< Ozeasza 10 >

1 Izrael jest macicą próżną, owoc przynosi sobie; czem więcej miewał owocu swego, tem więcej nabudował ołtarzów; a czem obfitsza jest ziemia jego, tem więcej nastawiał obrazów.
Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 Rozdziela się serce ich, przetoż winnymi są; on pokruszy ołtarze ich, i obrazy ich popsuje.
Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 Ponieważ mówią: Nie mamy króla, nawet nie boimy się Pana, a król nam co uczyni?
Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 Mówią słowa, przysięgając kłamliwie, gdy czynią przymierze; i wzrośnie sąd jako jad na zagonach polnych.
Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 Dla jałowic Bet Aweńskich zatrwożą się obywatele Samaryjscy, gdy kwilić będą nad nim, lud jego, i popije go, (którzy się więc radowali z niego) przeto, że sława jego odchodzi od niego.
Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 Nawet i sam do Assyryi zaprowadzony będzie za dar królowi Jareb; zawstydzi się Efraim, i zasroma się Izrael za radę swoję.
Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 Wycięty będzie król Samaryjski, jako piana na wierzchu wody.
Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 I będą wyżyny Awenu wytracone, grzech Izraelski; ciernie i oset wyrośnie na ołtarzach ich; a rzekną górom: Przykryjcie nas; a pagórkom: Upadnijcie na nas.
Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 Ode dni Gabaa grzeszyłeś, Izraelu! tam się ostali, nie zachwyciła ich w Gabaa bitwa przeciwko synom nieprawości podniesiona.
“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
10 Przetoż ich pokarzę według upodobania mego; bo się zbiorą na nich narody, aby byli karani dla dwojakich nieprawości swoich.
Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 Bo Efraim jest jako jałowica wyuczona, kocha się w młóceniu, chociażem Ja następował na cudny kark jej, abym do jazdy używał Efraima, Juda aby orał, a Jakób aby włóczył.
Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 I mówiłem: Siejcie sobie ku sprawiedliwości; żnijcie ku miłosierdziu, orzcie sobie nowinę; bo czas jest szukać Pana, aż przyjdzie, i spuści na was sprawiedliwość jako deszcz.
Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 Aleście orali niepobożność, żęliście nieprawość, jedliście owoc kłamstwa; albowiem ufasz w drodze swej i w mnóstwie mocarzów twoich.
Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 Dlategoż powstanie rozruch między ludem twoim, a wszystkie zamki twoje poburzone będą, tak jako poburzył Salman Bet Arbel w dzień bitwy; matki z synami roztrącone będą.
phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 Oto tak wam uczyni Betel dla wielkiej złości waszej; król Izraelski na świtaniu do szczętu zgładzony będzie.
Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

< Ozeasza 10 >