< Izajasza 20 >

1 Roku, którego Tartan przyciągnął do Azotu, posłany będąc od Sargona, króla Assyryjskiego, i walczył przeciw Azotowi, i dobył go;
Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
2 Onegoż czasu rzekł Pan przez Izajasza, syna Amosowego, mówiąc: Idź, a rozwiąż wór z biódr twoich, a bóty twoje zzuj z nóg twoich; i uczynił tak, i chodził nago i boso.
nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
3 I rzekł Pan: Jako chodzi sługa mój Izajasz nago i boso, na znak i na cud tego, co się ma stać trzeciego roku Egiptowi i Murzyńskiej ziemi:
Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
4 Tak powiedzie król Assyryjski więźniów Egipskich, i pojmanych Murzyńskich, młodych i starych, nagich i bosych, z obnażonemi zadkami na hańbę Egipczyków.
momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
5 I przelękną się, i wstydzić się będą za Murzynów, na których się oglądali, i za Egipczanów, z których się chlubili.
Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
6 Tedy rzecze dnia onego obywatel tej wyspy: Oto toć jest ucieczka nasza, do którejśmy uciekali o pomoc, abyśmy wyswobodzeni byli z mocy króla Assyryjskiego; jakożbyśmy tedy ujść mogli?
Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”

< Izajasza 20 >