< Rodzaju 37 >

1 I mieszkał Jakób w ziemi, gdzie przychodniem był ojciec jego, w ziemi Chananejskiej.
Yakobo ankakhala mʼdziko la Kanaani kumene abambo ake ankakhala.
2 Teć są pokolenia Jakóbowe: Józef, gdy miał siedemnaście lat, pasł z bracią swoją trzody, ( będąc pacholęciem ), z synami Bali, i z synami Zelfy, żon ojca swego; i odnosił Józef sławę ich złą do ojca ich.
Mbiri ya banja la Yakobo ndi iyi: Yosefe, mnyamata wa zaka 17 ankaweta nkhosa ndi abale ake, pamodzi ndi ana a Biliha ndi Zilipa, akazi a abambo ake. Tsono Yosefe ankabwera kudzawuza abambo ake zoyipa za abale ake.
3 A Izrael miłował Józefa nad wszystkie syny swe, iż mu się był w starości jego urodził, i sprawił mu suknią rozmaitych farb.
Tsono Israeli ankakonda Yosefe koposa ana ake ena onse, chifukwa anali mwana wobadwa muukalamba wake. Ndipo anamusokera mkanjo wa manja aatali.
4 A widząc bracia jego, że go miłował ojciec ich nad wszystkę bracią jego, nienawidzili go, i nie mogli nic łaskawie z nim mówić.
Pamene abale ake anaona kuti abambo awo ankakonda Yosefe kuposa aliyense wa iwo, anayamba kumuda Yosefe ndipo sankayankhula naye zamtendere.
5 I śnił się Józefowi sen, a gdy go powiedział braci swej, tem go więcej mieli w nienawiści.
Tsiku lina Yosefe analota maloto ndipo pamene anawuza abale ake za malotowo, iwo anawonjeza kumuda.
6 Bo rzekł do nich: Słuchajcie proszę snu tego, który mi się śnił.
Iye anawawuza kuti, “Tamvani maloto amene ndinalota:
7 Otośmy wiązali snopy na polu, a oto, wstawszy snop mój stanął, a około niego stojące snopy wasze kłaniały się snopowi mojemu.
Ife timamanga mitolo ya tirigu ku munda ndipo mwadzidzidzi mtolo wanga unayimirira chilili, pamene mitolo yanu inazungulira mtolo wangawo nʼkumawugwadira.”
8 I odpowiedzieli mu bracia jego: Izali królować będziesz nad nami? i panować nam będziesz? stądże go jeszcze mieli w większej nienawiści, dla snów jego, i dla słów jego.
Abale ake aja anamufunsa nati, “Kodi ukuyesa kuti ungakhale mfumu yathu? Ungadzatilamuliredi iweyo?” Ndipo anamuda kuposa kale chifukwa cha maloto ake ndi zimene ankakonda kunena kwa abambo awo.
9 Śnił mu się też jeszcze drugi sen, i powiedział go braci swej, mówiąc: Oto mi się znowu śnił sen: A ono słońce i miesiąc, i jedenaście gwiazd kłaniało mi się.
Tsiku lina analotanso maloto ena, ndipo anafotokozera abale ake za malotowo. Iye anati, “Tamverani, ndinalotanso maloto ena. Ulendo uno dzuwa ndi mwezi pamodzi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zimandigwadira.”
10 I powiedział ojcu swemu i braci swej, i gromił go ojciec jego i mówił mu: Cóż to za sen, coć się śnił? Izali przyjdziemy, ja i matka twoja z bracią twoją, abyśmyć się kłaniali aż do ziemi.
Atawuza abambo ake ndi abale ake malotowa, abambo ake anamukalipira nati, “Ndi maloto anji umalotawa? Kodi uganiza kuti ine, amayi ako pamodzi ndi abale ako onsewa tingadzabwere kudzakugwandira iwe?”
11 I nienawidzili go bracia jego; ale ojciec jego pilnie uważał tę rzecz.
Abale ake anamuchitira nsanje, koma abambo ake anasunga nkhaniyi mu mtima.
