< Jeremiasza 17 >

1 Grzech Judzki napisany jest piórem żelaznem, a ostrym dyjamentem wyryty jest na tablicy serca ich, i na rogach ołtarzów waszych;
“Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
2 Gdy wspominają synowie ich na ołtarze ich, i na gaje ich pod drzewem zielonem, na pagórkach wysokich.
Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
3 O góro, i pole moje! majętność twoję i wszystkie skarby twoje podam na rozszarpanie dla grzechu wyżyn twoich, które masz po wszystkich granicach twoich.
Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
4 A ty musisz zaniechać za przewinieniem twojem dziedzictwa twego, którem ci dał. I dam cię w niewolę nieprzyjaciołom twoim, i ziemi, której nie znasz; boście ogień rozniecili w popędliwości mojej, który aż na wieki gorzeć będzie.
Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
5 Tak mówi Pan: Przeklęty mąż, który ufa w człowieku, i który pokłada ciało ramieniem swojem, a od Pana odstępuje serce jego.
Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
6 Albowiem stanie się jako wrzos na puszczy, który nie czuje, gdy co dobrego przychodzi, ale bywa na suchych miejscach na puszczy w ziemi słonej, i w której nikt nie mieszka.
Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
7 Błogosławiony mąż, który ufa w Panu, a Pan jest nadzieją jego.
“Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
8 Bo będzie jako drzewo wszczepione nad wodami, a nad strumieniem zapuszczające korzenie swoje, które nie czuje, gdy przychodzi gorącość, ale liść jego zostaje zielony, a roku suchego nie frasuje się, i nie przestaje przynosić owocu.
Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
9 Najzdradliwsze jest serce nadewszystko i najprzewrotniejsze, któż je pozna?
Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
10 Ja Pan, który się badam serca, i doświadczam nerek, tak abym każdemu oddał według drogi jego, i według owocu spraw jego.
“Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
11 Jako kuropatwa zgromadza jajka, ale ich nie wylęga: tak, kto zbiera bogactwa, a niesprawiedliwie, w połowie dni swoich opuści je, a na ostatek będzie głupim;
Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
12 Ale miejsce świątnicy naszej, to jest stolica chwały Najwyższego, wiecznie trwa.
Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
13 O nadziejo Izraelska, Panie! wszyscy, którzy cię opuszczają, niech będą zawstydzeni; którzy odstępują odemnie, niech na ziemi zapisani będą; albowiem opuścili źródło wód żywych, Pana.
Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
14 Uzdrów mię, Panie! a będę uzdrowiony: zbaw mię, a będę zbawiony; albowiemeś ty chwała moja.
Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
15 Oto oni do mnie mówią: Gdzież jest to słowo Pańskie? Niechże już przyjdzie;
Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
16 Chociażem Ja tego nie zabiegał, abym był pasterzem twoim, anim dnia boleści pragnął, ty wiesz, cokolwiek wyszło z ust moich, przed obliczem twojem jest.
Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
17 Nie bądźże mi na postrach; tyś nadzieja moja w dzień utrapienia.
Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
18 Niech będą pochańbieni, którzy mię prześladują, a ja niech nie będę zawstydzony; niech się oni lękają, a ja niech się nie lękam; przywiedź na nich dzień utrapienia, a dwojakiem skruszeniem skrusz ich.
Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
19 Tak Pan rzekł do mnie: Idź, a stań w bramie synów ludu tego, którą wchodzą królowie Judzcy, i którą wychodzą, i we wszystkich bramach Jeruzalemskich,
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
20 I rzecz do nich: Słuchajcie słowa Pańskiego, królowie Judzcy, i wszystek Judo, i wszyscy obywatele Jeruzalemscy, którzy chadzacie temi bramami!
Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
21 Tak mówi Pan: Strzeżcie pilnie dusz waszych, a nie noście brzemion żadnych w dzień sabatu, ani ich wnoście bramami Jeruzalemskiemi;
Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
22 Ani wynaszajcie brzemion z domów waszych w dzień sabatu, ani żadnej roboty odprawujcie, ale święćcie dzień sabatu, jakom rozkazał ojcom waszym.
Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
23 Wszakże nie usłuchali, ani nakłonili ucha swego, owszem, zatwardzili kark swój, nie słuchając ani przyjmując nauki.
Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
24 A jeźli mię pilnie słuchać będziecie, mówi Pan, tak, żebyście nie wnosili brzemion bramami miasta tego w dzień sabatu, ale święcili dzień sabatu, nie odprawując weń żadnej roboty;
Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
25 Tedy wchodzić będą bramami miasta tego królowie i książęta siedzący na stolicy Dawidowej, jeżdżąc na wozach i na koniach, oni i książęta ich, mężowie Judzcy i obywatele Jeruzalemscy, i stać będzie to miasto aż na wieki.
Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
26 I zbieżą się z miast Judzkich i z okolicznych miejsc Jeruzalemskich, i z ziemi Benjaminowej, i z równin, i z tej góry, i od południa, przynosząc całopalenie, i ofiarę, i dar, i kadzidło, także i dziękczynienie niosąc do domu Pańskiego.
Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
27 Ale jeźli mię nie usłuchacie, abyście święcili dzień sabatu, a nie nosili brzemion, wchodząc bramami Jeruzalemskiemi w dzień sabatu, tedy rozniecę ogień w bramach jego, który pożre pałace Jeruzalemskie, a nie będzie ugaszony.
Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”

< Jeremiasza 17 >