< Izajasza 56 >

1 Tak mówi Pan: Strzeżcie sądu, a czyńcie sprawiedliwość; bo blisko tego, że zbawienie moje przyjdzie, a sprawiedliwość moja objawiona będzie.
Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
2 Błogosławiony człowiek, który to czyni, i syn człowieczy, który się trzyma tego, przestrzegając sabatu, aby go nie splugawił, a strzegąc ręki swej, aby nie uczyniła nic złego.
Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
3 Niech tedy nie mówi cudzoziemiec, który przystaje do Pana, mówiąc: Zaiste Pan mię odłączył od ludu swego; niech też nie mówi trzebieniec: Otom ja drzewo suche.
Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
4 Albowiem tak mówi Pan o trzebieńcach, którzyby przestrzegali sabatów moich, a obrali to, co mi się podoba, i trzymali przymierze moje:
Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
5 Żeć im dam w domu swym i między murami mojemi miejsce, i imię lepsze niżeli synów i córek; dam im imię wieczne, które nie będzie wygładzone.
ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
6 A cudzoziemców, którzyby przystali do Pana, aby mu służyli, a miłowali imię Pańskie, będąc u niego za sługi, wszystkich przestrzegających sabaty, aby go nie splugawili, i zachowujących przymierze moje;
Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
7 Tych przywiodę na górę świętobliwości mojej, a uweselę ich w domu modlitwy mojej; całopalenia ich i ofiary ich przyjemne będą na ołtarzu moim; bo dom mój domem modlitwy nazwany będzie u wszystkich narodów.
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
8 Tak mówi panujący Pan, który zgromadza rozpędzonych z Izraela: Jeszcze zgromadzę do niego, i do zgromadzonych jego.
Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
9 Wszystkie zwierzęta polne przyjdźcie na pożarcie, i wszystkie zwierzęta leśne.
Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10 Stróżowie jego ślepi, wszyscy zgoła nic nie umieją, wszyscy są psami niememi, nie mogą szczekać; ospałymi są, leżą, kochają się w drzemaniu.
Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
11 A są psami obżartemi, nie mogą się nigdy nasycić; sami się pasąc nie umieją nauczać. Wszyscy się za drogą swoją udali, każdy za łakomstwem swojem z strony swej, mówiąc:
Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
12 Pójdźcie, nabiorę wina, a upijemy się mocnym napojem, a będzie nam jako dziś tak i jutro, i jeszcze daleko obficiej.
Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”

< Izajasza 56 >