< Ozeasza 3 >

1 I rzekł Pan do mnie: Jeszcze idź, a rozmiłuj się niewiasty umiłowanej od innego, a cudzołożnicy, tak jako miłuje Pan synów Izraelskich, choć się oni oglądają na cudzych bogów, a miłują fasy wina.
Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
2 I kupiłem ją sobie za piętnaście srebrników i za półtora homera jęczmienia;
Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
3 I rzekłem do niej: Siedź mi tak przez wiele dni, a nie płódź wszeteczeństwa, ani chodź za mąż, a ja też dla ciebie.
Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
4 Bo przez wiele dni będą synowie Izraelscy bez króla i bez książęcia, i bez ofiary i bez bałwana, i bez Efodu i bez Terafim.
Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
5 A potem nawrócą się synowie Izraelscy i szukać będą Pana, Boga swego, i Dawida, króla swego, a przestraszeni będąc pójdą do Pana i do dobrotliwości jego w ostatnie dni.
Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.

< Ozeasza 3 >