< Izajasza 40 >

1 Cieszcie, cieszcie lud mój! mówi Bóg wasz.
Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
2 Mówcie do serca Jeruzalemu: ogłaszajcie mu, że się już dopełnił czas postanowiony jego, że jest odpuszczona nieprawość jego, i że wziął z ręki Pańskiej w dwójnasób za wszystkie grzechy swoje.
Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
3 Głos wołającego na puszczy: Gotujcie drogę Pańską, prostą czyńcie na pustyni ścieszkę Boga naszego.
Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
4 Każda dolina niech podniesiona będzie, a każda góra i pagórek niech poniżony będzie; co jest krzywego, niech się wyprostuje, a miejsca nierówne niech będą równiną.
Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
5 Bo się objawi chwała Pańska, a ujrzy wszelkie ciało społem, iż usta Pańskie mówiły.
Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
6 Głos mówiącego: Wołaj. I rzekł: Cóż mam wołać? To: Wszelkie ciało jest trawa, a wszystka zacność jego jako kwiat polny.
Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
7 Trawa usycha, kwiat opada; skoro wiatr Pański powionie nań; zaprawdęć ludzie są tą trawą.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
8 Trawa usycha, kwiat opada; ale słowo Boga naszego trwa na wieki.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
9 Wstąp sobie na górę wysoką, Syonie! który opowiadasz rzeczy ucieszne. Podnieś mocno głos twój, Jeruzalemie! które opowiadasz rzeczy pocieszne; podnieś, nie bój się, rzecz miastom Judzkim: Oto Bóg wasz.
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
10 Oto panujący Pan przyjdzie przeciwko mocnemu, a ramię jego panować będzie nad nim; oto zapłata jego z nim, a dzieło jego przed nim.
Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 Jako pasterz trzodę swoję paść będzie; do naręcza swego zgromadzi baranki, i na łonie swem piastować je będzie, a kotne zwolna poprowadzi.
Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
12 Kto zmierzył wody garścią swoją, a niebiosa piędzią rozmierzył? a kto proch ziemi miarą zmierzył? kto zważył na wadze góry, a pagórki na szalach?
Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
13 Któż doścignął ducha Pańskiego, a kto radcą jego był, żeby mu oznajmił?
Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
14 Z kim wszedł w radę, żeby mu rozumu przydał, a nauczył go ścieżek sądu? Kto go nauczył umiejętności, a drogę wszelakiej roztropności ukazał mu?
Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
15 Oto narody są jako kropla z wiadra, a jako proszek na szalach poczytane są; wyspy jako najmniejszą rzecz porywa.
Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
16 I Liban nie wystarczyłby ku wznieceniu ognia, i zwierzęta jego nie wystarczyłyby na całopalenie.
Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
17 Wszystkie narody są jako nic przed nim; za nic i za marność poczytane są u niego.
Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
18 Komuż tedy podobnym uczynicie Boga? A jakie podobieństwo przyrównacie mu?
Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
19 Rzemieślnik uleje bałwana a złotnik złotem go powlecze, i łańcuszki srebrne do niego odleje.
Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
20 A ten, który dla ubóstwa nie ma co ofiarować, obiera drzewo, któreby nie próchniało, i rzemieślnika umiejętnego sobie szuka, aby wygotował bałwana rytego, któryby się nie poruszył.
Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
21 Izali nie wiecie? Izali nie słyszycie? Izali się wam nie opowiada od początku? Izali nie zrozumiewacie od założenia gruntów ziemi?
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
22 Ten, który siedzi nad okręgiem ziemi, której obywatele są jako szarańcza; ten, który rozpostarł niebiosa jako cienkie płótno, a rozciągnął je, jako namiot ku mieszkaniu:
Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
23 Tenci książąt w niwecz obraca, sędziów ziemskich jako nic rozprasza.
Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
24 Że nie bywają szczepieni ani wsiani, ani się też wkorzeni w ziemi pień ich; i jako jedno powienie na nich, wnet usychają, a wicher jako źdźbło unosi ich.
Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
25 Komuż mię tedy przyrównacie, abym mu był podobny? mówi Święty.
Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
26 Podnieście ku górze oczy wasze, a obaczcie! Kto to stworzył? kto wywiódł w poczcie wojsko ich, a to wszystko z imienia przyzywa, według wielkości siły, i wielkiej mocy, tak, że ani jedno z nich nie zginie?
Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
27 Przeczże tedy powiadasz, Jakóbie! przeczże tak mówisz Izraelu: Skryta jest droga moja przed Panem, a sprawa moja przed Boga mego nie przychodzi?
Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
28 Izali nie wiesz? izaliś nie słyszał, że Bóg wieczny Pan, który stworzył granice ziemi, nie ustanie, ani się spracuje, i że nie może być dościgniona mądrość jego?
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
29 Który dodaje spracowanemu siły, a tego, który nie ma żadnej siły, moc rozmnaża.
Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
30 Młódź ustaje i omdlewa, a młodzieńcy w młodości upadają:
Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
31 Ale którzy oczekują Pana, nabywają nowej siły; podnoszą się piórami jako orły, bieżą a nie spracują się, chodzą a nie ustawają.
koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.

< Izajasza 40 >