< Rodzaju 24 >

1 A Abraham był stary i podeszły w leciech, a Pan błogosławił mu we wszystkiem.
Tsopano Abrahamu anali atakalamba kwambiri, ndipo Yehova anamudalitsa mu zonse anachita.
2 Tedy rzekł Abraham do starszego sługi swego w domu swym, który wszystkiem rządził, co miał: Połóż, proszę, rękę twoję pod biodro moje;
Tsiku lina Abrahamu anawuza wantchito wake wamkulu amene ankayangʼanira zonse anali nazo, kuti “Ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga.
3 A zaprzysięgnę cię przez Pana, Boga nieba, i Boga ziemi, abyś nie brał żony synowi memu z córek Chananejskich, między któremi ja mieszkam;
Ndikufuna kuti ulumbire pamaso pa Yehova, Mulungu wakumwamba ndi dziko lapansi, kuti sudzamupezera mwana wanga mkazi pakati pa atsikana Achikanaani a kuno kumene ndikukhala,
4 Ale pójdziesz do ziemi mojej, i do rodziny mojej, a stamtąd weźmiesz żonę Izaakowi, synowi memu.
koma kuti udzapita ku dziko la kwathu ndi kukamupezera mkazi mwana wanga Isake pakati pa abale anga.”
5 Tedy mu rzekł sługa: A jeźliby snać nie chciała niewiasta ona iść ze mną do tej ziemi, mamże odprowadzić syna twego do ziemi, z którejś ty wyszedł?
Wantchito uja anafunsa kuti, “Nanga atakhala kuti mkaziyo sakufuna kubwera nane kuno? Kodi ine ndingadzatenge mwana wanu ndi kubwerera naye ku dziko kumene munachokera?”
6 I rzekł mu Abraham: Strzeż się, abyś tam zasię nie zaprowadzał syna mego.
Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.
7 Pan Bóg niebieski, który mię wziął z domu ojca mego, i z ziemi rodziny mojej, i który mówił ze mną, a który mi przysiągł, mówiąc: Nasieniu twemu dam ziemię tę; on pośle Anioła swego przed obliczem twojem, i weźmiesz stamtąd żonę synowi memu.
Yehova Mulungu wakumwamba amene ananditenga kwa makolo anga nanditulutsa mʼdziko lobadwira, ameneyo anayankhula nane molumbira kuti, ‘Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko ili.’ Iyeyu adzatumiza mngelo wake kuti akutsogolere kumeneko kukapezera mwana wanga mkazi.
8 A jeźliby nie chciała ona niewiasta iść z tobą, wolny będziesz od tego poprzysiężenia mego; tylko syna mego nie zaprowadzaj tam.
Ngati mkaziyo adzakana kubwerera nawe ndiye kuti udzakhala womasuka ku lumbiro langa. Koma usadzamutenge mwana wanga ndi kubwerera naye kumeneko.”
9 Podłożył tedy sługa rękę swoję pod biodro Abrahama, pana swego, i przysiągł mu na to.
Choncho wantchitoyo anayika dzanja lake pansi pa ntchafu ya mbuye wake Abrahamu nalumbira kwa iye kuti adzachitadi monga mwa mawu a Abrahamu.
10 I wziął on sługa dziesięć wielbłądów, z wielbłądów pana swego, i poszedł; bo wszystkie dobra pana swego miał w rękach swych; a wstawszy puścił się do Aram Naharaim, do miasta Nachorowego.
Tsono wantchito uja anatengapo ngamira khumi mwa ngamira za mbuye wake pamodzi ndi zinthu zabwino za mitundumitundu. Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda wa Nahori, mʼdziko la Mesopotamiya.
11 I postawił wielbłądy przed miastem u studni wody, pod wieczór, tego czasu, którego zwykły niewiasty wychodzić czerpać wodę.
Atafika, anagwaditsa pansi ngamira zija pafupi ndi chitsime chimene chinali kunja kwa mzinda uja. Awa anali madzulo ndithu, nthawi imene amayi amapita kukatunga madzi.
12 I rzekł: Panie, Boże pana mego Abrahama! Niech mię proszę spotka dziś, czego żądam, a uczyń miłosierdzie z panem moim Abrahamem.
Ndipo wantchito uja anapemphera nati, “Haa, Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, mulole kuti zinthu zindiyendere ine lero, ndipo muonetseni mbuye wanga Abrahamu kukoma mtima kwanu kosasinthika.
13 Oto, ja stoję u studni, a córki obywateli miasta tego wyjdą czerpać wodę;
Taonani ndayima pambali pa chitsimechi, ndipo atsikana a mu mzindawu akubwera kudzatunga madzi.
