< Aggeusza 1 >

1 Roku wtórego Daryjusza króla, miesiąca szóstego, dnia pierwszego tegoż miesiąca, stało się słowo Pańskie przez Aggieusza proroka do Zorobabela, syna Salatyjelowego, książęcia Judzkiego, i do Jesuego, syna Jozedekowego, kapłana najwyższego, mówiąc:
Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
2 Tak powiada Pan zastępów, mówiąc: Ten lud mówi: Jeszcze nie przyszedł czas, czas budowania domu Pańskiego.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
3 Przetoż się stało słowo Pańskie przez Aggieusza proroka, mówiąc:
Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
4 Izali wam jest czas, abyście mieszkali w domach waszych listwowanych, a dom ten aby pusty stał?
“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
5 Teraz tedy tak mówi Pan zastępów: Uważajcież, jako się wam powodzi;
Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
6 Siejecie wiele, a mało zbieracie; jecie, ale się nie nasycacie; pijecie, ale nie ugaszacie pragnienia; obłóczycie się, ale się nikt nie może zagrzać, a ten, co sobie zapłatę zgromadza, zgromadza ją do worka dziurawego.
Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
7 Tak mówi Pan zastępów: Uważajcie, jako się wam powodzi;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
8 Wstąpcie na tę górę, i zwoźcie drzewo; budujcie ten dom, a zakocham się w nim, i będę uwielbiony, mówiPan.
Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
9 Poglądacie na wiele, a oto, mało dostawacie, a co wnosicie do domu, to Ja rozdmuchywam; dlaczego? mówi Pan zastępów; dlatego, że dom mój jest pusty, a międzytem się każdy z was stara o dom swój.
“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
10 Przetoż się nad wami niebo zawarło, aby rosy nie dawało; ziemia także zawarła się, aby nie wydawała urodzaju swego.
Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
11 A tak przyzwałem suszę na tę ziemię, i na te góry, i na pszenicę, i na moszcz, i na oliwę, i na to, coby miała wydać ziemia, i na ludzi i na bydło, i na wszystkę pracę ręczną.
Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
12 Tedy usłuchał Zorobabel, syn Salatyjelowy, i Jesua, syn Jozedekowy, kapłan najwyższy, i wszystkie ostatki ludu, głosu Pana, Boga swego, i słów Aggieusza proroka, ponieważ go posłał Pan, Bóg ich; bo się lud bał oblicza Pańskiego.
Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
13 Tedy Aggieusz, poseł Pański, rzekł do ludu, będąc w poselstwie Pańskiem, mówiąc: Jam z wami, mówi Pan.
Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
14 Wtem wzbudził Pan ducha Zorobabela, syna Salatyjelowego, książęcia Judzkiego, i ducha Jesuego, syna Jozedekowego, kapłana najwyższego, i ducha ostatków wszystkiego ludu, że przyszedłszy robili około domu Pana zastępów, Boga swego.
Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
15 Dnia dwudziestego i czwartego, miesiąca szóstego, roku wtórego Daryjusza króla;
pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

< Aggeusza 1 >