< Jeremiasza 13 >

1 Tak rzekł Pan do mnie: Idź, a kup sobie pas lniany, a opasz nim biodra swoje; ale do wody nie kładź go.
Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.”
2 Kupiłem tedy pas według rozkazania Pańskiego, i opasałem biodra moje.
Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.
3 Potem stało się słowo Pańskie do mnie powtóre, mówiąc:
Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti,
4 Weźmij ten pas, któryś kupił, który jest na biodrach twoich, a wstawszy idź do Eufratesa, a skryj go tam w dziurę skalną.
“Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.”
5 I szedłem a skryłem go u Eufratesa, jako mi był Pan rozkazał.
Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.
6 A po wyjściu wielu dni rzekł Pan do mnie: Wstań, idź do Eufratesa, a weźmij stamtąd on pas, którym ci tam rozkazał skryć.
Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.”
7 Szedłem tedy do Eufratesa, a wykopawszy wziąłem on pas z miejsca onego, gdziem go był skrył, a oto skażony był on pas, tak, iż się niczemu nie godził.
Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.
8 I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Pamenepo Yehova anandiwuza kuti,
9 Tak mówi Pan: Tak skażę pychę Judzką i wielką pychę Jeruzalemską,
“Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
10 Ludu tego bardzo złego, który się zbrania słuchać słów moich, który chodzi w uporze serca swego, i chodzi za bogami obcymi, służąc im i kłaniając się im; i będzie podobien temu pasowi, który się niczemu nie godzi.
Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu.
11 Bo jako pas przylega do biódr męża, takiem Ja był przypoił do siebie wszystek dom Izraelski, i wszystek dom Judzki, mówi Pan, aby byli ludem moim, a to ku sławie i ku chwale, i ku ozdobie; ale nie byli posłuszni.
Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.
12 Przetoż rzecz im to słowo. Tak mówi Pan, Bóg Izraelski: Wszelkie naczynie winne bywa napełnione winem; a gdy rzeką: Wiemyć to dobrze, że wszelkie naczynie winne bywa napełnione winem,
“Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’
13 Tedy im rzeczesz: Tak mówi Pan: Oto Ja napełnię wszystkich obywateli tej ziemi, i królów, którzy siedzą miasto Dawida na stolicy jego, i kapłanów i proroków, także i wszystkich obywateli Jeruzalemskich pijaństwem;
Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu.
14 I rozrażę jednego o drugiego, jako ojców tak i synów, mówi Pan; nie przepuszczę, nie sfolguję, ani się zmiłuję, abym ich skazić nie miał.
Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’”
15 Słuchajcież, a pojmujcie uszyma, nie podnoście się; boć Pan mówi.
Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu, musadzitukumule, pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.
16 Dajcie Panu, Bogu swemu, chwałę, pierwej niżby ciemności przywiódł, a pierwej niżby się obraziły nogi wasze o góry ciemne; i czekalibyście światłości, ale Bóg obróciłby je w cień śmierci i przemieniłby je w zaćmienie.
Lemekezani Yehova Mulungu wanu asanagwetse mdima, mapazi anu asanayambe kupunthwa mʼchisisira chamʼmapiri. Asanasandutse kuwala mukuyembekezerako kukhala mdima wandiweyani.
17 A jeźliż tego słuchać nie będziecie, w skrytościach płakać będzie dusza moja dla pychy waszej, a płacząc płakać będzie, i wyleje oko moje łzy, bo pojmana będzie trzoda Pańska.
Koma ngati simumvera, ndidzalira kwambiri chifukwa cha kunyada kwanu. Mʼmaso mwanga mwadzaza ndi misozi yowawa chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.
18 Mów królowi i królowej: Upokorzcie się, usiądźcie na ziemi; bo spadła z głowy waszej korona chwały waszej.
Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti, “Tsikani pa mipando yaufumuyo, pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo zagwa pansi.”
19 Miasta na południe zawarte będą, tak, że nie będzie, ktoby je otworzył; przeniesiony będzie wszystek Juda, przeniesiony będzie do szczętu.
Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula. Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo, watengedwa yense ukapolo.
20 Podnieście oczy wasze, a obaczcie tych, którzy idą z północy. Gdzie jest ta trzoda, którejć się zwierzono? gdzie jest stado chwały twojej?
Tukula maso ako kuti uwone amene akubwera kuchokera kumpoto. Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti, nkhosa zanu zokongola zija?
21 Cóż rzeczesz, gdy cię (nieprzyjaciel) nawiedzi? Boś ich ty nauczyła, aby byli nad tobą książętami przednimi; izali cię boleści nie ogarną, jako niewiastę rodzącą?
Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira? Kodi sudzamva zowawa ngati za mayi pa nthawi yake yochira?
22 Mówiszli w sercu swojem: Przeczżeby to przypaść miało na mię? Dla mnóstwa nieprawości twojej odkryte będą podołki twoje, gwałtem obnażone będą pięty twoje.
Ndipo ngati udzadzifunsa kuti, “Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?” Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri kuti zovala zanu zingʼambike ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.
23 Azaż może murzyn odmienić skórę swoję, albo lampart pstrociny swoje? także i wy, azaż będziecie mogli dobrze czynić, nauczywszy się źle czynić?
Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake, kapena kambuku kusintha mawanga ake? Inunso amene munazolowera kuchita zoyipa simungathe kusintha.
24 Przetoż rozproszę ich jako źdźbło, które się rozlatuje od wiatru z pustyni.
“Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.
25 Tenci będzie los twój, i dział odmierzony tobie odemnie, mówi Pan, przeto, żeś mię zapomniała, a ufałaś w kłamstwie.
Limeneli ndiye gawo lanu, chilango chimene ndakukonzerani chifukwa chondiyiwala Ine ndi kutumikira milungu yabodza, akutero Yehova.
26 A tak i Ja odkryję podołek twój aż na twarz twoję, aby się okazała sromota twoja.
Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso kuti umaliseche wanu uwonekere.
27 Widziałem cudzołóstwa twoje i poryzanie twoje, sprosność wszeteczeństwa twego na pagórkach, i na polu; widziałem, mówię, obrzydliwości twoje. Biada tobie, Jeruzalemie! i pókiż się nie oczyścisz? kiedyż to wżdy będzie?
Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu ndi ziwerewere zanu, zochitika pa mapiri ndi mʼminda. Tsoka iwe Yerusalemu! Udzakhala wosayeretsedwa pa zachipembedzo mpaka liti?”

< Jeremiasza 13 >