< Rodzaju 42 >

1 A widząc Jakób, że było zboże w Egipcie, rzekł do synów swoich: Czemuż się oglądacie jeden na drugiego?
Yakobo atamva kuti ku Igupto kuli tirigu, anati kwa ana ake, “Nʼchifukwa chiyani mukungoyangʼanana wina ndi mnzake?
2 I mówił im: Otom słyszał, że jest zboże w Egipcie. Jedźcież tam, a kupcie nam stamtąd, abyśmy żywi byli, a nie pomarli.
Ine ndamva kuti ku Igupto kuli tirigu. Pitani kumeneko mukatigulireko kuti tisafe ndi njala.”
3 Jechało tedy dziesięć braci Józefowych kupować zboże, do Egiptu;
Choncho abale ake khumi a Yosefe anapita kukagula tirigu ku Igupto.
4 Ale Benjamina, brata Józefowego nie posłał Jakób z bracią jego, bo mówił: By snać nie przypadło nań co złego.
Koma Yakobo sanamulole Benjamini mngʼono wake wa Yosefe kuti apite nawo chifukwa anaopa kuti choyipa chingamuchitikire.
5 I szli synowie Izraelowi pospołu z innymi tamże idącymi kupować zboże; albowiem był głód w ziemi Chananejskiej.
Choncho ana a Israeli aja anapita pamodzi ndi gulu la anzawo kukagula tirigu pakuti ku Kanaani kunalinso njala.
6 A Józef był przedniejszym rządcą w onej ziemi; onże sprzedawał zboża wszystkiemu ludowi ziemi. A gdy przyszli bracia Józefowi, kłaniali mu się twarzą do ziemi.
Pakuti Yosefe anali nduna yayikulu yolamulira dziko la Igupto, ndiye kuti analinso amene ankagulitsa tirigu kwa anthu onse. Choncho abale ake a Yosefe nawonso anabwera, ndipo anamugwadira pansi.
7 A ujrzawszy Józef bracią swą, poznał je; lecz stawił się im jako obcy, i mówił do nich surowo, i rzekł do nich: Skądeście przyszli? I odpowiedzieli: Z ziemi Chananejskiej, abyśmy nakupili żywności.
Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.”
8 Tedy poznał Józef bracią swą; ale go oni nie poznali.
Ngakhale Yosefe anawazindikira abale ake, koma iwo sanamuzindikire.
9 I wspomniał Józef na sny, które mu się śniły o nich, i rzekł im: Szpiegowieście wy, a przyszliście, abyście przepatrzyli miejsca nieobronne tej ziemi.
Pamenepo anakumbukira maloto aja amene analota za iwo ndipo anati, “Inu ndinu akazitape! Mwabwera kudzazonda dziko lathu kuti muone pamene palibe chitetezo.”
10 A oni mu odpowiedzieli: Nie tak, panie mój; ale słudzy twoi przyszli, aby nakupili żywności.
Iwo anayankha, “Ayi mbuye wathu, antchito anufe tabwera kudzagula chakudya.
11 Wszyscyśmy synowie jednego męża; ludzieśmy szczerzy, a nie są słudzy twoi szpiegami.
Tonse ndife ana a munthu mmodzi. Ndife antchito anu okhulupirika osati akazitape.”
12 A on rzekł do nich: Nie tak, aleście nieobronne miejsca tej ziemi przyszli przepatrować.
Iye anawawuza kuti, “Ayi! Inu mwabwera kudzaona pamene palibe chitetezo mʼdziko muno.”
13 I rzekli: Dwanaście nas braci było sług twoich, synów jednego męża w ziemi Chananejskiej; a oto, najmłodszy z ojcem naszym teraz jest w domu, a jednego już nie masz.
Koma iwo anayankha, “Tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri. Abambo athu ndi mmodzi, ndipo kwathu ndi ku Kanaani. Panopo wotsiriza ali ndi abambo athu ndipo wina anamwalira.”
14 I rzekł im Józef: Toć jest com ja wam powiedział, mówiąc: Szpiegowieście wy.
Yosefe anawawuza kuti, “Ndi momwe ndaneneramo: Inu ndinu akazitape.
