< Izajasza 54 >

1 Śpiewaj niepłodna! która nie rodzisz, śpiewaj głośno, a krzycz, która w porodzeniu nie pracujesz; bo więcej będzie synów opuszczonej, niż synów tej, która ma męża, mówi Pan.
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 Rozprzestrzeń miejsce namiotu swego, a opon przybytków swych nie zabraniaj rozciągnąć: wyciągnij powrozy twoje, a kołki twoje utwierdź.
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 Bo się na prawo i na lewo rozsilisz, a nasienie twoje narody odziedziczy, i miasta spustoszone osadzi.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 Nie bój się, bo pohańbiona nie będziesz; a nie zapalaj się, bo nie przyjdziesz na posromocenie; owszem na zelżywość młodości twojej zapomnisz, a na pohańbienie wdowstwa twego więcej nie wspomnisz.
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 Albowiem małżonkiem twoim jest stworzycie twój, Pan zastępów imię jego, a odkupiciel twój, Święty Izraelski, Bogiem wszystkiej ziemi zwany będzie.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 Bo cię jako żony opuszczonej i strapionej w duchu, Pan powoła, a jako żony młodej, gdy odrzuconą będziesz, mówi Bóg twój.
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 Na małą chwilkę opuściłem cię; ale zaś w litościach wielkich zgromadzę cię.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 W maluczkim gniewie skryłem maluczko twarz swoję przed tobą; ale w miłosierdziu wiecznem zlituję się nad tobą, mówi Pan, odkupiciel twój.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 Bo to jest u mnie, co przy potopie Noego; jakom przysiągł, że się więcej nie będą rozlewać wody Noego po ziemi: takem przysiągł, że się nie rozgniewam na cię, ani cię zgromię.
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 A choćby się i góry poruszyły, i pagórki się zachwiały: jednak miłosierdzie moje od ciebie nie odstąpi, a przymierze pokoju mego nie wzruszy się, mówi twój miłościwy Pan.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 O utrapiona, wichrem rozmiotana, z pociechy obrana! oto Ja położę na karbunkułach kamienie twoje, a na szafirach założę cię.
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 I uczynię z kryształu okna twoje, a bramy twoje z kamienia rubinowego, i wszystkie granice twoje z kamienia kosztownego.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 A wszyscy synowie twoi będą wyuczeni od Pana, i obfitość pokoju będą mieli synowie twoi.
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Na sprawiedliwości ugruntowana będziesz; od ucisku się oddalisz, przetoż się go bać nie będziesz; i od starcia; bo się nie przybliży do ciebie.
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Oto nie jeden mieszkać będzie z tobą, który nie jest mój; ale ktoby mieszkając z tobą, był przeciwnym tobie, upadnie.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 Otom ja stworzył kowala poddymającego węgle w ogniu, a wyjmującego naczynie ku robocie swojej: Jam też stworzył pustoszyciela, aby wytracał.
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 Żadne naczynie urobione przeciw tobie nie zdarzy się, a każdy język powstawający przeciw tobie na sądzie potępisz. Toć jest dziedzictwo sług Pańskich, a sprawiedliwość ich odemnie, mówi Pan.
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.

< Izajasza 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark