< Hebrajczyków 10 >

1 Albowiem zakon mając cień przyszłych dóbr, a nie sam obraz rzeczy, jednakiemiż ofiarami, które na każdy rok ustawicznie ofiarują, nigdy nie może tych, którzy do nich przystępują, doskonałymi uczynić.
Malamulo ndi chithunzithunzi cha zinthu zabwino zimene zikubwera, osati madalitso enieniwo. Pa chifukwa chimenechi sizingatheke konse kuti nsembe zimodzimodzi, zoperekedwa kawirikawiri, kosalekeza ndi chaka ndi chaka, kuti nʼkusandutsa angwiro amene amabwera kudzapembedza.
2 Bo inaczej przestano by ich było ofiarować, przeto żeby już nie mieli żadnego sumienia o grzechy ci, którzy ofiarują, będąc raz oczyszczeni.
Ngati zikanamatero iwowo akanasiya kupereka nsembezo. Pakuti opembedzawo akanamayeretsedwa kamodzi kokha, sibwenzi chikumbumtima chawo chikuwatsutsabe chifukwa cha machimo awo.
3 Ale przy tych ofiarach dzieje się przypomnienie grzechów na każdy rok.
Koma nsembezo zimawakumbutsa anthuwo machimo awo chaka ndi chaka.
4 Albowiem nie można rzec, aby krew wołów i kozłów miała gładzić grzechy.
Chifukwa nʼkosatheka kuti magazi angʼombe yayimuna ndi mbuzi yayimuna achotse machimo.
5 Przetoż wchodząc na świat, mówi: Ofiary i obiaty nie chciałeś, aleś mi ciało sposobił.
Nʼchifukwa chake Khristu atabwera pa dziko lapansi anati, “Simunafune nsembe kapena zopereka, koma thupi munandikonzera.
6 Całopalenia i ofiary za grzech nie upodobałyć się.
Simunakondwere nazo nsembe zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo.
7 Tedym rzekł: Oto idę (na początku księgi napisano o mnie), abym czynił, o Boże! wolę twoję;
Tsono, Ine ndinati, ‘Ndili pano Ine, Inu Mulungu, ndabwera kudzachita zimene mukufuna monga zinalembedwa mʼMalemba.’”
8 Powiedziawszy wyżej: Żeś ofiary i obiaty, i całopalenia za grzech nie chciał, ani sobie upodobał, (które według zakonu bywają ofiarowane).
Poyamba Iye anati, “Nsembe kapena zopereka zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo, Inu simunazifune kapena kukondwera nazo.” Ngakhale kuti Malamulo ndiye amanena kuti ziperekedwe.
9 Tedy rzekł: Oto idę, abym czynił, o Boże wolę twoję; znosi pierwsze, aby wtóre postanowił.
Pamenepo Iye anati, “Ndili pano Ine, ndabwera kudzachita zimene mukufuna.” Khristu anachotsa nsembe zoyamba zija kuti mʼmalo mwake ayikemo nsembe za mtundu wachiwiri.
10 Przez którą wolę jesteśmy poświęceni przez ofiarę ciała Jezusa Chrystusa raz uczynioną.
Chifukwa chakuti Yesu Khristu anachita zimene Mulungu anafuna kuti achite, ndife oyeretsedwa ndi nsembe ya thupi lake, limene analipereka kamodzi kokha.
11 A wszelkić kapłan stoi na każdy dzień, służbę Bożą odprawując, a jednakież ofiary częstokroć ofiarując, które nigdy grzechów zgładzić nie mogą.
Wansembe aliyense amayimirira tsiku ndi tsiku nʼkutumikira, ndipo amapereka nsembe imodzimodzi mobwerezabwereza, nsembe zimene sizingathe kuchotsa machimo.
12 Lecz ten jednę ofiarę ofiarowawszy za grzechy, na wieki siedzi na prawicy Bożej,
Koma pamene wansembe uyu anapereka kamodzi kokha nsembe imodzi yokha chifukwa cha machimo, Iye anakhala pansi ku dzanja lamanja la Mulungu.
13 Na koniec oczekując, ażby położeni byli nieprzyjaciele jego podnóżkiem nóg jego.
Kumeneko akudikira tsono kuti Mulungu asandutse adani ake kukhala chopondapo mapazi ake.
14 Albowiem jedną ofiarą doskonałymi uczynił na wieki tych, którzy bywają poświęceni.
Chifukwa cha nsembe imodzi Iye anasandutsa angwiro kwamuyaya iwo amene akuwayeretsa.
15 A świadczy nam to i sam Duch Święty; albowiem powiedziawszy pierwej:
Mzimu Woyera nayenso akuchitira umboni za zimenezi kwa ife. Poyamba Iye anati,
16 Toć jest przymierze, które postanowię z nimi po onych dniach, mówi Pan: Dam prawa moje do serca ich, a na myślach ich napiszę je.
“Ili ndi pangano limene ndidzachita nawo atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika malamulo anga mʼmitima mwawo, ndipo ndidzawalemba mʼmaganizo mwawo.”
17 A grzechów ich i nieprawości ich nie wspomnę więcej:
Ndipo akutinso: “Sindidzakumbukiranso konse machimo awo ndi zolakwa zawo.”
18 A gdzieć jest odpuszczenie ich, jużci więcej ofiary nie potrzeba za grzech.
Ndipo pamene machimo akhululukidwa, sipafunikanso nsembe yoperekedwa chifukwa cha machimowo.
19 Mając tedy, bracia! wolność, wnijść do świątnicy przez krew Jezusową,
Ndipo tsono abale, molimba mtima timalowa mʼMalo Opatulika kwambiri chifukwa cha magazi a Yesu.
20 (Drogą nową i żywą, którą nam poświęcił przez zasłonę, to jest przez ciało swoje.)
