< Rodzaju 32 >

1 A Jakób też poszedł w drogę swoję i potkali się z nim Aniołowie Boży.
Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
2 I rzekł Jakób ujrzawszy je: Obóz to Boży; i nazwał imię miejsca onego Mahanaim.
Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
3 Potem posłał Jakób posły przed sobą do Ezawa, brata swego, do ziemi Seir, do krainy Edomskiej.
Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
4 I rozkazał im mówiąc: Tak rzeczecie do pana mego Ezawa: To mówi sługa twój Jakób: U Labana byłem gościem, i mieszkałem z nim aż do tego czasu.
Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
5 A mam woły i osły, owce, i sługi, i służebnice, a posyłam odpowiedzieć panu memu, żebym znalazł łaskę w oczach twoich.
Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
6 I wrócili się posłowie do Jakóba, mówiąc: Przyszliśmy do brata twego Ezawa, który też idzie przeciwko tobie, a cztery sta mężów z nim.
Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
7 I zląkł się Jakób bardzo a strwożył się; i rozdzielił lud, który z nim był, i owce, i woły, i wielbłądy, na dwa hufce;
Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
8 I rzekł: Jeźliby przyszedł Ezaw do jednego hufca, a poraziłby go, tedy hufiec, który pozostanie, będzie zachowany.
Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
9 I rzekł Jakób: Boże ojca mego Abrahama, i Boże ojca mego Izaaka, Panie, któryś do mnie rzekł: Wróć się do ziemi twojej, i do rodziny twojej, a uczynięć dobrze.
Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
10 Mniejszym jest niż wszystkie zmiłowania, i niż wszystka prawda, którąś uczynił z sługą swym. Albowiem tylko o lasce mojej przeszedłem ten Jordan, a teraz mam dwa hufce.
Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
11 Wyrwij mię proszę z ręki brata mego, z ręki Ezawa; boć się go boję, by snać przyszedłszy nie zabił mię, i matki z synami.
Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
12 Wszakeś rzekł: Dobrze czyniąc będęć dobrze czynił, a rozmnożę nasienie twoje jako piasek morski, który zliczon być nie może, dla mnóstwa.
Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
13 I przenocował tam onej nocy, i wziął z tego, co miał przy ręku, upominek dla Ezawa, brata swego.
Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
14 To jest kóz dwieście, i kozłów dwadzieścia, owiec dwieście, i baranów dwadzieścia.
Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
15 Wielbłądzic odchowujących młode, ze źrebięty ich, trzydzieści, krów czterdzieści, i wołów dziesięć, dwadzieścia oślic, i dziesięć ośląt.
ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
16 I oddał je w ręce sług swoich, każde stado z osobna, i rzekł do sług swoich: Idźcie przede mną, a plac uczyńcie między stadem a między stadem.
Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
17 I rozkazał pierwszemu, mówiąc: Gdy się spotka z tobą Ezaw, brat mój, a spyta cię, mówiąc: Czyjeś ty? i dokąd idziesz? a czyje to stado przed tobą?
Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
18 Tedy powiesz: Sługi twego Jakóba jest to upominek, posłany panu memu Ezawowi, a oto, i sam idzie za nami.
Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
19 Także też rozkazał drugiemu, i trzeciemu, i wszystkim idącym za temi stady, mówiąc: Temiż słowy mówcie do Ezawa, gdy go potkacie.
Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
20 Powiecie mu też: Oto, sługa twój Jakób idzie za nami, mówił bowiem: Ubłagam oblicze jego upominkiem, który idzie przede mną, a potem ujrzę oblicze jego; owa mię snać w łaskę przyjmie.
Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
21 I poszedł w przód on upominek przed obliczem jego, a sam przenocował onej nocy z hufcem swoim.
Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
22 Wstawszy tedy onej nocy, wziął obie żony swe, i dwie służebnice swoje, i jedenaście synów swoich, i przeszedł przez bród Jabok,
Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
23 A wziąwszy je, przeprawił je przez tęż rzekę, i przeprowadził wszystko, co miał.
Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
24 A tylko sam Jakób został.
Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
25 A oto, biedził się z nim mąż aż do wejścia zorzy; który widząc, że go nie mógł przemóc, uderzył Jakóba w staw biodry jego, i wytrąciła się z stawu biodra Jakóbowa, gdy się z nim mocował.
Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
26 I rzekł: Puść mię, bo już wschodzi zorza. I odpowiedział: Nie puszczę cię, aż mi będziesz błogosławił.
Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
27 Tedy mu rzekł: Co za imię twoje? I odpowiedział: Jakób.
Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
28 I rzekł: Nie będzie nazywane więcej imię twoje Jakób, ale Izrael; boś sobie mężnie poczynał z Bogiem, i z ludźmi, i przemogłeś.
Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
29 I spytał Jakób mówiąc: Oznajmij mi proszę imię twoje; a on odpowiedział: Czemu się pytasz o imieniu mojem? I tamże mu błogosławił.
Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
30 Tedy nazwał Jakób imię miejsca onego Fanuel, mówiąc: Iżem widział Boga twarzą w twarz, a zachowana jest dusza moja.
Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
31 I weszło mu słońce, kiedy minął miejsce Fanuel, a on uchramował na biodrę swoję.
Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
32 Przetoż nie jadają synowie Izraelscy żyły skurczonej, która jest przy stawie biodry, aż do dnia tego, iż był uderzył w staw biodry Jakóbowej, i w żyłę skurczoną.
Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.

< Rodzaju 32 >