< Izajasza 61 >

1 Duch Panującego Pana jest nademną; przeto mię pomazał Pan, abym opowiadał Ewangeliję cichym, posłał mię, abym związał rany tych, którzy są skruszonego serca, abym zwiastował pojmanym wyzwolenie, a więźniom otworzenie ciemnicy;
Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
2 Abym ogłosił miłościwy rok Pański, i dzień pomsty Boga naszego; abym cieszył wszystkich płaczących;
Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
3 Abym sprawił radość płaczącym w Syonie, a dał im ozdobę miasto popiołu, olejek wesela miasto smutku, odzienie chwały miasto ściśnionego; i będą nazwani drzewami sprawiedliwości, szczepieniem Pańskiem, abym był uwielbiony.
Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
4 Tedy pobudują spustoszenie starodawne, pustynie stare naprawią, a odnowią miasta spustoszone, puste za wielu narodów.
Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
5 Bo się stawią cudzoziemcy, a paść będą stada wasze, a synowie cudzoziemców oraczami waszymi i winiarzami waszymi będą.
Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
6 Ale wy kapłanami Pańskimi nazwani będziecie, sługami Boga naszego zwać was będą; majętności pogan używać będziecie, a w sławie ich wywyższeni będziecie.
Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
7 Za dwojakie pohańbienie i zelżywość waszę śpiewać będziecie; z działu ich, i w ziemi ich dwojakie dziedzictwo posiądziecie, a tak wesele wieczne mieć będziecie.
Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
8 Ja Pan miłuję sąd, a mam w nienawiści łupiestwo przy całopaleniu; przetoż sprawię, aby uczynki ich działy się w prawdzie, a przymierze wieczne postanowię z nimi.
“Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
9 I znajome będzie między poganami nasienie ich, a potomstwo ich w pośrodku narodów; wszyscy, którzy ich ujrzą, poznają ich, że są nasieniem, któremu Pan pobłogosławił.
Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
10 Weseląc weselić się będą w Panu, a dusza moja rozraduje się w Bogu moim; bo mię oblókł w szaty zbawienia, a płaszczem sprawiedliwości przyodział mię, jako oblubieńca ozdobnego chwałą, i jako oblubienicę ozdobioną w klejnoty swoje.
Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
11 Bo jako ziemia wydaje płód swój, a jako ogród nasienie swoje wywodzi, tak panujący Pan wywiedzie sprawiedliwość i chwałę swoję przed wszystkie narody.
Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.

< Izajasza 61 >