< Izajasza 60 >

1 Powstań, objaśnij się! ponieważ przyszła światłość twoja, a chwała Pańska weszła nad tobą.
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Bo oto ciemności okryją ziemię, a zaćmienie narody; ale nad tobą wejdzie Pan, a chwała jego nad tobą widziana będzie.
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 I będą chodzić narody w światłości twojej, a królowie w jasności, która wejdzie nad tobą.
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 Podnieś w około oczy twe, a spojrzyj; ci wszyscy, którzy się zgromadzili, pójdą do ciebie; synowie twoi z daleka przyjdą, a córki twoje przy boku twoim chowane będą.
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Tedy oglądasz to, a rozweselisz się; tedy się zdumieje i rozszerzy serce twoje, gdy się obróci ku tobie zgraja morska, a moc narodów przyjdzie do ciebie.
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Obfitość wielbłądów okryje cię, także dromedarze z Madyjan i z Efy. Wszyscy ci przyjdą z Saby, złoto i kadzidło przyniosą, a chwały Pańskie opowiadać będą.
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
7 Wszystkie stada z Kedar zgromadzą się do ciebie; barany z Nebajotu służyć ci będą, a ofiarowane będąc na ołtarzu moim, przyjemne będą; a tak dom majestatu mego ozdobię.
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 I rzeczesz: Którzyż to są, co się jako obłoki zlatują, i jako gołębie do okien swoich?
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Na mięć zaiste wyspy oczekują, i okręty morskie zdawna, aby przywiedli synów twoich z daleka, także srebro swoje z sobą, i złoto swoje imieniowi Pana, Boga twego, i Świętego Izraelskiego; bo cię uwielbi.
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 I pobudują cudzoziemcy mury twoje, a królowie ich służyć ci będą, gdyż w rozgniewaniu mojem uderzę cię, a w upodobaniu mojem zlituję się nad tobą.
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 I będą otworzone bramy twoje ustawicznie; we dnie i w nocy nie będą zatkane, aby przywiedziono do ciebie moc pogan, i królowie ich aby byli przywiedzieni.
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Naród ten i królestwo, którećby nie służyło, zginie; narody takie, mówię, do szczętu spustoszone będą.
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
13 Sława Libanu do ciebie przyjdzie, jedlina, sosna, także bukszpan, dla ozdoby miejsca świątnicy mojej, abym miejsce nóg moich uwielbił.
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Przyjdą także do ciebie w pokorze synowie tych, którzy cię trapili, i będą się kłaniać stopom nóg twoich, którzykolwiek pogardzili tobą, i nazwią cię miastem Pańskiem, Syonem Świętego Izraelskiego.
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 Miasto tego, coś opuszczona i w nienawiści była, tak, że nie było, ktoby przez cię chodził, wystawię cię za dostojność wieczną, i wesele od narodu do narodu.
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
16 Bo ssać będziesz mleko narodów, i piersiami królów karmiona będziesz; i poznasz, iżem Ja Pan, zbawieciel twój i odkupiciel twój, mocarz Jakóbowy;
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Miasto miedzi naniosę złota, a miasto żelaza naniosę srebra, a miasto drew miedzi, a miasto kamienia żelaza; i postawię nad tobą dozorców spokojnych, i urzędników sprawiedliwych.
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Nie będzie więcej słychać o drapiestwie w ziemi twojej, o zburzeniu i spustoszeniu na granicach twoich; ale ogłaszać będziesz zbawienie na murach twoich, a chwałę w bramach twoich.
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
19 Nie będziesz miał więcej słońca za światłość dzienną, a jasność miesiąca nie oświeci cię, ale Pan będzie światłością twoją wieczną, a Bóg twój sławą twoją.
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Nie zajdzie więcej słońce twoje, a miesiąc twój nie skryje się; bo Pan będzie wieczną światłością twoją; a tak dokonają się dni smutku twego.
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Lud także twój, którzybykolwiek byli sprawiedliwi, na wieki odziedziczą ziemię; będą latoroślą szczepienia mego, dziełem rąk moich, abym w niem był uwielbiony.
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Najmniejszy rozmnoży się na tysiące, a maluczki poczet w naród niezliczony. Ja Pan czasu swego prędko to uczynię.
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

< Izajasza 60 >