< Izajasza 13 >

1 Brzemię Babilonu, które widział Izajasz, syn Amosowy.
Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Na górze wysokiej podnieście chorągiew, podwyżcie głos do nich, dajcie znać ręką, a niechaj wnijdą w bramy książęce.
Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
3 Jam przykazał poświęconym moim; przyzwałem też i mocarzów moich do wykonania gniewu mego, którzy się weselą z wywyższenia mego.
Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 Głos zgrai na górach, jako ludu gęstego, głos i dźwięk królestw i narodów zgromadzonych: Pan zastępów spisuje wojsko na wojnę.
Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
5 Ciągną z ziemi dalekiej, od kończyn niebios, mianowicie Pan i naczynia popędliwości jego, aby zburzył wszystkę ziemię.
Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Kwilcie! albowiem blisko jest dzień Pański, który przyjdzie jako spustoszenie od Wszechmocnego.
Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 Dlatego wszelkie ręce osłabieją, a wszelkie serce człowiecze stopnieje.
Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 I będą przestraszeni, uciski i trapienia ogarną ich, jako rodząca boleć będą. Każdy nad bliźnim swoim zdumieje się, oblicza ich płomieniowi podobne będą.
Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 Oto dzień Pański srogi idzie w zapalczywości i popędliwości gniewu, aby obrócił tę ziemię w pustynię, a grzeszników jej aby z niej wygładził.
Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 Bo gwiazdy niebieskie i planety ich nie dopuszczą świecić światłu swemu; zaćmi się słońce, gdy wschodzić będzie, a miesiąc nie wyda światła swego.
Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
11 I nawiedzę na okręgu ziemskim złość, a na niezbożnych nieprawości ich; i uczynię koniec pysze hardych, a hardość okrutników zniżę.
Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 Męża droższym uczynię nad szczere złoto, a człowieka nad złoto z Ofir.
Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 Dlatego zatrząsnę niebem, a poruszy się ziemia z miejsca swego w rozgniewaniu Pana zastępów, i w dzień popędliwego gniewu jego.
Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 I będzie jako łani przepłoszona, i jako trzoda, której nie ma kto zgromadzić; każdy się do ludu swego obróci, i każdy do ziemi swojej uciecze.
Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Ktokolwiek znaleziony będzie, przebity będzie; a każdy, którzy się kolwiek do nich przyłączy, od miecza polęże.
Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 Nadto i dziatki ich roztrącane będą przed oczyma ich; domy ich splundrowane będą, a żony ich pogwałcone będą.
Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 Oto Ja pobudzę przeciwko nim Medów, którzy o srebro nie będą dbali, a w złocie nie będą się kochali;
Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 Ale z łuków dziatki postrzelają, a nad płodem żywota nie zmiłują się, oko ich synom nie przepuści.
Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 I będzie Babilon, który był ozdobą królestw i sławą zacności Chaldejczyków, jako podwrócenie od Boga Sodomy i Gomory.
Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 Nie będą się w nim osadzać na wieki, ani mieszkać od narodu aż do narodu; ani tam rozbije namiotu Arabczyk, ani tam pasterze z stadami odpoczywać będą.
Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 Ale tam zwierz odpoczywać będzie, a domy ich bestyjami napełnione będą; i będą tam mieszkać sowy, a pokusy tam skakać będą.
Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 I będą się sobie ozywać straszne potwory na pałacach ich, a smoki na zamkach rozkosznych. A blisko tego że przyjdzie czas jego, a dni jego nie odwloką się.
Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.

< Izajasza 13 >