< Rodzaju 39 >

1 Tedy Józef był zawiedzion do Egiptu; i kupił go Potyfar, dworzanin Faraonów, hetman żołnierstwa, mąż Egipczanin, z ręki Ismaelitów, którzy go tam byli zawiedli.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 I był Pan z Józefem, który był mężem szczęśliwie postępującym, a mieszkał w domu pana swego Egipczanina.
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 I baczył pan jego, że Pan był z nim, a iż wszystko co on czynił, Pan szczęścił w ręku jego.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 I znalazł Józef łaskę w oczach jego, i służył mu; i przełożył go nad domem swym, a podał wszystko co miał, w ręce jego.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 I stało się, gdy go przełożył nad domem swym, i nad wszystkiem, co miał, błogosławił Pan domowi Egipczanina dla Józefa; i było błogosławieństwo Pańskie nad wszystkiem, cokolwiek miał w domu i na polu.
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 Przetoż poruczył wszystko, co miał, w ręce Józefowe, i ni o czem u siebie nie wiedział, tylko o chlebie, którego pożywał. A był Józef pięknej twarzy, i wdzięczny na wejrzeniu.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 I stało się potem, iż obróciła żona pana jego oczy swoje na Józefa, i rzekła: Śpij ze mną.
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 Ale nie chciał: i rzekł do żony pana swego: Oto, pan mój nie wie, tak jako ja, co jest w domu jego; bo wszystko, co miał, podał w ręce moje.
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 I nie masz nikogo w domu tym nad mię przedniejszego, i nie wyjął mi nic z mocy, prócz ciebie, przeto żeś ty jest żona jego; jakoż bym tedy miał uczynić tę wielką złość, i grzeszyć przeciwko Bogu?
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 I stało się, gdy ona namawiała Józefa na każdy dzień, a on jej nie zezwalał, aby spał z nią, albo bywał z nią:
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 Tedy dnia niektórego, gdy wszedł do domu, dla odprawowania pracy swej, a nie było tam z domowników nikogo w domu;
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 Uchwyciła go za szatę jego, mówiąc: Śpij ze mną. Ale on zostawiwszy szatę swoję w ręku jej, uciekł, i wyszedł precz.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 A gdy ona obaczyła, iż zostawił szatę swoję w ręku jej, a uciekł precz;
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 Tedy zawołała na czeladź domu swego, i rzekła do nich, mówiąc: Wejcie, wprowadził pan do nas męża Hebrejczyka, aby nas zelżył; albowiem wszedł do mnie, aby ze mną spał, ażem wołała głosem wielkim.
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 A gdy usłyszał, żem wyniosła głos mój, i zawołała, zostawiwszy szatę swoję u mnie, uciekł, i wyszedł precz.
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 I zatrzymała jego szatę u siebie, aż przyszedł pan jego do domu swego;
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 I rzekła do niego w te słowa, mówiąc: Wszedł do mnie sługa ten Hebrejczyk, któregoś przywiódł do nas, aby mię zelżył.
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 A gdym podniosła głos swój, i zawołała, tedy zostawił szatę swą u mnie, i uciekł precz.
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 I stało się, gdy usłyszał pan jego słowa żony swojej, które rzekła do niego, mówiąc: Tak mi uczynił sługa twój, rozgniewał się bardzo.
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 I wziął pan Józefa, a dał go do domu więzienia, tam, gdzie więźnie królewskie sadzano, i był tam w domu więzienia.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 A Pan był z Józefem, i skłoniwszy ku niemu miłosierdzie, dał mu łaskę w oczach przełożonego nad domem więzienia.
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 Tedy przełożony nad domem więzienia, podał w moc Józefowi wszystkie więźnie, którzy byli w domu więzienia; a wszystko, co tam czynić mieli, to on sprawował.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 A przełożony nad domem więzienia nie doglądał tego, czego mu się powierzył, dla tego iż Pan był z nim, a co on czynił, to Pan szczęścił.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

< Rodzaju 39 >