12 I odeszli bracia jego, aby paśli trzody ojca swego w Sychem.
Tsono abale ake anapita kukadyetsa ziweto za abambo awo ku Sekemu,
13 Tedy rzekł Izrael do Józefa: Izali bracia twoi nie pasą w Sychem? pójdźże, a poślę cię do nich; a on odpowiedział: Otom ja.
ndipo Israeli anati kwa Yosefe, “Tsono, ndikufuna kukutuma kwa abale ako.” Iye anayankha nati, “Chabwino.”
14 Rzekł mu tedy: Idźże teraz, a dowiedz się, jako się mają bracia twoi, i co się dzieje z trzodami, i dasz mi znać. Wysłał go tedy z doliny Hebron, i przyszedł do Sychem.
Choncho anati kwa iye, “Pita ukaone ngati abale ako ali bwino. Ukaonenso nkhosa ngati zili bwino. Kenaka ubwere udzandiwuze.” Choncho Israeli anatuma Yosefe kuchokera ku chigwa cha Hebroni. Yosefe atafika ku Sekemu,
15 I nadszedł go niektóry mąż, a on się błąkał po polu; i pytał go mąż on mówiąc:
munthu wina anamupeza akungozungulirazungulira mʼmunda ndipo anamufunsa, “Ukufunafuna chiyani?”
16 Czegóż szukasz? A on odpowiedział: Braci mojej szukam; powiedz mi proszę, gdzie oni pasą.
Iye anayankha, “Ndikufuna abale anga. Mungandiwuze kumene akudyetsa ziweto zawo?”
17 Tedy rzekł on człowiek: Odeszli stąd; bom słyszał, gdy mówili: Pójdźmy do Dotain. I szedł Józef za bracią swoją, a znalazł je w Dotain.
Munthuyo anayankha nati, “Anasamukako kuno. Ndinawamva akuti, ‘Tiyeni tipite ku Dotani.’” Choncho Yosefe analondola abale ake ndipo anakawapeza ku Dotani.
18 I ujrzeli go z daleka, a pierwej niż do nich przyszedł, radzili o nim, aby go zabili.
Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.
19 I mówili jeden do drugiego: Onoż mistrz on snów idzie.
Iwo anawuzana nati, “Uyo akubwera apo wamaloto uja.
20 Teraz tedy pójdźcie, a zabijmy go, i wrzućmy go w jaką studnią, a rzeczemy: Zły go zwierz pożarł; a tak obaczymy, na co mu wynijdą sny jego.
Tsono tiyeni timuphe ndi kuponya thupi lake mu chimodzi mwa zitsime izi ndipo tidzati anadyedwa ndi nyama zakuthengo zolusa. Tsono timuonera zomwe ziti zichitike ndi maloto ake aja.”
21 Co gdy usłyszał Ruben, chciał go wybawić z rąk ich, mówiąc: Nie zabijajmy go.
Koma Rubeni atamva izi, anapulumutsa Yosefe. Iye anati kwa abale ake, “Ayi, tisamuphe,
22 Nad to rzekł do nich Ruben: Nie wylewajcie krwi, ale wrzućcie go w tę studnią, która jest na puszczy, a ręki nie ściągajcie nań. A to mówił, aby go wybawił z rąk ich, i powrócił go ojcu swemu.
tisakhetse magazi. Tiyeni timuponye mʼchitsime ku chipululu konkuno. Koma tisamuvulaze nʼkomwe. Rubeni ananena zonsezi kuti apulumutse Yosefe ndi kuti pambuyo pake akamupereke kwa abambo awo.”
23 I stało się, gdy przyszedł Józef do braci swej, zwlekli go z sukni jego, z sukni rozmaitych farb, którą miał na sobie.
Choncho Yosefe atafika kwa abale ake, iwo anamuvula mkanjo wake wamanja aatali uja umene anavala
24 A porwawszy go, wrzucili go w studnią, która studnia była czcza, i nie było w niej wody.
ndipo anamutenga namuponya mʼchitsime chopanda madzi komanso mopanda chilichonse.
25 A usiadłszy, aby jedli chleb, podnieśli oczy swe, i ujrzeli, a ono poczet Ismaelitów, idących z Galaad; a wielbłądy ich niosły korzenie, i kadzidło, i myrrę, a szły, aby to zaniosły do Egiptu.
