenie, na zdumienie, na poświstanie, i na przeklęstwo, jako się to dziś okazuje.
Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
19 Faraona też, króla Egipskiego, i sług jego, i książąt jego, i wszystek lud jego;
Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
20 I to wszystko pospólstwo, także wszystkich króli ziemi Uz, i wszystkich króli ziemi Filistyńskiej, i Aszkalon, i Gazę, i Akkaron, i ostatek Azotu;
ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
21 Edomczyków, i Moabczyków, i synów Ammonowych;
Edomu, Mowabu ndi Amoni.
22 I wszystkich królów Tyrskich, i wszystkich królów Sydońskich, i królów tej krainy, która jest przy morzu;
Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
23 Dedana i Temę, i Buzę, i wszystkich, którzy mieszkają w ostatnich kątach:
ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
24 I wszystkich królów Arabskich, i wszystkich królów tego pospólstwa, które mieszka na puszczy;
Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
25 Także wszystkich królów Zymry i wszystkich królów Elam, i wszystkich królów Medskich;
Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
26 Owszem, wszystkich królów północnych, bliskich i dalekich, jednego jako drugiego; wszystkie też królestwa ziemi, którekolwiek są na obliczu ziemi; a król Sesak będzie pił po nich.
ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
27 I rzecz do nich: Tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Pijcie, a popijcie się, owszem zwracajcie, i padajcie tak, abyście nie powstali dla miecza, który Ja poślę między was.
“Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
28 A jeźliby nie chcieli wziąć kubka z ręki twojej, aby pili, tedy rzeczesz do nich: Tak mówi Pan zastępów: Koniecznie pić musicie.
Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
29 Bo ponieważ na to miasto, które nazwane jest od imienia mego, Ja zaczynam przywodzić złe rzecz, a wybyście bez karania być mieli? Nie będziecie bez karania; bom Ja miecz przyzwał na wszystkich obywateli tej ziemi, mówi Pan zastępów.
Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
30 Przetoż ty prorokuj przeciwko nim te wszyskie słowa, a mów do nich: Pan z wysoka zaryczy, a mieszkania świętobliwości swojej wyda głos swój, rycząc zaryczy z mieszkania swego; krzyk pobudzających się jako tłoczących prasę, rozlegać się będzie prze ciwko wszystkim obywatelom tej ziemi.
“Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
31 I przejdzie huk aż do kończyn ziemi; bo się Pan rozpiera z tymi narodami, w sąd sam wchodzi ze wszelkiem ciałem, niezbożnych poda pod miecz, mówi Pan.
Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
32 Tak mówi Pan zastępów: Oto udręczenie pójdzie z narodu do narodu, a wicher wielki powstanie od kończyn ziemi;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
33 I będą pobici od Pana czasu onego od końca ziemi aż do końca ziemi; nie będą ich płakać, ani zbierać, ani chować; będą jako gnój na polu.
Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
34 Narzekajcie pasterze i wołajcie, a walajcie się w popiele, wy najzacniejsi tej trzody! bo się wypełniły dni wasze, zabicia i rozproszenia waszego, i upadniecie jako naczynie drogie.
Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
35 I zginie ucieczka pasterzom, a ujście najzacniejszym tej trzody.
Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
36 Głos wołania pasterzy, i narzekanie najzacniejszych tej trzody słychać będzie; bo Pan spustoszy pastwiska ich.
Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
37 I zagubione będą spokojne pastwiska dla zapalczywości gniewu Pańskiego,
Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
38 Który opuści jako lew jaskinię swoję; bo ziemia ich przyjdzie na spustoszenie dla zapalczywości pustoszyciela, i dla popędliwości gniewu jego.
Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.

< Jeremiasza 25 >