< Ozeasza 1 >

1 Słowo Pańskie, które się stało do Ozeasza, syna Berowego, za dni Uzyjasza, Joatama, Achaza, Ezechyjasza, królów Judzkich, i za dni Jeroboama, syna Joazowego, króla Izraelskiego.
Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
2 Gdy począł Pan mówić do Ozeasza, rzekł Pan do Ozeasza: Idź, pojmij sobie żonę wszetecznicę, i spłódź dzieci z wszeteczeństwa; bo się ta ziemia, bez wstydu wszeteczeństwo płodząc, od Pana odwróciła.
Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
3 Odszedł tedy, i pojął Gomorę, córkę Dyblaimską, która poczęła i porodziła mu syna.
Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
4 I rzekł Pan do niego: Nazów imię jego Jezreel: bo jeszcze po małym czasie nawiedzę krew Jezreel nad domem Jehu, a sprawię to, że ustanie królestwo domu Izraelskiego.
Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
5 A dnia onego złamię łuk Izraelski w dolinie Jezreel.
Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
6 I poczęła znowu i porodziła córkę; i rzekł mu Pan: Nazów imię jej Loruchama; bo się więcej nie zmiłuję nad domem Izraelskim, lecz ich zapewne wygładzę.
Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
7 Ale nad domem Judzkim zmiłuję się, i wybawię ich przez Pana, Boga ich, a nie wybawię ich przez łuk, i przez miecz, i przez wojnę, i przez konie i przez jezdnych.
Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
8 Potem ostawiwszy Loruchamę znowu poczęła i porodziła syna.
Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
9 I rzekł Pan: Nazów imię jego Loami; boście wy nie ludem moim, a Ja też nie będę waszym.
Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
10 Wszakże liczba synów Izraelskich będzie jako piasek morski, który ani zmierzony ani zliczony być może; i stanie się, że miasto tego, co im rzeczono: Nie jesteście wy ludem moim, rzeczono im będzie: Wyście synami Boga żyjącego.
“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
11 I będą zgromadzeni synowie Judzcy i synowie Izraelscy wespół, a postanowiwszy nad sobą głowę jednę, wynijdą z tej ziemi; bo będzie wielki dzień Jezreela.
Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”

< Ozeasza 1 >