< Izajasza 22 >

1 Brzemię doliny widzenia. Cóż ci się stało, żeś wszystka na dachy wystąpiła?
Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
2 Miasto pełne wrzasku, i zgiełku, miasto weselące się! Pobici twoi nie są pobici mieczem, ani zginęli w bitwie.
Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
3 Wszyscy książęta twoi naporząd się rozpierzchnęli, od strzelców powiązani są wespół, i ci, którzy z daleka uciekają.
Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
4 Dlategom rzekł: Odstąpcie odemnie, abym gorzko płakał; nie kwapcie się, cieszyć mię w spustoszeniu córki ludu mojego.
Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
5 Albowiem to jest dzień ucisku i podeptania, i zamięszania od Pana, Pana zastępów, w dolinie widzenia, dzień burzenia murów, i wołania na góry.
Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
6 Elam też wziął sajdak z wozami ludu wojennego, a Kir okazał tarczę swoję.
Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
7 I stało się, że wyborne doliny twoje napełnione były wozami, a jezdni się potężnie zaszańcowali u bramy.
Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
8 I odkryta była zasłona Judowa; a poglądałeś dnia onego na zbrojownię w domu lasu.
zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
9 I poglądaliście na rozwaliny miasta Dawidowego, bo ich wiele było; i zgromadziły się wody sadzawki dolnej.
inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
10 Także policzyliście domy w Jeruzalemie, a rozwaliliście domy na oprawę murów.
Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
11 Uczyniliście też przekop między dwoma murami, dla wód stawu starego, a nie oglądaliście się na tego, co go sprawił, a tego, który go zdawna zbudował, nie widzieliście.
Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
12 Nadto, gdy wołał Pan, Pan zastępów, dnia onego do płaczu i do narzekania, i do obłysienia się, i do przepasania się worem;
Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
13 A oto radość i wesele wasze, zabijać woły, i bić owce, a jedząc mięso, i pijąc wino, mówić: Jedzmy, pijmy, bo jutro pomrzemy.
Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
14 Aleć to doszło uszów moich, mówi Pan zastępów. Przetoż wam ta nieprawość nie będzie odpuszczona; aż pomrzecie, mówi Pan, Pan zastępów.
Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Tak mówi Pan, Pan zastępów: Idź, wnijdź do tego podskarbiego, do Sobny, który jest przełożonym w domu, i rzecz:
Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
16 Co ty tu masz? albo kogo tu masz, żeś tu sobie wykował grób? Wykowałeś sobie na wysokiem miejscu grób swój, a wystawiłeś na skale przybytek swój?
Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
17 Oto Pan, który cię przykrył jako zacnego męża, a który cię kosztownie przyodział,
“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
18 Prędko cię zatoczy jako kulę do ziemi szerokiej i przestronnej; tam umrzesz, tam i wozy sławy twojej zginą, o hańbo domu Pana swego!
Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
19 A tak wypędzę cię z stanowiska twego, a z urzędu twego złożę cię.
Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
20 A dnia onego przyzwię sługę swego Elijakima, syna Helkijaszowego;
“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 I oblekę go w szatę twoję, i pasem twoim potwierdzę go, panowanie też twoje dam w rękę jego; i będzie za ojca obywatelom Jeruzalemskim, i domowi Judzkiemu.
Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 I położę klucz domu Dawidowego na ramieniu jego; gdy otworzy, nikt nie zawrze, a gdy zawrze, nikt nie otworzy.
Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 I wbiję go jako gwóźdź na miejscu pewnem, a będzie stolicą chwały domu ojca swego.
Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 A zawiśnie na nim wszystka sława domu ojca jego, synowie i córki, i wszystko naczynie by najmniejsze, od naczynia, z którego piją, aż do każdego naczynia winnego.
Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 Dnia onego, mówi Pan zastępów, będzie wyjęty gwóźdź, który był wbity na miejscu pewnem, a będzie przycięty i upadnie; odcięte będzie i brzemię, które jest na nim; bo Pan mówił.
“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.

< Izajasza 22 >