< Ozeasza 2 >

1 Mówcie braciom waszym, o ludu mój! i siostrom waszym, o ty, coś miłosierdzia dostąpiła!
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 Rozpierajcie się z matką waszą, rozpierajcie się; bo ona nie jest żoną moją, a Jam też nie jest mężem jej, póki nie odejmie wszeteczeństw swoich od oblicza swego, a cudzołóstw swych z pośród piersi swoich;
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 Bym jej snać nago nie zewlekł a nie postawił jej, jaką była w dzień narodzenia swego, i nie uczynił jej jako pustynia, i nie zostawił jej jako ziemia sucha, i nie umorzył jej pragnieniem:
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 I nad synami jej nie zmiłowałbym się, przeto, że są synami z wszeteczeństwa,
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 Bo wszeteczeństwo płodzi matka ich, sprosność czyni rodzicielka ich; bo mówiła: Pójdę za miłośnikami moimi, którzy mi dodawają chleba mego, i wody mojej, wełny mojej, i lnu mego, oliwy mojej i napojów moich.
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Przetoż oto Ja zagrodzę cierniem drogę jej, a ugrodzę płot, aby ścieżek swoich nie znalazła.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 Tedy biegać będzie za miłośnikami swymi, wszakże ich nie dogoni; i szukać ich będzie, ale nie znajdzie. Tedy rzecze: Pójdę a wrócę się do męża swego pierwszego; bo mi lepiej było na on czas, niżeli teraz.
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 Bo ona nie wie tego, żem Ja dawał jej zboże, i moszcz, i oliwę; nawet dawałem jej obfitość srebra i złota, które oni obracają na Baala.
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 Dlatego wrócę się, i zabiorę zboże moje czasu jego, i moszcz mój czasu jego, i odbiorę jej wełnę moję, i len mój dany na okrywanie nagości jej.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 A teraz odkryję sprosność jej przed oczyma miłośników jej, a nikt jej nie wyrwie z ręki mojej.
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 I uczynię koniec wszystkiemu weselu jej, świętom jej, nowym miesiącom jej, i sabatom jej, i wszystkim uroczystym świętom jej.
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 Popustoszę też winne macice jej i figowe drzewa jej, przeto, że mówi: Moja to zapłata, którą mi dali miłośnicy moi; i obrócę je w lasy, a pożrą je zwierzęta polne.
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 I nawiedzę na niej dni Baalowe, w które im kadzi, a strojąc się w nausznice swoje i w klejnoty swoje, chodzi za miłośnikami swymi, ale mnie zapomina, mówi Pan.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 Przetoż oto Ja nią łudzić będę, gdy ją wywiodę na puszczę, a łaskawie z nią mówić będę;
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 I dam jej winnice jej od tegoż miejsca, i dolinę Achor, miasto drzwi nadziei; i będzie tam śpiewała, jako za dni młodości swojej, to jest, jako w dzień, którego wychodziła z ziemi Egipskiej.
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 A dnia onego mówi Pan, będziesz mię zwała: Mężu mój! a nie będziesz mię więcej zwała: Baalu mój!
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 Bo odejmę imiona Baalów od ust twoich, że ani wspominani będą więcej imieniem swojem.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 I uczynię dla ciebie przymierze dnia onego z zwierzem polnym, i z ptastwem niebieskiem i z płazem ziemskim, a łuk i miecz pokruszę, i wojnę z ziemi zniosę, i sprawię, że bezpiecznie mieszkać będą.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 I poślubię cię sobie na wieki: poślubię cię, mówię, sobie w sprawiedliwości i w sądzie i w miłosierdziu i w litościach;
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 Poślubię cię też sobie w wierze, i poznasz Pana.
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 Dnia onego wysłucham, mówi Pan, wysłucham, mówi, niebiosa, a one wusłuchają ziemię;
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 A ziemia wysłucha zboże i moszcz i oliwę, a te rzeczy wysłuchają Jezreela.
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 Bo ją sobie rozsieję na ziemi, a zmiłuję się nad tą, co była w niełasce, i rzekę do tego, co nie był ludem moim: Tyś jest lud mój! a on rzecze: Tyś jest Bóg mój.
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”

< Ozeasza 2 >