< Izajasza 12 >
1 I rzeczesz dnia onego: Wysławiać cię będę, Panie! przeto, że będąc rozgniewany na mię, odwróciłeś zapalczywość gniewu twego, a ucieszyłeś mię.
Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
2 Oto Bóg zbawienie moje, ufać będę, a nie ulęknę się; albowiem Pan, Bóg mój, jest mocą moją, i pieśnią moją, i zbawieniem mojem.
Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 I będziecie z radością czerpać wody ze zdrojów tegoż zbawienia.
Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 I rzeczecie dnia onego: Wysławiajcie Pana wzywajcie imienia jego, opowiadajcie między narodami sprawy jego, przypominajcie, że wysokie jest imię jego.
Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Śpiewajcie Panu, albowiem wielkie rzeczy uczynił; niech to będzie wiadomo po wszystkiej ziemi.
Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Wykrzykaj a śpiewaj, obywatelko Syońska! albowiem wielki jest w pośrodku ciebie Święty Izraelski.
Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”