< Rodzaju 44 >

1 Rozkazał tedy Józef temu, który był sprawcą domu jego, mówiąc: Napełnij wory mężów tych zbożem, jako mogą znieść, a włóż pieniądze każdego na wierzch woru jego.
Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
2 Kubek też mój, kubek srebrny, włóż na wierzch woru młodszego z pieniędzmi za zboże jego; i uczynił według słów Józefowych, jako mu rozkazał.
Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
3 A gdy było rano, mężowie oni puszczeni są, sami i osłowie ich.
Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
4 Wyszedłszy tedy z miasta, gdy nie daleko byli, rzekł Józef do tego, który był sprawcą domu jego: Wstań, goń te męże, a dogoniwszy ich, mów do nich: Czemuście oddali złe za dobre?
Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
5 Azaż nie ten jest kubek, z którego pija pan mój? i azaż on pewnie nie zgadnie przezeń, jacyście wy? źleście uczynili, coście uczynili.
Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
6 Dogoniwszy ich tedy, mówił do nich te słowa.
Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
7 Ale oni odpowiedzieli mu: Czemu mówi pan mój takowe słowa? nie daj tego Boże, aby to słudzy twoi uczynić mieli.
Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
8 Oto pieniądze, któreśmy byli znaleźli na wierzchu worów naszych, odnieśliśmy zaś do ciebie z ziemi Chananejskiej; a jakoż byśmy kraść mieli z domu pana twego srebro albo złoto?
Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
9 U którego by to znaleziono z sług twoich, niechaj umrze; a my będziemy pana mego niewolnikami.
Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
10 Tedy on rzekł: Niechże tak będzie, jako mówicie; jednak przy którym się znajdzie kubek, ten niech będzie niewolnikiem, a wy będziecie niewinnymi.
Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
11 Prędko tedy każdy złożył wór swój na ziemię; i rozwiązali każdy wór swój.
Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
12 I szukał od starszego począwszy; a u młodszego przestał; i znalazł kubek w worze Benjaminowym.
Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
13 Tedy oni rozdarli szaty swoje, i włożywszy brzemię każdy z nich na osła swego, wrócili się do miasta.
Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
14 Przyszedł tedy Judas, i bracia jego do domu Józefa, który tam jeszcze był, i upadli przed obliczem jego na ziemię.
Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
15 I rzekł do nich Józef: Cóżeście to uczynili? azaście nie wiedzieli, że pewnie zgadnie mąż taki, jakim ja jest?
Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
16 Tedy odpowiedział Judas: Cóż odpowiemy panu memu, cóż rzeczemy? i jako się my usprawiedliwić mamy? Bóg znalazł nieprawość sług twoich; otośmy niewolnikami pana mego, i my, i ten, w którego ręku znaleziony jest kubek.
Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
17 A on rzekł: Nie daj Boże, abym to uczynić miał! mąż, w którego ręku znaleziony jest kubek, ten będzie niewolnikiem moim; a wy jedźcie w pokoju do ojca waszego.
Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
18 Zatem przystąpił do niego Judas i rzekł: Słuchaj mię panie mój; niechaj przemówi proszę sługa twój które słowo w uszy pana mego, a niech się nie zapala gniew twój na sługę twego, gdyżeś ty jest jako sam Farao.
Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
19 Pan mój pytał sług swoich mówiąc: Macież ojca albo brata?
Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
20 Tedyśmy odpowiedzieli panu swemu: Mamyć ojca starego, i chłopię w starości jego spłodzone małe, a brat jego umarł, a został sam tylko po matce swej, i ojciec jego miłuje go.
Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
21 Potem mówiłeś do nas sług swoich: Przywiedźcie go do mnie, abym go oglądał oczyma memi:
“Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
22 I mówiliśmy do pana mego: Nie będzie mogło chłopię opuścić ojca swego; bo gdyby opuściło ojca swego, umarłby.
Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
23 Tedyś rzekł do sług swoich: Jeźli nie przyjdzie brat wasz młodszy z wami, nie ujrzycie więcej oblicza mojego.
Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
24 I stało się, gdyśmy odeszli do sługi twego, ojca mojego, i powiedzieliśmy mu te słowa pana mego:
Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
25 Tedy rzekł ojciec nasz: Jedźcie znowu, a kupcie nam trochę żywności.
“Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
26 I powiedzieliśmy: Nie możemy tam iść: lecz jeźli brat nasz młodszy będzie z nami, tedy pojedziemy; bo inaczej nie będziemy mogli oglądać oblicza męża onego, jeźli brat nasz młodszy nie będzie z nami.
Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
27 I rzekł sługa twój, ojciec mój, do nas: Wy wiecie, że dwóch synów urodziła mi żona moja;
“Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
28 I wyszedł jeden ode mnie, i rzekłem: Zaiste od zwierza rozdarty jest, i nie widziałem go do tych miast;
Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
29 A weźmiecieli i tego od oblicza mego, a przypadnie nań śmierć, tedy doprowadzicie sędziwość moję z żałością do grobu. (Sheol h7585)
Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol h7585)
30 Przetoż teraz jeślibym przyszedł do sługi twego, ojca mojego, a dziecięcia by z nami nie było, (ponieważ dusza jego jest przywiązana do duszy jego),
“Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
31 Stanie się, skoro ujrzy, iż dziecięcia nie będzie, że umrze; a odprowadzą słudzy twoi sędziwość sługi twego, ojca naszego, z żałością do grobu. (Sheol h7585)
ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol h7585)
32 Bo sługa twój przyrzekł za to dziecię, gdy je brał od ojca swego, mówiąc: Jeźlić go zaś nie przywiodę, tedy będę winien grzechu przeciw ojcu memu po wszystkie dni.
Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
33 Teraz tedy niech zostanie proszę sługa twój miasto dziecięcia tego niewolnikiem pana mego, a dziecię niech idzie z bracią swoją.
“Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
34 Bo jakoż ja mam wrócić się do ojca mego, gdy tego dziecięcia ze mną nie będzie? chybabym chciał patrzyć na żałość, która by przyszła na ojca mego.
Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”

< Rodzaju 44 >