14 Panienka tedy, do której bym rzekł: Nachyl proszę wiadra twego, że się napiję, a ona by rzekła: Pij, owszem i wielbłądy twoje napoję; ta niech będzie, którąś zgotował słudze twemu Izaakowi; a po tem poznam, żeś uczynił miłosierdzie z panem moim.
Ine ndipempha mtsikana wina kuti, ‘Chonde tula mtsuko wako kuti ndimweko madzi.’ Tsono iye akayankha kuti ‘Imwani,’ ndipo ndidzapatsanso ngamira zanu madziwo, ameneyo akhale mkazi amene mwasankhira mtumiki wanu Isake.” Zimenezi zikachitika, ndidzadziwa kuti mwaonetsadi kukoma mtima kwanu kosasinthika kwa mbuye wanga.
15 I stało się, że pierwej niż przestał mówić, oto, Rebeka wychodziła, która się urodziła Batuelowi, synowi Melchy, żony Nachora, brata Abrahamowego, niosąc wiadro na ramieniu swem.
Asanatsirize kupemphera, anangoona Rebeka watulukira atasenza mtsuko wake pa phewa. Iyeyu anali mwana wa Betueli mwana wa Milika, mkazi wa Nahori mʼbale wake wa Abrahamu.
16 A dzieweczka ona była bardzo piękna na wejrzeniu, panna, a której mąż nie uznał; ta przyszedłszy do studni, napełniła wiadro swe, i wracała się.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri, namwali amene sanadziwe mwamuna. Iye anatsikira ku chitsime nadzaza mtsuko nakweranso ku mtunda.
17 Tedy zabieżał jej on sługa, i rzekł: Daj mi się proszę napić trochę wody z wiadra twego.
Wantchito uja anathamanga kukakumana naye nati, “Chonde patseko madzi pangʼono a mu mtsuko wakowo kuti ndimwe.”
18 A ona rzekła: Pij, panie mój, i prędko złożyła wiadro swe na rękę swoję, i dała mu pić.
Mtsikanayo anati, “Imwani mbuye wanga.” Ndipo mofulumira anatsitsa mtsuko uja nawuyika mʼmanja ndi kumupatsa kuti amwe.
19 A gdy mu się dała napić, rzekła: I wielbłądom twoim naczerpię, aż się napiją.
Atatha kupereka madzi akumwa kwa mlendo uja, mtsikanayo anati, “Ndikatungiranso ngamira madzi kuti zimwe mpaka zitakwana.”
20 I wylała prędko wodę z wiadra swego w koryto, a bieżawszy jeszcze do studni czerpać, naczerpała wszystkim wielbłądom jego.
Choncho anafulumira kukhuthula madzi a mu mtsuko aja momwera ziweto, nathamanga kubwerera ku chitsime kukatunga madzi ena, ndipo anatunga okwanira ngamira zake zonse.
21 A on mąż zdumiewał się nad nią, uważając z milczeniem, jeźli mu Pan zdarzył drogę jego, czyli nie.
Modekha, munthu uja anayangʼanitsitsa kwambiri mtsikana uja kuti adziwedi ngati Yehova anamutsogolera pa ulendo wake uja kapena ayi.
22 I gdy się napiły wielbłądy, wyjął on mąż nausznicę złotą, która ważyła pół sykla, i dwie manele, i dał na ręce jej, które ważyły dziesięć syklów złota.
Ngamira zija zitatha kumwa, mlendo uja anatulutsa chipini chagolide cholemera theka la sekeli ndi zibangiri zagolide ziwiri zolemera masekeli 100.
23 I rzekł: Czyjaś ty córka, powiedz mi, proszę? a jeźli w domu ojca twego miejsce dla nas, gdzie byśmy przenocowali?
Kenaka anafunsa namwaliyo kuti, “Chonde tandiwuza, kodi ndiwe mwana wa yani? Ndipo kodi malo alipo kwanu woti ife nʼkugona?”
24 A ona mu rzekła: Jestem córka Batuela, syna Melchy, którego urodziła Nachorowi.
Anamuyankha kuti, “Ine ndine mwana wa Betueli, mwana amene Milika anaberekera Nahori.”
25 Nad to rzekła mu: Jest u nas dosyć plew i pastwy, i miejsce do przenocowania.
Ndipo anapitiriza kunena kuti, “Chakudya chodyetsa nyamazi chilipo kwathu ndipo malo woti mugone aliponso.”
