< Rodzaju 4 >

1 Potem Adam poznał Ewę, żonę swoję, która poczęła i porodziła Kaina, i rzekła: Otrzymałam męża od Pana.
Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
2 I porodził zasię brata jego Abla; i był Abel pasterzem owiec, a Kain był rolnikiem.
Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
3 I stało się po wielu dni, iż przyniósł Kain z owocu ziemi ofiarę Panu.
Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
4 Także i Abel przyniósł z pierworodztw trzód swoich i z tłustości ich; i wejrzał Pan na Abla i na ofiarę jego.
Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
5 Ale na Kaina i na ofiarę jego nie wejrzał; i rozgniewał się Kain bardzo, i spadła twarz jego.
Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
6 Tedy rzekł Pan do Kaina: Przeczżeś się zapalił gniewem a czemu spadła twarz twoja?
Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
7 Azaż, jeźli dobrze czynić będziesz, nie będziesz wywyższon? a jeźli nie będziesz dobrze czynił, we drzwiach grzech leży; a do ciebie chuć jego będzie, a ty nad nim panować będziesz.
Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
8 I rozmawiał Kain z Ablem bratem swoim. I stało się, gdy byli na polu, że powstał Kain na Abla brata swego, i zabił go.
Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
9 I rzekł Pan do Kaina: Gdzież jest Abel brat twój? który odpowiedział: Nie wiem; izalim ja stróżem brata mego?
Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
10 I rzekł Bóg: Cóżeś uczynił? Głos krwi brata twego woła do mnie z ziemi.
Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
11 Teraz tedy przeklętym będziesz na ziemi, która otworzyła usta swe, aby przyjęła krew brata twego z ręki twojej.
Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
12 Gdy będziesz sprawował ziemię, nie wyda więcej mocy swej tobie; tułaczem, i biegunem będziesz na ziemi.
Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
13 Tedy rzekł Kain do Pana: Większa jest nieprawość moja, niżby mi ją odpuścić miano.
Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
14 Oto mię dziś wyganiasz z oblicza tej ziemi, a przed twarzą twoją skryję się, i będę tułaczem, i biegunem na ziemi; i stanie się, że ktokolwiek mię znajdzie, zabije mię.
Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
15 I rzekł mu Pan: Zaiste, ktobykolwiek zabił Kaina, siedmioraką odniesie pomstę. I włożył Pan na Kaina piętno, aby go nie zabijał, ktobykolwiek znalazł.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
16 Tedy odszedł Kain od oblicza Pańskiego, i mieszkał w ziemi Nod, na wschód słońca od Eden.
Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
17 I poznał Kain żonę swą, która poczęła, i porodziła Enocha; i zbudował miasto, i nazwał imię miasta tego imieniem syna swego, Enoch.
Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
18 I urodził się Enochowi Irad, a Irad spłodził Mawiaela, a Mawiael spłodził Matusaela, a Matusael spłodził Lamecha.
Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
19 I pojął sobie Lamech dwie żony; imię jednej, Ada, a imię drugiej, Sella.
Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
20 Tedy urodziła Ada Jabala, który był ojcem mieszkających w namieciech, i pasterzów.
Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
21 A imię brata jego było Jubal, który był ojcem wszystkich grających na harfie, i na muzyckiem naczyniu.
Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
22 Sella też urodziła Tubalkaina, rzemieślnika wszelkiej roboty, od miedzi i od żelaza. A siostra Tubalkainowa była Noema.
Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
23 Tedy rzekł Lamech żonom swym, Adzie i Selli: Słuchajcie głosu mego, żony Lamechowe, posłuchajcie słów moich; zabiłbym ja męża za zranienie moje, i młodzieńca za siność moję.
Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
24 Jeźlić siedmiokroć mścić się będą za Kaina, tedyć za Lamecha siedemdziesiąt i siedem kroć.
Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
25 I poznał jeszcze Adam żonę swą, która urodziła syna, i nazwała imię jego Set, mówiąc: Dał mi Bóg inne potomstwo miasto Abla, którego zabił Kain.
Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
26 Setowi też urodził się syn, i nazwał imię jego Enos. Na ten czas poczęto wzywać imienia Pańskiego.
Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

< Rodzaju 4 >