Atakhala pansi kuti adye chakudya, anatukula maso naona gulu la Aismaeli akubwera kuchokera ku Giliyadi. Ngamira zawo zinanyamula zonunkhiritsa bwino zakudya zamitundumitundu, ndipo zimenezi ankapita nazo ku Igupto.
26 Tedy rzekł Judas do braci swej: Cóż za pożytek, choćbyśmy zabili brata naszego, i zataili krwi jego?
Yuda anafunsa abale ake nati, “Kodi tidzapindula chiyani tikapha mʼbale wathuyu ndi kuphimbitsa magazi ake?
27 Pójdźcie, a przedajmy go Ismaelitom, a ręka nasza niech nie będzie na nim; brat bowiem nasz, i ciało nasze jest; i usłuchali go bracia jego.
Bwanji timugulitse kwa Aismaeliwa, koma ife tisamuchite kanthu kalikonse. Ameneyu ndi mʼbale wathu thupi limodzi ndi ife.” Abale ake anavomereza zimenezi.
28 A gdy mijali oni mężowie, Madyjańscy kupcy, tedy wyciągnęli, i wyjęli Józefa z studni, i sprzedali Józefa Ismaelitom za dwadzieścia srebrników, którzy zaprowadzili Józefa do Egiptu.
Amalonda ena a ku Midiyani ankadutsa pomwepo. Tsono abale ake a Yosefe anamutulutsa Yosefe uja mu chitsime chija ndipo anamugulitsa kwa Aismaeli aja pamtengo wa masekeli makumi awiri. Choncho anapita naye Yosefe ku Igupto.
29 Tedy się wrócił Ruben do onej studni, a oto, już nie było Józefa w studni; i rozdarł szaty swoje.
Rubeni atabwerera ku chitsime kuja anapeza kuti Yosefe mulibe mʼchitsimemo. Pamenepo iye anangʼamba zovala zake
30 A wróciwszy się do braci swej, rzekł: Pacholęcia nie masz, a ja dokąd? ja dokąd pójdę?
nabwerera kwa abale ake nati, “Mnyamata uja mulibemo! Nanga ndilowere kuti ine tsopano?”
31 Tedy wzięli suknią Józefowe, i zabili kozła, a umaczali suknią we krwi.
Tsono anapha kamwana ka mbuzi, natenga mkanjo wa Yosefe ndi kuwunyika mʼmagazi ake.
32 I posłali onę suknią rozmaitych farb, aby ją zaniesiono do ojca jego, i rzekli: Tęś my znaleźli, poznajże teraz, jeźli to suknia syna twego, czyli nie
Iwo anatenga mkanjo uja nabwerera nawo kwa abambo awo nati, “Ife tapeza mkanjowu. Tawuyangʼanitsitsani muone ngati uli wa mwana wanu.”
33 A poznawszy ją, rzekł: Suknia jest syna mego; zwierz zły pożarł go; koniecznie rozszarpany jest Józef.
Iye anawuzindikira ndipo anati, “Ndi mkanjo wa mwana wanga umenewu! Nyama yakuthengo yolusa yamudya. Mosakayika, mwana wanga Yosefe wakhadzulidwa.”
34 Tedy rozdarłszy Jakób szaty swe, włożył wór na biodra swoje, żałując syna swego przez wiele dni.
Pamenepo Yakobo anangʼamba zovala zake, navala chisaka mʼchiwuno mwake. Iye analira maliro a mwana wake masiku ambiri.
35 I zeszli się wszyscy synowie jego, i wszystkie córki jego, aby go cieszyli, lecz nie dał się cieszyć, ale mówił: Zaprawdę zstąpię za synem moim do grobu; i płakał go ojciec jego. (Sheol h7585)
Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake. (Sheol h7585)
36 A Madyjańczycy sprzedali Józefa do Egiptu Potyfarowi, dworzaninowi Faraonowemu, hetmanowi żołnierstwa.
Amidiyani aja anagulitsa Yosefe kwa Potifara, mmodzi mwa nduna za Farao ku Igupto. Potifarayu anali mkulu wa asilikali olonda nyumba ya Farao.

< Rodzaju 37 >