26 I pokłonił się on człowiek i dał chwałę Panu,
Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,
27 I rzekł: Błogosławiony Pan, Bóg pana mego Abrahama, który nie oddalił miłosierdzia swego i prawdy swojej od pana mojego, albowiem gdym był w drodze, przyprowadził mię Pan w dom braci pana mego.
nati, “Alemekezeke Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene waonetsa kukoma mtima kwake kosasintha ndi kukhulupirika kwake kwa mbuye wanga. Yehova wanditsogolera pa ulendo wanga mpaka ndafika ku nyumba kwa abale ake a mbuye wanga.”
28 Bieżała tedy dzieweczka, i oznajmiła w domu matki swej, jako się co stało.
Mtsikana uja anathamanga nakafotokozera zimenezi anthu a kwa amayi ake.
29 I miała Rebeka brata imieniem Labana; i wybieżał Laban przeciwko onemu mężowi aż ku studni.
Tsono Rebeka anali ndi mlongo wake dzina lake Labani.
30 Bo ujrzawszy nausznicę, i manele na ręku siostry swej, i usłyszawszy słowa Rebeki, siostry swej, mówiącej: Tak mówił do mnie ten mąż; przyszedł do onego męża, a oto, on stał przy wielbłądach u studni.
Iyeyu atangoona chipini pa mphuno ndi zibangiri pa mikono ya mlongo wake komanso kumva zimene mlendo uja ananena kwa Rebekayo, anathamangira kwa mlendo uja, ndipo anamupeza atangoyima ndi ngamira zake pafupi ndi chitsime.
31 I rzekł do niego: Wnijdź błogosławiony Pański; przecz byś stał na dworze, jużem ja nagotował dom, i miejsce wielbłądom?
Iye anati, “Tiyeni kwathu, ndinu munthu amene Yehova wamudalitsa. Bwanji mwangoyimirira panja pano? Ine ndakukonzerani malo ogona inu ndi ngamira zanu.”
32 Tedy wszedł mąż on w dom; a Laban rozsiodłał wielbłądy, i dał plew i pastwy wielbłądom, i wody dla umycia nóg jego, i nóg mężów onych, którzy z nim byli.
Choncho munthu uja analowa mʼnyumba. Labani anatsitsa katundu anali pa ngamira uja. Kenaka anazipatsa ngamira zija chakudya, ndiponso anapereka madzi wosamba mapazi kwa mlendo uja ndi anthu ena onse.
33 I położył przedeń, coby jadł; ale on rzekł: Nie będę jadł, aż pierwej odprawię rzecz swoję. Tedy rzekł Laban: Mówże.
Chakudya chitabwera mlendo uja anati, “Sindidya mpaka nditakuwuzani zimene ndadzera kuno.” Labani anati, “Yankhulani.”
34 I rzekł: Jam jest sługa Abrahamów;
Motero iye anati, “Ine ndine wantchito wa Abrahamu.
35 A Pan ubłogosławił pana mego bardzo, i stał się możnym; bo mu nadał owiec, i wołów, i srebra, i złota, i sług, i służebnic, i wielbłądów, i osłów.
Yehova wadalitsa mbuye wanga kwambiri, ndiponso walemera. Wamupatsa nkhosa ndi ngʼombe, siliva ndi golide, antchito aamuna ndi antchito aakazi, komanso ngamira ndi abulu.
36 A urodziła Sara, żona pana mego syna panu memu, w starości jego, któremu dał wszystko, co ma.
Sara, mkazi wa mbuye wanga anamubalira iye mwana wamwamuna ngakhale kuti Sarayo anali wokalamba. Tsono mbuye wanga wamupatsa mwanayo chuma chonse.
37 I poprzysiągł mię pan mój, mówiąc: Nie weźmiesz żony synowi memu z córek Chananejskich, w których ziemi ja mieszkam;
Tsono mbuye wanga anandilumbiritsa kuti ndisunge mawu ake akuti, ‘Usadzamupezere mwana wanga mkazi kuchokera mwa atsikana a dziko lino la Kanaani,
38 Ale do domu ojca mego pójdziesz i do rodziny mojej; a weźmiesz stamtąd żonę synowi mojemu.
koma upite ku banja la abambo anga ndi kwa abale anga kuti ukamupezere mkazi mwana wanga.’”
39 I rzekłem do pana mego: Nie pójdzie snać ta niewiasta ze mną.
“Ndipo ine ndinati kwa mbuye wanga, ‘Nanga mkaziyo akakapanda kubwera nane pamodzi?’
