< Izajasza 31 >

1 Biada tym, którzy zstępują do Egiptu o pomoc, a na koniach spolegają, i ufają w wozach, że ich wiele, i w jezdnych, iż są mocni bardzo, a nie oglądają się na Świętego Izraelskiego, a Pana nie szukają!
Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
2 Aleć on też jest mądry, przetoż przywiedzie złe, a słów swoich nie odmieni; lecz powstanie przeciw domowi złośników i przeciwko ratunkowi tych, którzy broją nieprawość.
Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
3 Albowiem Egipczanie są ludzie a nie Bóg, a konie ich ciało, a nie duch. Przetoż skoro Pan wyciągnie rękę swą, padnie i pomocnik, padnie i ten, któremu dawają pomoc; a tak wszyscy społem zginą.
Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
4 Bo tak rzekł Pan do mnie: Jako gdy ryczy lew, i szczenię lwie nad łupem swym, a choć zwoływają przeciwko niemu gromadę pasterzy, przecie się on wrzasku ich nie lęka, ani się korzy przed hukiem ich; tak Pan zastępów zstąpi, aby walczył o górę Syońską, i o pagórek jej.
Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
5 Jako ptaki latają około gniazda swego, tak obroni Pan zastępów Jeruzalem, i owszem, broni i wybawia, a przechodząc z pomstę zachowa.
Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
6 Nawróćcie się do tego, od którego głęboko zabrnęli synowie Izraelscy,
Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
7 Albowiem dnia onego odrzuci każdy bałwany swe srebrne, i bałwany swe złote, które wam naczyniły ręce wasze na grzech.
Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
8 I upadnie Assyryjczyk od miecza nie męskiego, a miecz nie człowieczy pożre go: i uciecze przed mieczem, a młodzieńcy jego hołdownikami będą.
“Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
9 A tak opokę swoję od strachu minie, a książęta jego ulękną się przed chorągwią, mówi Pan, którego ogień jest na Syonie, a piec w Jeruzalemie.
Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.

< Izajasza 31 >