< Izajasza 34 >

1 Przystąpcie, narody! ku słuchaniu, a wy ludzie pilnie uważajcie! Niech słucha ziemia, i pełność jej, okrąg ziemi, i wszystko, co się rodzi na niej.
Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
2 Bo rozgniewanie Pańskie jest na wszystkie narody, a popędliwość jego na wszystko wojsko ich; wytraci je jako przeklęte, a poda je na zabicie.
Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
3 I będą wyrzuceni pobici ich, a z trupów ich smród wynijdzie, a krew ich z gór popłynie.
Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
4 I niszczeć będzie wszystko wojsko niebieskie, a niebiosa jako księgi zwinione będą, i wszystko wojsko ich opadnie, jako opada liść z winnej macicy, i jako opada niedojrzały owoc z figowego drzewa.
Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
5 Albowiem opojony jest na niebie miecz mój; oto zstąpi na Edomczyków, i na sąd ludu przeklętego odemnie.
Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
6 Miecz Pański pełny będzie krwi, utłuści się w łoju i we krwi baranków i kozłów, w łoju nerek baranich; bo ofiara Pańska będzie w Bocra, a porażka wielka w ziemi Edomskiej.
Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
7 Zstąpią z nimi i jednorożce, i byki z wołami, i opojona będzie krwią ziemia ich, a proch ich będzie opojony tukiem.
Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
8 Albowiem to dzień pomsty Pańskiej będzie, i rok odpłaty, aby się pomszczono Syonu.
Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
9 I obrócą się potoki jej w smołę, a proch jej w siarkę, a ziemia jej obróci się w smołę gorejącą;
Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
10 Ani w nocy ani we dnie nie zagaśnie, na wieki będzie występował dym jej; od narodu do narodu pustą zostanie; na wieki wieczne nie będzie, ktoby szedł przez nią.
Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
11 Ale ją pelikan i bąk posiędą, a sowa i kruk mieszkać w niej będą; i rozciągnie po niej sznur spustoszenia, i wagi próżności.
Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
12 Szlachty jej na królestwo wzywać będą, ale nie będzie tam żadnego; bo wszyscy książęta jej wniwecz się obrócą.
Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
13 I urosną na pałacach ich ciernie, pokrzywy i oset na zamkach ich; i będzie przybytkiem smoków, a mieszkaniem strusiów.
Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
14 Tam się będą potykały dzikie zwierzęta z koczkodanami, i pokusa jedna drugiej ozywać się będzie; tam leżeć będzie jędza, a znajdzie sobie odpocznienie.
Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
15 Tam sobie sęp gniazdo uczyni, zniesie jajka, i wylęże, a schowa pod cień swój; tamże się zlecą kanie jedna do drugiej.
Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
16 Szukajcież w księgach Pańskich, a czytajcie; ani jedno z tych nie uchybi, a jedno bez drugiego nie będzie; albowiem usta Pańskie to rozkazały, a duch jego sam zgromadzi je.
Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
17 Bo im on los rzucił, a ręka jego onę im sznurem rozmierzyła; aż na wieki dziedzicznie ją posiądą, od narodu do narodu mieszkać w niej będą.
Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.

< Izajasza 34 >