40 Tedy mi odpowiedział: Pan, przed któregom ja obliczem chodził, pośle Anioła swego z tobą, i poszczęści drogę twoję; a weźmiesz żonę synowi memu z rodziny mojej, i z domu ojca mego.
“Iye anayankha, ‘Yehova amene ndakhala ndikumumvera nthawi zonse, adzatumiza mngelo wake kuti akuperekeze ndipo adzakuthandiza mpaka ukamupezere mwana wanga mkazi kuchokera ku mtundu wanga, wa fuko langa.
41 Tedy wolen będziesz od poprzysiężenia mego, gdy przyjdziesz do rodziny mojej; ale jeźlićby jej nie dano, wolen będziesz od poprzysiężenia mego.
Ukadzachita zimenezi udzakhala mfulu wosamangidwa ndi lumbiro langali. Koma tsono ukadzafika kwa fuko langa, ndipo ngati sadzalola kukupatsa mbeta ya mwana wanga, aponso udzamasuka ku lumbiro langali.’”
42 Przyszedłem tedy dziś do studni, i rzekłem Panie, Boże pana mego Abrahama, jeźliż ty teraz szczęścisz drogę moję, którę ja idę:
“Tsono lero lino pamene ndafika pa chitsime, ndinapempha kuti, ‘Yehova, Mulungu wa mbuye wanga, Abrahamu, ngati Inu mwandidalitsadi pa ulendowu,
43 Oto, ja stoję u studni wody; niechajże panienka, która wynijdzie czerpać wodę, a gdybym jej rzekł: Daj mi proszę napić się trochę wody z wiadra twego;
taonani ndayima pambali pa chitsime ichi; ndipo ndidzati kwa namwali amene atabwere kudzatunga kuti, chonde nditamwako madzi a mu mtsuko wakowu,’
44 A ona by rzekła do mnie: I ty pij, naczerpię też i wielbłądom twoim: ta będzie żoną, którą zgotował Pan synowi pana mego.
ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”
45 Niżelim ja tedy przestał mówić w sercu swem, oto, Rebeka wychodziła, niosąc wiadro swe na ramieniu swem, i przyszła do studni, a czerpała; którejm rzekł: Daj mi pić proszę.
“Ndisanatsirize kupemphera, ndinangoona Rebeka akutulukira mtsuko wake uli pa phewa. Anatsetserekera ku chitsime kukatunga madzi ndipo ndinati kwa iye, ‘Chonde patseko madzi akumwa.’
46 Ona tedy prędko złożywszy wiadro z siebie, rzekła: Pij, owszem i wielbłądy twoje napoję. I piłem; napoiła też i wielbłądy.
“Mofulumira, anatsitsa mtsuko wake pa phewa pake nati, ‘Imwani ndiponso ndizimwetsa madzi ngamira zanuzi.’ Kotero ine ndinamwa ndipo anamwetsanso ngamirazo.
47 I pytałem jej, mówiąc: Czyjaś ty córka? i odpowiedziała: Jestem córka Batuela, syna Nachorowego, którego mu urodziła Melcha, tedym włożył nausznice na twarz jej, i manele na ręce jej.
“Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,
48 Zatem pokłoniwszy się, dałem chwałę Panu, i błogosławiłem Panu, Bogu pana mego Abrahama, który mię prowadził drogą prawą, abym wziął córkę brata pana mego, synowi jego
kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
49 Przetoż teraz, jeźli chcecie uczynić miłosierdzie i prawdę z panem moim, oznajmijcie mi: a jeźli nie, powiedzcie mi też, żebym się obrócił na prawo albo na lewo.
Tsono ngati mukufuna kuonetsa kukoma mtima kwanu kwa mbuye wanga, ndikuonetsa kukhulupirika kwanu, ndiwuzeni; ndipo ngati si choncho ndiwuzeninso kuti ndidziwe chochita.”
50 Tedy odpowiedział Laban i Batuel, mówiąc: Od Pana ta rzecz wyszła; my tobie w niczem przeczyć nie możemy.
Labani ndi Betueli anayankha nati, “Izi ndi zochokera kwa Yehova, ndipo ife sitinganenepo kanthu.
51 Oto Rebeka przed tobą; weźmij ją, a idź; a niech będzie żoną syna pana twego, jako rzekł Pan.
Nayu Rebeka, mutengeni muzipita naye kuti akakhale mkazi wa mwana wa mbuye wanu, monga Yehova wanenera.”
52 I stało się, gdy usłyszał sługa Abrahamów słowa ich pokłonił się aż do ziemi Panu.
Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.
