< Izajasza 8 >

1 I rzekł Pan do mnie: Weźmij sobie księgi wielkie, a napisz na nich pismem człowieczem: Pospiesz się do łupu, pokwap się do korzyści.
Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
2 Tedym wziął sobie za świadków wiernych Uryjasza kapłana, i Zacharyjasza, syna Jeberechyjaszowego.
Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 Wtemem przystąpił do prorokini, która począwszy porodziła syna. I rzekł Pan do mnie: Nazów imię jego: Pospiesz się do łupu, pokwap się do korzyści.
Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
4 Albowiem niżeli będzie umiało to dziecię wołać: Ojcze mój i matko moja, lud króla Assyryjskiego pobierze bogactwa Damaszku, i łupy Samaryi.
Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 Nadto rzekł jeszcze Pan do mnie, mówiąc:
Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 Ponieważ wzgardził lud ten wody Syloe, które cicho płyną, a waseli się z Rasyna, i syna Romelijaszowego:
“Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
7 Przetoż oto Pan przywiedzie na nich wody rzeki gwałtownej i wielkiej, to jest króla Assyryjskiego, i wszystkę sławę jego, tak, że wystąpi ze wszystkich strumieni swoich, a wyleje ze wszystkich brzegów swoich.
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
8 Pociecze i przez ziemię Judzką, wyleje a rozejdzie się, aż do szyi wzbierze; a rozszerzone skrzydła jego napełnią szerokość ziemi twojej, o Immanuelu!
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
9 Zbierajcie się narody, wszakże potłumione będziecie. Przyjmujcie w uszy wszyscy w dalekiej ziemi; przepaszcie się, wszakże potłumieni będziecie; przepaszcie się, wszakże potłumieni będziecie.
Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Wnijdźcie w radę, a będzie rozerwana; namówcie się, a nie ostoi się; bo Bóg z nami.
Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
11 Tak bowiem Pan rzekł do mnie, ująwszy mię za rękę, i dał mi przestrogę, żebym nie chodził drogą ludu tego, mówiąc:
Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 Nie mówcie: Sprzysiężenie. Kiedykolwiek ten lud mówi: Sprzysiężenie, nie strachajcie się jako oni, ani się lękajcie.
“Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
13 Pana zastępów samego poświęcajcie; a on niech będzie bojaźnią waszą, i on strachem waszym.
Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 A będzie wam poświęceniem; ale kamieniem obrażenia i opoką otrącenia obydwom domom Izraelskim, sidłem i siecią obywatelom Jeruzalemskim.
ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 I otrąci się wielu ich o nie, upadną i skruszeni będą, usidlą się a pojmani będą.
Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
16 Zawiąż to świadectwo, zapieczętuj zakon między uczniami moimi.
Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 Tedy będę oczekiwał Pana, który skrył oblicze swoje od domu Jakóbowego, i poczekam go.
Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
18 Oto ja i dzieci, które mi dał Pan, są na znaki i na cuda w Izraelu, od Pana zastępów, który mieszka na górze Syon.
Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
19 A tak jeźliby wam rzekli: Dowiadujcie się od czarowników i od wieszczków, którzy szepcą i markocą, rzeczcie: Izali się nie ma dowiadywać lud u Boga swego? azaż umarłych miasto żywych radzić się ma?
Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
20 Do zakonu raczej i do świadectwa; ale jeźli nie chcą, niechże mówią według słowa tego, w którem niemasz żadnej zorzy.
kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
21 Dlaczego każdy z nich utrapiony i zgłodniały tułaćby się musiał; a będąc zgłodniałym, sam w sobie gniewać się będzie, i złorzeczyć królowi swemu, i Bogu swemu, w górę poglądając.
Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
22 A gdy na ziemię spojrzy, oto ucisk i ciemność, zaćmienie, bieda, i obaczy, że jest wrażony do ciemności.
Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.

< Izajasza 8 >