< Habakuka 1 >
1 Brzemię, które widział prorok Abakuk.
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 Dokądże wołać będę, o Panie! a nie wysłuchasz? Dokądże do ciebie przed gwałtem krzyczeć będę, a nie wybawisz?
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Przeczże dopuszczasz, abym patrzył na nieprawość, i widział bezprawie, i zgubę, i gwałt przeciwko sobie? i przecz się znajduje ten, który swar i niezgodę roznieca?
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 Dlatego naruszony bywa zakon, a prawu się nigdy dosyć nie dzieje; albowiem niepobożny otacza sprawiedliwego, dlatego wychodzi sąd przewrotny.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 Spojrzyjcie na narody a obaczcie i dziwujcie się z zdumieniem, przeto, iż czynię nieco za dni waszych, o czem gdy wam powiadać będą, nie uwierzycie.
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 Albowiem oto Ja wzbudzę Chaldejczyków, naród srogi i prędki, który szeroko pójdzie przez ziemię, aby posiadł mieszkania cudze.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 Straszny jest i ogromny; od niego samego wynijdzie sąd jego, i wywyższenie jego.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 Konie jego prędsze będą niż lamparty, a sroższe nad wilki wieczorne; szeroko rozciągną się jezdni jego, a jezdni jego z daleka przyjdą, przylecą jako orzeł spieszący się do żeru.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 Każdy z nich dla łupiestwa przyjdzie; obrócą twarze swoje na wschód słońca, a więźniów zgromadzą jako piasek.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 Ten i z królów szydzić będzie, a książęta będą na pośmiech u niego; ten też z każdej twierdzy naśmiewać się będzie, a usypawszy wały weźmie ją.
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Tedy się odmieni duch jego, a wystąpi i przewini, myśląc, że ta moc jego jest boga jego.
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 Izaliś ty nie jest od wieku, Panie, Boże mój, święty mój? myć nie pomrzemy; o Panie! postawiłeś go na sąd; ty, o skało nasza! na karanieś go ugruntował.
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 Czyste są oczy twoje, tak, że na złe patrzyć i bazprawia widzieć nie mogą; przeczżebyś miał patrzyć na czyniących przewrotność? Przeczżebyś miał milczeć, ponieważ niezbożnik pożera sprawiedliwszego niżeli sam?
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 Miałżebyś zaniechać ludzi jako ryb morskich, jako płazu, który nie ma pana?
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 Wszystkie wędą wyciąga, zagarnia je niewodem swoim, i zgromadza je do sieci swoich; dlategoż się weseli i raduje.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 Przeto ofiaruje niewodowi swemu i kadzi sieci swojej; albowiem przez nie utył dział jego, a pożywienie jego hojniejsze.
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Izali dlatego będzie zapuszczał niewód swój, a ustawicznie zabijał narody bez litości?
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?