< Rodzaju 45 >
1 Tedy się Józef nie mógł dalej wstrzymać przed wszystkimi, którzy stali przed nim, i zawołał: Wyprowadźcie wszystkie ode mnie. I nie został nikt przy nim, gdy się dał poznać Józef braci swej.
Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake.
2 I podniósł głos swój z płaczem; co słyszeli Egipczanie, słyszał też dom Faraonów.
Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
3 I rzekł Józef do braci swej: Jamci jest Józef; a żywże jeszcze ojciec mój? i nie mogli mu bracia jego odpowiedzieć, bo się zlękli oblicza jego.
Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.
4 Tedy rzekł Józef do braci swej: Przystąpcie, proszę, do mnie; i przystąpili. Zatem rzekł: Jam jest Józef, brat wasz, któregoście sprzedali do Egiptu.
Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!
5 Jednak teraz nie frasujcie się, ani trwożcie sobą, żeście mię tu sprzedali; boć dla zachowania żywota waszego posłał mię Bóg przed wami.
Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu.
6 Bo już dwa lata głodu było na ziemi, a jeszcze pięć lat zostaje, których nie będą orać ani żąć.
Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola.
7 Posłał mię tedy Bóg przed wami, abym was zachował ostatek na ziemi, a żebym wam dodał żywności na oswobodzenie wielkie.
Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.
8 Teraz tedy nie wyście mię tu posłali, ale Bóg, który mię postanowił ojcem Faraonowym, i panem wszystkiego domu jego, a panującym nad wszystką ziemią Egipską.
“Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine.
9 Spieszcież się, a idźcie do ojca mego, i mówcie do niego: Toć wskazuje syn twój Józef: Uczynił mię Bóg panem wszystkiego Egiptu, przyjedźże do mnie, a nie omieszkaj.
Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe.
10 I będziesz mieszkał w ziemi Gosen; a będziesz blisko mnie, ty i synowie twoi, i synowie synów twoich, i trzody twoje, i woły twoje, i wszystko, co masz.
Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine.
11 A będę cię tam żywił; bo jeszcze pięć lat głodu będzie, abyś od niedostatku nie zginął, ty, i dom twój, i wszystko, co masz.
Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’
12 A oto, oczy wasze widzą, i oczy brata mego, Benjamina, że usta moje mówią do was.
“Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu.
13 Oznajmijcie też ojcu memu wszystkę zacność moje w Egipcie, i wszystko coście widzieli; spieszcie się tedy, a przyprowadźcie tu ojca mojego.
Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”
14 Zatem padł na szyję Benjamina, brata swego, i płakał; Benjamin też płakał na szyi jego.
Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira.
15 I pocałowawszy wszystkę bracią swoję, płakał nad nimi; a potem rozmawiali z nim bracia jego.
Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.
16 I rozgłoszono tę wieść w domu Faraonowym, mówiąc: Przyjechali bracia Józefowi; i podobało się to w oczach Faraonowych, i w oczach sług jego.
Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera.
17 Tedy rzekł Farao do Józefa: Powiedz braci swej: Uczyńcie tak: nakładłszy brzemion na bydła wasze, idźcie; a wróćcie się do ziemi Chananejskiej;
Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani.
18 A wziąwszy ojca waszego, i czeladź waszę, przyjedźcie do mnie; i dam wam dobre miejsce w ziemi Egipskiej, i będziecie używać tłustości ziemi.
Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’”
19 I rozkaż im mówiąc: To uczyńcie: weźmijcie sobie z ziemi Egipskiej wozów, dla dziatek waszych i dla żon waszych, a wziąwszy ojca waszego przyjedźcie tu.
“Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno.
20 A oko wasze niech nie żałuje sprzętu waszego, gdyż dobro wszystkiej ziemi Egipskiej wasze będzie.
Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’”
21 Uczynili tedy tak synowie Izraelowi; i dał im Józef wozy według rozkazania Faraonowego; dał im też żywności na drogę.
Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.
22 Dał z onychże wszystkich każdemu odmienne szaty; ale Benjaminowi dał trzy sta srebrników, i pięcioro szat odmiennych.
Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu.
23 Ojcu też swemu posłał te rzeczy: dziesięć osłów, niosących z najlepszych rzeczy Egipskich, i dziesięć oślic, niosących zboże, i chleb, i żywność ojcu jego na drogę.
Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake.
24 Puścił tedy bracią swą, i odjechali, a mówił do nich: Nie wadźcie się na drodze.
Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”
25 Którzy wyjechawszy z Egiptu przyjechali do ziemi Chananejskiej, do Jakóba ojca swego.
Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani.
26 I oznajmili mu, mówiąc: Jeszczeć żyw Józef, a onci jest panem nad wszystką ziemią Egipską; i zemdlało serce jego; bo im nie wierzył.
Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira.
27 Lecz oni powiedzieli mu wszystkie słowa Józefowe, które mówił do nich. A ujrzawszy wozy, które posłał Józef, aby go na nich przywieziono, tedy ożył duch Jakóba, ojca ich.
Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka.
28 I rzekł Izrael: Dosyć mam na tem, gdy jeszcze Józef, syn mój, żyje; pójdę a oglądam go, pierwej niż umrę.
Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”