< Izajasza 1 >

1 Widzenie Izajasza, syna Amosowego, które widział nad Judą i nad Jeruzalemem, za dni Ozeasza, Joatama, Achaza, i Ezechijasza, królów Judzkich.
Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
2 Słuchajcie niebiosa, a ty ziemio przyjmij w uszy swe! Albowiem Pan mówi: Synówem wychował i wywyższył; ale oni odstąpili odemnie.
Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
3 Zna wół gospodarza swego, i osieł żłób pana swego; ale Izrael mię nie zna, lud mój nie zrozumiewa.
Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
4 Biada narodowi grzesznemu, ludowi obciążonemu nieprawością, nasieniu złośliwych; synom skażonym! Opuścili Pana, do gniewu pobudzili świętego Izraelskiego, odwrócili się nazad.
Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
5 Przeczże tem więcej przyczyniacie przestępstwa, im więcej was biją? Wszystka głowa chora, i wszystko serce mdłe.
Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
6 Od stopy nogi aż do wierzchu głowy niemasz na nim nic całego; rana i siność, i rany zagniłe nie są wyciśnione, ani zawiązane, ani olejkiem odmiękczone.
Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
7 Ziemia wasza spustoszona, miasta wasze popalone ogniem. Ziemię waszę cudzoziemcy przed wami pożerają i pustoszą, jako zwykli cudzoziemcy.
Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
8 I została córka Syońska jako chłodnik na winnicy, jako budka w ogrodzie ogórczanym, i jako miasto zburzone.
Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
9 By nam był Pan zastępów nie zostawił trochy ostatków, bylibyśmy jako Sodoma, stalibyśmy się byli Gomorze podobnymi.
Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
10 Słuchajcie słowa Pańskiego, książęta Sodemscy! przyjmujcie w uszy zakon Boga naszego, ludzie Gomorscy!
Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
11 Cóż mi po mnóstwie ofiar waszych? mówi Pan. Jużem syty całopalenia baranów, i łoju tłustego bydła; a krwi cielców, i baranków, i kozłów nie pragnę.
Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
12 Gdy przychodzicie, abyście się okazywali przed twarzą moją, któż tego żądał z rąk waszych, abyście deptali sieni moje?
Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
13 Nie ofiarujcież więcej ofiary daremnej. Kadzenie jest mi obrzydłością; nowiu miesiąca i sabatu, gdy zwoływacie zgromadzenia, nie mogę ścierpieć (bo nieprawością jest) ani dnia zapowiedzianego.
Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
14 Nowych miesięcy waszych, i uroczystych świąt waszych nienawidzi dusza moja; stały mi się ciężarem; upracowałem się nosząc je.
Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
15 Przetoż gdy wyciągniecie ręce wasze, skryję oczy moje przed wami; a gdy rozmnożycie modlitwę, nie wysłucham; bo ręce wasze krwi są pełne.
Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
16 Omyjcie się, czystymi bądźcie, odejmijcie złość uczynków waszych od oczów moich; przestańcie źle czynić.
sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
17 Uczcie się dobrze czynić; szukajcie sądu, podźwignijcie uciśnionego, sąd czyńcie sierocie, ujmujcie się o krzywdę wdowy.
phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
18 Przyjdźcież teraz, a rozpierajmy się z sobą, mówi Pan: Choćby były grzechy wasze jako szarłat, jako śnieg zbieleją; choćby były czerwone jako karmazyn, jako wełna białe będą.
Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
19 Będziecieli powolni, a posłuchacie mię, dóbr ziemi pożywać będziecie.
Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
20 Lecz jeźli nie będziecie posłusznymi, ale odpornymi, od miecza pożarci będziecie; bo usta Pańskie mówiły.
koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
21 Jakoć się stało nierządnicą to miasto wierne, pełne sądu? Sprawiedliwość mieszkała w niem; lecz teraz mężobójcy.
Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22 Srebro twoje obróciło się w żużeł; wino twoje pomięszało się z wodą.
Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23 Książęta twoi są uporni, i towarzysze złodziei; każdy z nich miłuje dary, a jadą za nagrodą; sierocie nie czynią sprawiedliwości, a sprawa wdowy nie przychodzi przed nich.
Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
24 Przetoż mówi Pan, Pan zastępów, możny Izraelski: Oto ucieszę się nad nieprzyjaciółmi moimi, a pomszczę się nad przeciwnikami swymi.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
25 I obrócę rękę moję na cię, a wypalę aż do czysta zużelicę twoję, i odpędzę wszystkę cenę twoję.
Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26 A przywrócę sędziów twoich, jako przedtem byli, i radców twoich, jako na początku. Potem cię nazywać będą miastem sprawiedliwości, miastem wiernem.
Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
27 Syon w sądzie okupione będzie, a ci, co się do niego nawrócą, w sprawiedliwości.
Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
28 Ale przewrotnicy i grzesznicy wespół starci będą, a ci, co opuścili Pana, zniszczeją.
Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
29 Albowiem zawstydzeni będziecie dla gajów, którycheście pożądali; i pohańbieni dla ogrodów, któreście sobie obrali.
“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
30 Gdy się staniecie jako dąb, z którego liście opadły, a jako ogród, w którym wody niemasz.
Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31 I będzie mocarz jako zgrzebia, a ten, który go uczynił, jako iskra; i zapalą się oboje pospołu, a nie będzie, ktoby zagasił.
Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”

< Izajasza 1 >