< Izajasza 7 >

1 I stało się za dni Achaza, syna Joatamowego, syna Uzyjasza, króla Judzkiego, że przyciągnął Rasyn, król Syryjski, i Facejasz, syn Romelijasza, króla Izraelskiego, pod Jeruzalem, aby walczył przeciw niemu: ale go nie mógł dobyć.
Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
2 I oznajmiono domowi Dawidowemu, mówiąc: Zmówiła się Syryja z Efraimem. Tedy się poruszyło serce jego, i serce ludu jego, jako się poruszają drzewa leśne od wiatru.
Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
3 Tedy rzekł Pan do Izajasza: Wyjdź teraz przeciw Achazowi, ty, i Sear Jasub, syn twój, na koniec rur sadzawki wyższej, na drogę pola farbierzowego;
Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
4 A powiedz mu: Patrz, abyś się nie frasował; nie bój się, a serce twoje niechaj się nie lęka tych dwóch ostatków głowien kurzących się, to jest, zapalczywości gniewu Rasyna z Syryjczykami, i syna Romelijaszowego,
Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
5 Przeto, że złą radę uradzili przeciw tobie Syryjczyk, Efraim, i syn Romelijaszowy, mówiąc:
Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
6 Ciągnijmy przeciwko ziemi Judzkiej, a utrapmy ją leżą, i oderwijmy ją do siebie, a postanówmy króla w pośród niej, syna Tabealowego.
‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
7 Tak mówi Pan Panujący: Nie stanie się, i nie będzie to.
Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
8 Albowiem głową Syryi jest Damaszek, a głową Damaszku Rasyn; a po sześćdziesięciu i pięciu latach będzie potarty Efraim, tak, iż więcej ludem nie będzie.
pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
9 Między tem głową Efraimową będzie Samaryja, a głową Samaryi syn Romelijaszowy. Jeźli nie uwierzycie, pewnie się nie ostoicie.
Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
10 Nadto jeszcze rzekł Pan do Achaza, mówiąc:
Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
11 Żądaj sobie znaku od Pana, Boga twego, bądź na dole nisko, bądź wysoko w górze. (Sheol h7585)
“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
12 Tedy odpowiedział Achaz: Nie będę żądał, ani będę kusił Pana.
Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
13 A prorok rzekł: Słuchaj teraz, domie Dawidowy! Małoż się wam zda, uprzykrzać się ludziom, że się uprzykrzacie i Bogu mojemu?
Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
14 Przetoż wam sam Pan znak da. Oto panna pocznie i porodzi syna, a nazwie imię jego Immanuel.
Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
15 Masło i miód jeść będzie, ażby umiał odrzucać złe, a obierać dobre. -
Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
16 Owszem, pierwej niż będzie umiało to dziecię odrzucać złe i obierać dobre, ziemia, którą się ty brzydzisz, opuszczona będzie od dwóch królów swoich.
Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
17 Ale na cię Pan przywiedzie i na lud twój, i na dom ojca twego, dni, jakich nie było ode dnia, którego odstąpił Efraim od Judy, a to przez króla Assyryjskiego.
Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
18 Albowiem stanie się dnia onego, że zaświśnie Pan na muchy, które są na końcu rzek Egipskich, i na pszczoły, które są w ziemi Assyryjskiej.
Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
19 I przyjdą a usiądą wszystkie w dolinach pustych, i w rozpadlinach skalnych, i na wszystkich drzewach urodzajnych.
Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
20 Dnia onego ogoli Pan brzytwą najętą przez tych, którzy są za rzeką, to jest (przez króla Assyryjskiego) głowę, i włosy na nogach, także i brodę wszcząt ogoli.
Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
21 I stanie się dnia onego, że ledwie człowiek żywo krówkę, albo dwie owce zachowa.
Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
22 A wszakże dla obfitości mleka, którego nadoi, będzie jadł masło; masło zaiste i miód będzie jadł, ktokolwiek pozostanie w ziemi.
Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
23 Stanie się też onegoż dnia, iż każde miejsce, gdzie było tysiąc winnych macic za tysiąc srebrników, ostem i cierniem porośnie.
Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
24 Tedy z strzałami i z łukiem tam chodzić będą; bo ostem i cierniem zarośnie wszystka ziemia.
Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
25 Na wszystkie też góry, które motyką kopane być mogą, nie przyjdzie strach ostu i ciernia; ale będą na pastwisko wołom, i na podeptanie owcom.
Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.

< Izajasza 7 >