< Izajasza 18 >

1 Biada ziemi, którą zaćmiają skrzydła, która jest przy rzekach ziemi Murzyńskiej!
Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
2 Która posyła posłów przez morze po wodach w łodziach z sitowia, mówiąc: Idźcie, posłowie prędcy! do narodu rozszarpanego i splundrowanego, do ludu strasznego z dawna i dotąd, do narodu do szczętu podeptanego, którego ziemię rzeki rozerwały.
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
3 Wszyscy obywatele świata i mieszkający na ziemi ujrzycie, gdy będzie chorągiew podniesiona na górach, i gdy w trąby trąbić będą, usłyszycie.
Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
4 Albowiem tak mówi Pan do mnie: Uspokoję się, a przypatrywać się będę z przybytku mojego, a będę jako ciepło jasne po deszczu, a jako obłok wypuszczający rosę gorącości żniwa.
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
5 Bo przed zbieraniem wina, gdy się puści pączki, a kwiat wyda grono cierpkie jeszcze rosnące, tedy oberznie latorostki nożami, a gałęzie odejmie i obetnie.
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
6 I będą zostawione wszystkie wespół ptastwu na górach i zwierzętom ziemskim; i będzie na nich przez lato ptastwo, a wszelaki zwierz ziemski na nich zimować będzie.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
7 Czasu onego przyniesiony będzie dar Panu zastępów od ludu rozszarpanego i splundrowanego, od ludu strasznego z dawna i dotąd, od narodu do szczętu podeptanego, którego ziemię rzeki rozrywały; a przeniesiony będzie na miejsce imienia Pana zastępów, na górze Syon.
Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.

< Izajasza 18 >