Iye anatitsekulira njira yatsopano ndi yamoyo kudutsa chinsalu chotchinga, chimene ndi thupi lake.
21 I kapłana wielkiego nad domem Bożym;
Ndiponso tili ndi wansembe wamkulu woyangʼanira nyumba ya Mulungu.
22 Przystąpmyż z prawdziwem sercem w zupełności wiary, mając oczyszczone serca od sumienia złego,
Tsono tiyeni tiyandikire kwa Mulungu ndi mtima woona ndi wodzaza ndi chikhulupiriro. Popeza mitima yathu yayeretsedwa, ndi yopanda chikumbumtima chotitsutsa, ndiponso matupi athu asambitsidwa ndi madzi woyera.
23 I omyte ciało wodą czystą, trzymajmy wyznanie nadziei niechwiejące się; (boć wierny jest ten, który obiecał; )
Tiyeni tigwiritsitse mosagwedezeka zimene timaziyembekezera ndi kuzivomereza, pakuti amene anatilonjezayo ndi wokhulupirika.
24 I przypatrujmy się jedni drugim ku pobudzaniu się do miłości i do dobrych uczynków,
Tiziganizira mmene tingalimbikitsirane wina ndi mnzake pokondana ndi kuchita ntchito zabwino.
25 Nie opuszczając społecznego zgromadzenia naszego, jako niektórzy obyczaj mają, ale napominając jedni drugich, a to tem więcej, czem więcej widzicie, iż się on dzień przybliża.
Tiyeni tisaleke kusonkhana kwathu pamodzi monga mmene ena amachitira, koma tizilimbikitsana makamaka poona kuti tsiku la Ambuye layandikira.
26 Albowiem jeźlibyśmy dobrowolnie grzeszyli po wzięciu znajomości prawdy, nie zostawałaby już ofiara za grzechy;
Ngati ife tipitirira kuchimwa mwadala pamene tikudziwa choona, palibenso nsembe ina imene ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.
27 Ale straszliwe niejakie oczekiwanie sądu i zapalenie ognia, który pożreć ma przeciwników.
Koma kumangodikira kokha ndi mantha chiweruzo ndiponso moto woopsa umene udzawononga adani a Mulungu
28 Kto by odrzucił zakon Mojżeszowy, bez miłosierdzia za świadectwem dwóch albo trzech umiera.
Aliyense amene amakana malamulo a Mose amaphedwa popanda nʼchifundo chomwe, malingana pali mboni ziwiri kapena zitatu.
29 Co się wam zda? Jakoż sroższego karania godzien jest ten, kto by Syna Bożego podeptał i krew przymierza, przez którą był poświęcony, za pospolitą miał, i Ducha łaski zelżył?
Koposa kotani nanga ululu wachilango chimene adzalandire munthu amene amapeputsa Mwana wa Mulungu, amene amayesa magazi a pangano, amene anamuyeretsa, kukhala chinthu chodetsedwa, ndi kunyoza Mzimu wachisomo?
30 Albowiem znamy tego, który powiedział: Mnie pomsta, Ja oddam, mówi Pan; i zasię: Pan sądzić będzie lud swój.
Pakuti timadziwa amene anati, “Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.” Iye anatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.”
31 Strasznać rzecz jest wpaść w ręce Boga żywego.
Nʼchinthu choopsa kugwa mʼmanja a Mulungu wamoyo.
32 Wspomnijcie na dni pierwsze, w których będąc oświeceni, znosiliście wielki bój utrapienia,
Kumbukirani masiku akale aja mutangowunikiridwa chatsopano, pa nthawi imeneyi munapirira zowawa zambiri.
33 Lubo to, gdyście byli i urąganiem, i utrapieniem na podziw wystawieni lub też gdyście się stali uczestnikami tych, z którymi się tak obchodzono.
Nthawi zina ankakunyozani pagulu ndi kukuzunzani. Nthawi zina munkamva zowawa pamodzi ndi amene ankasautsidwa chotere.
34 Albowiemeście i z więzienia mego ze mną utrapieni byli i rozchwycenie majętności waszych przyjęliście z radością, wiedząc, że macie w sobie lepszą majętność w niebie, i trwającą.
Munkawamvera chisoni amene anali mʼndende ndiponso munkalola mokondwera kuti akulandeni katundu wanu chifukwa munkadziwa kuti muli nacho chuma choposa ndi chosatha.
35 Przetoż nie odrzucajcie ufności waszej, która ma wielką zapłatę.
Tsono musataye kulimbika mtima kwanuko pakuti mudzalandira nako mphotho yayikulu.
36 Albowiem cierpliwości wam potrzeba, abyście wolę Bożą czyniąc, odnieśli obietnicę.
Nʼkofunika kuti mupirire kuti pamene muchita chifuniro cha Mulungu mudzalandire zimene Iye analonjeza.
37 Boć jeszcze bardzo, bardzo maluczko, a oto ten, który ma przyjść, przyjdzie, a nie omieszka.
Pakuti nʼkanthawi kochepa chabe, Iye amene akubwera adzabwera ndipo sadzachedwa ayi.
38 A sprawiedliwy z wiary żyć będzie; a jeźliby się kto schraniał, nie kocha się w nim dusza moja.
Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro. Ndipo ngati iye abwerera mʼmbuyo chifukwa cha mantha, Ine sindidzakondwera naye.
39 Lecz my nie jesteśmy z tych, którzy się schraniają ku zginieniu, ale z tych, którzy wierzą ku pozyskaniu duszy.
Koma ife sindife amodzi a iwo obwerera mʼmbuyo mwa mantha ndi owonongedwa, koma ndife amodzi a amene akukhulupirira ndi wopulumutsidwa.

< Hebrajczyków 10 >