< Izajasza 35 >

1 Weselić się z tego będzie pustynia i miejsce leśne, a rozraduje się i zakwitnie jako róża.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 Ślicznie zakwitnie, i radując się weselić się będzie z wykrzykaniem; chwała Libanu będzie jej dana, i ozdoba Karmelu i Saronu. One ujrzą chwałę Pańską i ozdobę Boga naszego.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Umacniajcie ręce osłabiałe, a kolana zemdlałe posilajcie.
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Mówcie do zatrwożonych w sercu: Zmocnijcie się, nie bójcie się; oto Bóg wasz z pomstą przyjdzie; z nagrodą Bóg sam przyjdzie, i zbawi was.
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Tedy się otworzą oczy ślepych, a uszy głuchych tworzone będą.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Tedy poskoczy chromy jako jeleń, a niemych język śpiewać będzie; albowiem wody na puszczy wynikną, a potoki na pustyniach.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 I stanie się miejsce suche jeziorem, a bezwodne źródłami wód; w łożyskach smoków, kędy legali, trawa, trzcina, i sitowie rość będzie.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 I będzie tam droga i ścieszka, która drogą świętą słynąć będzie; nie pójdzie po niej nieczysty, ale będzie dla onych samych. Którzy tą drogą pójdą, i głupi nawet, nie zbłądzą.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Nie będzie tam lwa, a okrutny zwierz nie będzie chodził po niej, ani się tam znajdzie; ale wybawieni po niej chodzić będą.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 Odkupieni, mówię, Pańscy nawrócą się, i przyjdą na Syon z śpiewaniem, a wesele wieczne będzie na głowie ich; radość i wesele otrzymają, a żałość i smutek uciecze.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

< Izajasza 35 >