< Izajasza 45 >

1 To mówi Pan pomazańcowi swemu Cyrusowi, którego prawicę ujmę, a porażę przed nim narody, i biodra królów rozpaszę, a pootwieram przed nim wrota, i bramy nie będą zamknięte.
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 Ja przed tobą pójdę, a krzywe drogi wyprostuję, wrota miedziane skruszę, a zawory żelazne porąbię;
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 I dam ci skarby skryte, i klejnoty schowane, abyś poznał, żem Ja Pan, Bóg Izraelski, który cię przyzywam imieniem twojem.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 Dla sługi mego Jakóba, i dla Izraela, wybranego mego, nazwałem cię imieniem twojem, przezwiskiem twojem, chociaż mię nie znasz.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 Jam Pan, a niemasz żadnego więcej, oprócz mnie niemasz żadnego Boga; przepasałem cię, aczkolwiek mię nie znasz:
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 Aby poznali od wschodu słońca, i od zachodu słońca, iż niemasz żadnego oprócz mnie, Jam Pan, a niemasz żadnego więcej;
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Który czynię światłość, i stwarzam ciemności; sprawuję pokój, i stwarzam złe. Ja Pan czynię to wszystko.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Spuście niebiosa rosę z góry, a obłoki niech kropią sprawiedliwość; niech się otworzy ziemia, a niech wyrośnie zbawienie, a sprawiedliwość niech wespół zakwitnie. Ja Pan sprawię to.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Biada temu, który się spiera z stworzycielem swoim, będąc skorupą, jako inne skorupy gliniane. Izali glina rzecze garncarzowi swemu: Cóż czynisz? Robota twoja zaprawdę nikczemna jest.
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Biada temu, który mówi ojcu: Cóż płodzisz? a niewieście: Cóż porodzisz?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Tak mówi Pan, Święty Izraelski, i Twórca jego: O przyszłe rzeczy pytajcie mię, a synów moich, i sprawę rąk moich poruczajcie mi.
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 Jam uczynił ziemię, i człowiekam na niej stworzył. Jam jest, którego ręce rozciągnęły niebiosa, a wszystkiemu wojsku ich rozkazuję.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 Jam go wzbudził w sprawiedliwości, i wszystkie drogi jego wyprostuję. Onci zbuduje miasto moje, a więźniów moich wypuści, nie za okup, ani za dar, mówi Pan zastępów.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Tak mówi Pan: Praca Egipska, i kupiectwo Murzynów, i Sebejczyków, mężowie wysocy do ciebie przyjdą, a twoi będą; za tobą chodzić będą, w pętach pójdą, tobie się kłaniać, i tobie się korzyć będą, mówiąc: Tylko w tobie jest Bóg, a niemasz żadnego więcej, oprócz tego Boga.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Zaprawdę tyś jest Bóg skryty, Bóg Izraelski, zbawiciel.
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 Wszyscy się oni zawstydzą, i pohańbieni będą; czyniciele bałwanów społu z hańbą odstąpią.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 Ale Izrael zbawion będzie przez Pana zbawieniem wiecznem; nie zawstydzicie się, ani będziecie pohańbieni, aż na wieki wieczne.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 Bo tak mówi Pan, który stworzył niebiosa (ten Bóg, który stworzył ziemię, i uczynił ją! który ją utwierdził, nie na próżno stworzył ją, na mieszkanie utworzył ją): Jam Pan, a niemasz żadnego więcej.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Nie mówiłem potajemnie na miejscu ziemskiem ciemnem; nie na próżno mówię nasieniu Jakóbowemu: Szukajcie mię. Ja Pan mówię sprawiedliwość, a zwiastuję prawość.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Zgromadźcie się, a przyjdźcie; przybliżcie się wespół, wy, którzyście pozostali między poganami. Nic nie wiedzą, którzy się z drewnianemi bałwanami swemi noszą; bo się modlą bogu, który nie może wybawić.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Oznajmujcież a przywiedźcie innych, a niech pospołu w radę wnijdą, a ukażą, kto to od dawnego czasu przepowiedział? kto od onego czasu oznajmił? Izali nie Ja Pan? Boć niemasz żadnego innego Boga oprócz mnie. Niemasz Boga sprawiedliwego, i zbawiciela innego oprócz mnie.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Obejrzyjcież się na mię, abyście zbawione były wszystkie kończyny ziemi; bom Ja Bóg, a niemasz żadnego więcej.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 Przysiągłem sam przez się; wyszło z ust moich słowo sprawiedliwe, które się nazad nie wróci: Że się mnie kłaniać będzie wszelkie kolano, i przysięgać każdy język.
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 Mówiąc: Tylko w Panu mam wszelką sprawiedliwość i siłę. Takowi aż do niego przyjdą; ale pohańbieni będą wszyscy, którzy się gniewem zapalają przeciwko niemu.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 W Panu usprawiedliwione będzie, i przechwalać się będzie wszystko nasienie Izraelskie.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< Izajasza 45 >