15 Przez to was doświadczę; żywie Farao, nie wynijdziecie stąd, aż mi tu przyjdzie brat wasz młodszy.
Ndiye ndikuyesani motere: Ine ndikulumbira pali Farao ndithu, inuyo simudzachoka malo ano mpaka wotsirizayo atabwera kuno.
16 Poślijcież jednego z was, aby przywiódł brata waszego, a wy w więzieniu będziecie, ażby były doświadczone słowa wasze, jestli prawda przy was; a jeźli nie, żywie Farao, żeście wy szpiegowie.
Tumizani mmodzi wa inu akamutenge mʼbale wanuyo ndipo ena nonsenu musungidwa mʼndende, kuti titsimikize ngati zimene mukunenazi ndi zoona. Apo ayi, pali Farao ndithu, inu ndinu akazitape!”
17 Tedy je dał pod straż do trzech dni.
Ndipo onse anawayika mʼndende kwa masiku atatu.
18 I mówił do nich Józef dnia trzeciego: Uczyńcie tak, a żyć będziecie; boć się ja boję Boga.
Pa tsiku lachitatu Yosefe anawawuza kuti, “Popeza ine ndimaopa Mulungu, ndipo inuyo ngati mukufuna kukhala ndi moyo muchite izi:
19 Jeźliście szczerzy, brat wasz jeden niech będzie okowany w więzieniu, gdzieście wy byli; a wy jedźcie i odnieście zboże, abyście odjęli głodowi domy wasze.
Ngati muli anthu achilungamo, mmodzi wa inu atsale mʼndende, pamene ena nonse mupite kwanu kuti muwatengere chakudya anthu akwanu kuli njalako.
20 A brata waszego młodszego przywiedźcie do mnie, a sprawdzą się słowa wasze, i nie pomrzecie. I uczynili tak.
Mukabwere naye kuno mngʼono wanu wotsirizayo kuti titsimikizire zimene munanena kuti musafe.” Ndipo anachita zomwezo.
21 I mówili jeden do drugiego: Zaprawdęśmy zgrzeszyli przeciwko bratu naszemu; bo widząc utrapienie duszy jego, gdy się nam modlił, nie wysłuchaliśmy go; dla tegoż przyszedł na nas ten kłopot.
Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Ndithu ife tinalakwira mʼbale wathu uja popeza kuti ngakhale tinaona kuvutika kwake ndi kumva kulira kwake pamene ankatidandaulira kuti timuchitire chifundo, koma ife sitinamvere. Nʼchifukwa chake masautso awa atigwera.”
22 Odpowiedział im tedy Ruben, mówiąc: Izalim wam nie mówił temi słowy: Nie grzeszcie przeciw pacholęciu? a nie usłuchaliście; otóż teraz krwi jego z rąk naszych szukają.
Rubeni anayankha, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musamuchite kanthu mnyamata uja? Koma inu simunamvere! Tsopano tikulandira malipiro a magazi ake.”
23 A oni nie wiedzieli, żeby rozumiał Józef; bo tłumacz był między nimi.
Koma sanadziwe kuti Yosefe ankawamva popeza kuti ankagwiritsa ntchito wotanthauzira poyankhula naye.
24 Odwróciwszy się tedy od nich Józef, płakał; a obróciwszy się do nich, mówił z nimi, i wziąwszy od nich Symeona, związał go przed oczyma ich.
Yosefe anapita pambali payekha kukalira. Kenaka anabweranso nadzayankhula nawo. Iye anatenga Simeoni namumanga iwo akuona.
25 I rozkazał Józef, aby napełniono wory ich zbożem, i wrócono pieniądze ich każdemu do woru jego, i żeby im dano żywności na drogę; i uczyniono tak.
Yosefe analamula kuti awadzazire matumba awo ndi tirigu, awayikiremo ndalama zawo momwemo ndiponso awapatse chakudya cha panjira. Izi anawachitiradi.
26 Tedy oni włożywszy zboża swoje na osły swe, odjechali stamtąd.
Abale a Yosefe aja anasenzetsa abulu awo tirigu amene anagula uja ndipo ananyamuka ulendo wawo.
27 I rozwiązawszy jeden z nich wór swój, aby dał obrok osłowi swemu w gospodzie, ujrzał pieniądze swoje, które były na wierzchu w worze jego.
Atafika pamalo pena poti agone, mmodzi mwa iwo anatsekula thumba lake kuti atapemo chakudya cha bulu wake. Atangomasula anaona kuti ndalama zake zili pakamwa pa thumba.
