< Izajasza 2 >

1 Słowo, które widział Izajasz, syn Amosowy, nad Judą i nad Jeruzalemem.
Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
2 I stanie się w ostateczne dni, że będzie przygotowana góra domu Pańskiego na wierzchu gór, i wywyższy się nad pagórkami, a zbieżą się do niej wszystkie narody.
Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3 I pójdzie wiele ludzi, mówiąc: Pójdźcie a wstąpmy na górę Pańską, do domu Boga Jakóbowego, a będzie nas uczył dróg swoich, i będziemy chodzili ścieszkami jego; albowiem z Syonu wyjdzie zakon, a słowo Pańskie z Jeruzalemu.
Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4 I będzie sądził między narodami, a będzie karał wiele ludzi. I przekują miecze swe na lemiesze, a włócznie swe na sierpy; nie podniesie naród przeciw narodowi miecza, ani się będą ćwiczyć do bitwy.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
5 Domie Jakóbowy! pójdźcie, a chodźmy w światłości Pańskiej.
Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
6 Aleś ty opuścił lud swój, dom Jakóbowy! gdyż są pełni obrzydliwości narodów wschodnich, i są wieszczkami jako Filistynowie, a w synach cudzych się kochali.
Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7 I napełniona jest ziemia ich srebrem i złotem, a końca niemasz skarbom ich.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8 Napełniona jest ziemia ich końmi, a końca niemasz wozom ich. Napełniona też jest ziemia ich bałwanami, robocie rąk swoich kłaniają się, które poczyniły palce ich.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9 I kłania się pospolity człowiek, a uniża się i zacny mąż; przetoż nie odpuszczaj im.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
10 Wnijdź w skałę, a skryj się w prochu przed strachem Pańskim, i przed chwałą majestatu jego.
Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Oczy wyniosłe człowiecze zniżone będą, a wysokość ludzka nachylona będzie; ale sam Pan wywyższony będzie dnia onego.
Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
12 Albowiem dzień Pana zastępów przyjdzie na wszelkiego pysznego i wyniosłego, i na każdego wywyższonego, że będzie poniżony;
Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
13 I na wszystkie cedry Libańskie wysokie a podniosłe, i na wszystkie dęby Basańskie;
tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 I na wszystkie góry wysokie, i na wszystkie pagórki wyniosłe;
tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 I na każdą wieżę wysoką, i na każdy mur obronny;
tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
16 I na wszystkie okręty morskie, i na wszystkie malowania rozkoszne.
tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
17 I będzie nachylona wyniosłość człowiecza, a wywyższenie ludzkie zniżone będzie; ale sam Pan wywyższony będzie dnia onego.
Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18 Lecz bałwany ich do szczętu pokruszone będą.
ndipo mafano onse adzatheratu.
19 Tedy wnijdą do jaskiń skalnych, i do jam podziemnych przed strachem Pańskim, i przed chwałą majestatu jego, gdy powstanie, aby ziemię potarł.
Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 Dnia onego wrzuci człowiek bałwany swe srebrne i bałwany swe złote, które mu naczyniono, aby się im kłaniał, w dziury kretów i nietoperzy.
Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 I wnijdzie w rozpadliny skalne, i na wierzchołki opok przed strachem Pańskim, i przed chwałą majestatu jego, gdy powstanie, aby potarł ziemię.
Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
22 Przestańcież ufać w człowieku, którego dech jest w nozdrzach jego; bo za cóż on ma być poczytany?
Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?

< Izajasza 2 >