< Izajasza 15 >

1 Brzemię Moabczyków. Ponieważ w nocy zburzone i spustoszone będzie Ar Moabskie, ponieważ w nocy zburzone i spustoszone będzie Kir Moabskie:
Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 Wstąpi do Bait, i do Dybon, i do Bamot z płaczem; nad Nebo, i nad Medebą Moab kwilić będzie; na każdej głowie jego będzie łysina, i każda broda ogolona będzie.
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 Na ulicach jego przepaszą się worem; na dachach jego i na rynkach jego każdy kwilić będzie, wracajac się z płaczem.
Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
4 I będzie wołał Hesebon i Eleale, aż w Jahas słyszany będzie głos ich; owszem i zbrojni Moabscy narzekać będą, a dusza każdego z nich porzewniać sobie będzie, mówiąc:
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
5 Serce moje ryczy nad Moabem i nad twierdzami jego, aż słyszeć w Zoar, jako jałowica trzyletnia; bo drogą Luchytską z płaczem pójdzie, a na drodze Choronaim krzyk jako w porażce podniosą;
Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 Przeto, że wody Nymrym zginą, że poschną zioła, uwiędnie trawa, a nic nie będzie zielonego.
Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 Przetoż, cokolwiek sobie zachowali, i majętności ich, odniosę do potoku Arabskiego.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 Bo obejdzie krzyk granicę Moabską, aż do Eglaim narzekanie jego, i aż do Beer Elim kwilenie jego;
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 Ponieważ i wody Dymońskie krwi pełne będą: bo przyłożę Dymonowi przydatki, a na tych, którzyby uszli z Moabczyków, poślę lwy, i na ostatki w tej ziemi.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

< Izajasza 15 >