< Izajasza 6 >

1 Roku, którego umarł król Uzyjasz, widziałem Pana, siedzącego na stolicy wysokiej i wyniosłej, a podołek jego napełniał kościół.
Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
2 Serafinowie stali nad nim, sześć skrzydeł miał każdy z nich; dwoma zakrywał twarz swoję, a dwoma przykrywał nogi swoje, a dwoma latał.
Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira.
3 I wołał jeden do drugiego, mówiąc: Święty, święty, święty, Pan zastępów; pełna jest wszystka ziemia chwały jego.
Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti “Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse. Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”
4 I poruszyły się podwoje u drzwi od głosu wołającego, a dom pełny był dymu.
Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
5 I rzekłem: Biada mnie! jużem zginął, przeto, żem człowiek splugawionych warg, a mieszkam w pośrodku ludu, który ma splugawione wargi; a iż króla, Pana zastępów, widziały oczy moje.
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
6 I przyleciał do mnie jeden z Serafinów, mając w ręce swej węgiel rozpalony, który kleszczykami wziął z ołtarza;
Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe.
7 I dotknął się ust moich, a rzekł: Oto się dotknął ten węgiel warg twoich, a odejdzie nieprawość twoja, a grzech twój zgładzony będzie.
Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
8 Potemem słyszał głos Pana mówiącego: Kogoż poślę? a kto nam pójdzie? Tedym rzekł: Otom ja, poślij mię.
Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?” Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
9 A on rzekł: Idź, a powiedz ludowi temu: Słuchajcie słuchając, a nie rozumijcie, a widząc patrzajcie, a nie poznawajcie.
Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa: “‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa; kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
10 Zatwardź serce ludu tego, a uszy jego obciąż, i oczy jego zawrzyj, aby nie widział oczyma swemi, a uszyma swemi nie słyszał, i sercem swem nie zrozumiał, a nie nawrócił się, i nie był uzdrowion.
Tsono anthu amenewa uwaphe mtima; uwagonthetse makutu, ndipo uwatseke mʼmaso. Mwina angaone ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi mitima yawo, kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
11 A gdym rzekł: Dokądże Panie? A on rzekł: Dokąd nie spustoszeją miasta, tak aby nie było obywatela; i domy, aby nie było w nich człowieka, a ziemia do szczętu nie spustoszeje;
Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?” Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti, “Mpaka mizinda itasanduka mabwinja nʼkusowa wokhalamo, mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo, mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
12 Dokąd Pan daleko nie zapędzi wszelkiego człowieka, a nie będzie doskonałe spustoszenie w pośród ziemi;
mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali, dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
13 Dokąd jeszcze na nią dziesiąta zguba nie przyjdzie, a dopiero skażona będzie, A wszakże jako one dęby, które są przy bramie Zallechet podporą, tak nasienie święte jest podporą jej.
Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko, nachonso chidzawonongedwa. Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu imasiyira chitsa pamene ayidula, chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”

< Izajasza 6 >