28 I rzekł do braci swej: Wrócono mi pieniądze moje, a oto, są w worze moim. Tedy im upadło serce, i zdumieli się, jeden do drugiego mówiąc: Cóż nam to Bóg uczynił?
Iye anati kwa abale akewo, “Ndalama zanga andibwezera, izi zili mʼthumba mwangamu.” Mitima yawo inachita ngati yachokamo ndipo anali ndi mantha ambiri, nati, “Ndi chiyani chimene Mulungu watichitira?”
29 Zatem przyszli do Jakóba, ojca swego, do ziemi Chananejskiej, i powiedzieli mu wszystko, co się im przydało, mówiąc:
Atafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani anafotokoza zonse zimene zinawachitikira nati,
30 Mówił z nami on mąż, pan onej ziemi, surowo, i udał nas za szpiegi ziemi;
“Nduna yayikulu ya mʼdzikomo inatiyankhula mwa ukali kwambiri ndipo inkatiyesa kuti ndife akazitape.
31 A myśmy mu rzekli: Szczerzyśmy, nie byliśmy szpiegami;
Koma tinamuwuza kuti, ‘Ndife anthu woona mtima osati akazitape.
32 Dwanaście nas było braci synów ojca naszego; jednego już nie masz, a młodszy teraz jest z ojcem naszym w ziemi Chananejskiej.
Ife tonse tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri, abambo mmodzi. Mmodzi anamwalira, ndipo wamngʼono ali ndi abambo athu ku Kanaani.’”
33 I mówił do nas mąż on, pan onej ziemi: Po tem poznam, żeście szczerzy; brata waszego jednego zostawcie u mnie, a zboże dla odjęcia głodowi domów waszych weźmijcie a idźcie;
Ndipo nduna ija inati kwa ife, “Kuti ndidziwedi kuti ndinu anthu owona mtima muchite izi: Mmodzi mwa inu atsale ndi ine kuno, ndipo enanu mutenge chakudya ndi kubwerera kwanu kumene kuli njalako.
34 Potem przywiedźcie brata waszego młodszego do mnie, abym poznał, żeście wy nie szpiegowie, ale szczerzy; tedy wam wrócę brata waszego, a w tej ziemi handlować będziecie.
Koma mundibweretsere wotsirizayo kuti ndidziwedi kuti sindinu akazitape koma anthu achilungamo. Kenaka ndidzakubwezerani mʼbale wanuyu ndipo mukhoza kuchita malonda mʼdzikoli.”
35 I stało się, gdy wypróżniali wory swoje, a oto, każdy znalazł węzeł pieniędzy swych w worze swoim; a obaczywszy węzły z pieniędzmi swymi, oni i ojciec ich, polękali się.
Pamene amakhuthula matumba awo a tirigu aliyense anapeza kuti kathumba kake ka ndalama kali momwemo. Ataona zimenezi, iwo pamodzi ndi abambo awo anachita mantha kwambiri.
36 I rzekł im Jakób, ojciec ich: Osierociliście mię, Józefa nie masz, i Symeona nie masz, a Benjamina weźmiecie; na mię się to wszystko złe zwaliło.
Abambo awo Yakobo anawawuza kuti, “Mwandilanda ana anga ine. Yosefe anamwalira ndipo Simeoni palibenso, ndiye tsopano mukufuna mutengenso Benjamini. Zonsezi zandigwera ine!”
37 I rzekł Ruben do ojca swego, mówiąc: Dwóch synów moich zabij, jeźlić go zaś nie przywiodę; daj go do ręki mojej, a ja go tobie przywrócę.
Koma Rubeni anati kwa abambo ake, “Ngati sindidzabwera naye kwa inu, mudzaphe ana anga aamuna awiri. Muperekeni mʼmanja mwangamu ndipo ndidzamusamala ndi kubwera naye kwa inu.”
38 Ale on rzekł: Nie pójdzie syn mój z wami, gdyż brat jego umarł, a on sam tylko został; a jeźliby nań przypadło co złego na drodze, którą pójdziecie, tedy doprowadzicie sędziwość moję z żałością do grobu. (Sheol h7585)
Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.” (Sheol h7585)

< Rodzaju 42 >