< Izajasza 33 >

1 Biada tobie, który łupisz, chociażeś sam nie złupiony, i który zdradzasz, chociażeś sam nie był zdradzony! Gdy łupić przestaniesz, będziesz też złupiony; gdy zdradzać przestaniesz, będą cię też zdradzać.
Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
2 Panie! zmiłuj się nad nami, ciebie oczekujemy. Bądź ramieniem swoich na każdy poranek, a zbawieniem naszem czasu utrapienia.
Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
3 Przed głosem ogromnym rozpierzchną się narody; przed wywyższeniem twojem rozproszą się poganie.
Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
4 I będą zebrane łupy wasze, jako zbierają chrząszcze; a jako przypada szarańcza, tak oni przypadną na nie.
Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
5 Pan będzie wywyższony, bo mieszka na wysokości; napełni Syon sądem i sprawiedliwością.
Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
6 Mądrość i umiejętność będą utwierdzeniem czasów twoich, siłą i obfitem zbawieniem twem, a bojaźń Pańska skarbem twoim.
Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
7 Oto mocarze ich wołają na dworze, posłowie pokoju gorzko płaczą.
Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
8 Spustoszały drogi, przestano ścieszką chodzić; złamał przymierze, znieważył miasta, a człowieka za nic sobie nie ma.
Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
9 Płakała i zwątlała ziemia; zawstydzony jest Liban i uwiądł; Saron się stał jako pustynia, i otłuczono Basan i Karmel.
Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
10 Teraz powstanę, mówi Pan, teraz się wywyższę, teraz się podniosę.
Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
11 Począwszy słomę, urodzicie mierzwę; duch wasz was pożre jako ogień.
Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
12 I będą narody, jako wypalone wapno; będą jako ciernie wycięte, ogniem spalone.
Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
13 Słuchajcie, którzyście daleko, com uczynił, a bliscy poznajcie moc moję.
Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
14 Zlękli się na Syonie grzesznicy, strach zdjął obłudników mówiących: Któż z nas ostać się może przed ogniem pożerającym? Któż z nas ostać się może przed płomieniem wiecznym?
Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
15 Ten, który chodzi w sprawiedliwości, a mówi, co jest prawego; który się zyskiem niesprawiedliwym brzydzi; który otrząsa ręce swe, aby darów nie brał; który zatula uszy swe, aby nie słuchał o rozlaniu krwi, i zamruża oczy swoje, aby nie patrzał na złe:
Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
16 Ten na wysokościach mieszkać będzie, zamki na skałach będą ucieczką jego; chleb jego dany mu będzie, wody jego nie ustaną.
Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
17 Króla w piękności jego oglądają oczy twoje, ujrzą i ziemię daleką.
Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
18 Serce twoje będzie rozmyślało o starchu, mówiąc: Gdzie teraz jest pisarz? gdzież teraz jest poborca? gdzież jest obliczający wieże?
Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
19 Ludu okrutnego nie oglądasz, ludu głębokiej mowy, któregoś nie słyszał, i języka obcego, któregobyś nie rozumiał.
Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
20 Wejrzyj na Syon, miasto uroczystych swiąt naszych, oczy twoje niechaj patrzą na Jeruzalem, na mieszkanie spokojne, na namiot, który nie będzie przeniesion; kołki jego na wieki się nie poruszą, a żaden powróz jego nie zerwie się,
Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
21 Przeto, że nam na tem miejscu Pan wielmożny jest rzekami strumieni szerokich, po których nie pójdą z wiosłami, ani okręt wielki po nich przechodzić będzie.
Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
22 Bo Pan jest sędzia nasz, Pan zakonodawca nasz; Pan król nasz; on nas zbawi.
Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
23 Osłabiały powrozy twoje, nie będą mogły w klubie zatrzymać masztu twego, ani rozciągną żaglów. Tedy rozdzielone będą łupy korzyści wielkiej, że i chromi rozchwycą łupy.
Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
24 A nie rzecze żaden z obywateli: Zachorowałem; lud, który mieszka w nim, uwolniony będzie od nieprawości.
Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.

< Izajasza 33 >