< Izajasza 14 >

1 Albowiem zlituje się Pan nad Jakóbem, a obierze zasię Izraela, i da im odpocznąć w ziemi ich; a przyłączy się do nich cudzoziemiec, i przystaną do domu Jakóbowego.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Bo wezmą z sobą narody, i przywiodą je do miejsca swego; i weźmie je sobie dom Izraelski w ziemi Pańskiej w dziedzictwo za sługi i za służebnice; i imać będą tych, którzy ich imali, a panować będą nad tymi, którzy ich ciemiężyli.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 A dnia onego, któregoć Pan da odpocznienie od pracy twojej i od strachu twego, i od niewoli ciężkiej, w którąś był podbity,
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 Weźmiesz tę przypowieść przeciw królowi Babilońskiemu, i rzeczesz: O jako ustał poborca, ustał podatek złota!
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 Pan złamał kij niezbożnych, i rózgę panujących;
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 Tego, który ludzi bijał w zapalczywości biciem ustawicznem, panował w gniewie nad narodami bez litości dręczonemi;
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 Teraz odpoczywa i jest w pokoju wszystka ziemia, wszyscy głośno śpiewają;
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 I jodły się weselą nad tobą, i cedry Libańskie, mówiąc: Od tego czasu, jakoś ty poległ, nie powstał, ktoby nas podcinał.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 I piekło ze spodku wzruszyło się dla ciebie, aby tobie przychodzącemu zaszło; wzbudziło dla ciebie umarłych, wszystkich książąt ziemi; rozkazało powstać z stolic swoich i wszystkim królom narodów. (Sheol h7585)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
10 Ci wszyscy odpowiadając mówią do ciebie: I tyś zemdlony jako i my, a stałeś się nam podobnym.
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Strącona jest do piekła, pycha twoja i dźwięk muzyki twojej; podesłanoć mole, a robaki cię przykrywają. (Sheol h7585)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
12 Jakoż to, żeś spadł z nieba, o jutrzenko! która wschodzisz rano? powalonyś aż na ziemię, któryś wątlił narody!
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Wszakieś ty mawiał w sercu swem: Wstąpię na niebo, nad gwiazdy Boże wywyższę stolicę moję, a usiądę na górze zgromadzenia, na stronach północnych:
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 Wstąpię na wysokość obłoków, będę równy Najwyższemu.
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Wszakże strącon jesteś aż do piekła, w głębokość dołu. (Sheol h7585)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
16 Którzy cię ujrzą, za tobą się oglądać, i przypatrywać ci się będą mówiąc: Onże to mąż, który trwożył ziemię? który trząsał królestwami?
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 Który obrócił okrąg świata w pustynię, a miasta jego poburzył, a więźniom swoim nie otwarzał ciemnicy?
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Wszyscy królowie narodów, cokolwiek ich było, pochowani są w sławie, każdy w domu swoim.
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 Aleś ty odrzucony od grobu swego, jako latorośl obrzydła, jako szata zabitych, których poprzebijano mieczem, którzy zstępują do grobu kamienistego, jako ścierw podeptany.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Nie będzisz miał uczęstnictwa z nimi w pogrzebie; boś ziemię twoję pokaził, i lud swój pomordował; albowiem nasienie złośników nie będzie wspominane na wieki.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Gotujcie synów jego na zamordowanie dla nieprawości ojców ich, aby nie powstali, i nie odziedziczyli ziemi, nie napełnili miastami okręgu ziemskiego.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 Bo powstanę przeciwko nim, mówi Pan zastępów, a wykorzenię imię Babilonu, i ostatki jego, tak syna jako i wnuka, mówi Pan;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 I uczynię je osiadłością bąków, i kałużami wód, i wymiotę go miotłą spustoszenia, mówi Pan zastępów.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 Przysiągł Pan zastępów, mówiąc: Zaiste, jakom umyślił, tak będzie, a jakom uradził, tak się stanie;
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Iż potrę Assyryjczyka w ziemi mojej, a na górach moich podepczę go; a odejdzie od nich jarzmo jego, i brzemię jego z ramienia jego zdjęte będzie.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 Tać jest rada uradzona przeciw onej wszystkiej ziemi; a tać jest ręka wyciągniona przeciwko tym wszystkim narodom.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 A ponieważ Pan zastępów postanowił, któż to wzruszy? a rękę jego wyciągnioną któż odwróci?
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 Roku, którego umarł król Achaz, stało się to proroctwo;
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Nie raduj się, ty wszystka ziemio Filistyńska! iż złamana jest rózga tego, który cię bił; bo z korzenia wężowego wynijdzie bazyliszek, a płód jego będzie smok ognisty latający.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 I będą się paść pierworodni nędznych, a ubodzy bezpiecznie odpoczną; ale korzeń twój głodem wygubię a ostatki twoje wybiję.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Kwilże bramo! krzycz miasto! jużeś się rozpłynęła wszystka ty ziemio Filistyńska; bo od północy ogień przyjdzie, a nie będzie, coby stronił od pocztów jego.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 A cóż odpowiedzą posłom narodu? To, że Pan ugruntował Syon, a do niego się uciekać będą ubodzy ludu jego.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

< Izajasza 14 >