53 Zatem wyjął sługa on naczynia srebrne, i naczynia złote, i szaty, a oddał je Rebece; dał też upominki drogie bratu jej, i matce jej.
Kenaka wantchitoyo anatulutsa ziwiya zagolide ndi zasiliva ndi zovala nazipereka kwa Rebeka. Anaperekanso mphatso zina za mtengowapatali kwa mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka.
54 Jedli tedy i pili, on i mężowie, którzy z nim byli, i zostali tam na noc; a rano wstawszy, rzekł: Puśćcie mię do pana mego.
Tsono wantchito uja ndi anthu amene anali naye anadya, kumwa nagona komweko. Kutacha mmawa wake, wantchito uja anati, “Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
55 I rzekł brat jej, i matka jej: Niechaj pomieszka z nami dzieweczka dzień, albo dziesięć; potem pójdziesz.
Koma mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka anayankha kuti, “Muloleni mtsikanayu abakhala nafe masiku khumi kapena kupyolerapo, kenaka mukhoza kupita.”
56 A on rzekł do nich: Nie zatrzymywajcie mię, gdyż Pan poszczęścił drogę moję, puśćcie mię, abym jechał do pana mego.
Koma iye anawawuza kuti, “Chonde musandichedwetse. Yehova wandithandiza kale pa ulendo wanga. Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
57 Zatem rzekli: Zawołajmy dzieweczki, a spytajmy, co na to rzecze.
Koma iwo anati, “Bwanji timuyitane mtsikanayo ndipo timufunse ngati afuna kupita nanu panopa.”
58 Tedy zawołali Rebeki, i mówili do niej: Chceszże jechać z tym człowiekiem? A ona odpowiedziała: Pojadę.
Choncho iwo anamuyitana Rebeka uja namufunsa kuti, “Kodi ukufuna kupita ndi munthuyu panopa?” Iye anayankha kuti, “Ndipita.”
59 I puścili Rebekę siostrę swoję, z mamką jej, i sługę Abrahamowego, z mężami jego.
Kotero anamulola Rebeka pamodzi ndi mlezi wake kuti apite ndi wantchito wa Abrahamu pamodzi ndi anthu amene anali naye.
60 Tedy błogosławili Rebece, mówiąc jej: Siostraś nasza, rozmnóż się w tysiąc tysięcy, a niech posiądzie nasienie twoje bramy nieprzyjaciół swych.
Ndipo iwo anadalitsa Rebeka ndi kumuwuza kuti, “Iwe ndiwe mlongo wathu, Mulungu akudalitse iwe, ukhale mayi wa anthu miyandamiyanda; ndi kuti zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo.”
61 Tedy wstawszy Rebeka z dzieweczkami swemi, i wsiadłszy na wielbłądy jechały za onym mężem; i wziął sługa on Rebekę, i odjechał.
Kenaka Rebeka ndi antchito ake ananyamuka kukakwera ngamira zawo ndipo anapita naye pamodzi munthu uja. Choncho wantchito uja anatenga Rebeka nʼkumapita.
62 A Izaak wracał się z przechadzki od studni, którą zowią Żywiącego i Widzącego mię; bo mieszkał w ziemi południowej.
Pa nthawiyi nʼkuti Isake atafika kuchokera ku chitsime cha Wamoyo Wondipenya (Beeri-lahai-roi), popeza tsopano ankakhala ku Negevi.
63 A wyszedł był Izaak, dla modlitwy na pole pod wieczór, i podniósłszy oczy swe, ujrzał wielbłądy przychodzące.
Tsiku lina chakumadzulo, Isake anatuluka kukayendayenda ku munda, ndipo atakweza maso anaona ngamira zikubwera.
64 Podniosła też i Rebeka oczy swe, i ujrzała Izaaka, i zsiadła z wielbłąda;
Rebeka nayenso anatukula maso naona Isake. Ndipo anatsika pa ngamira yake
65 Bo rzekła do sługi: Cóż on za mąż, który idzie przez pole przeciwko nam? I odpowiedział sługa: Ten jest pan mój. A ona wziąwszy rańtuch nakryła się.
nafunsa wantchito uja kuti, “Kodi munthu uyo ndi ndani akuyenda mʼmundamo kubwera kudzakumana nafe?” Wantchitoyo anayankha, “Ndiye mbuye wanga.” Choncho Rebeka anatenga nsalu ndi kufunda kumaso.
66 I powiedział on sługa Izaakowi wszystko, co sprawił.
Tsono wantchito uja anawuza Isake zonse zimene anazichita.
67 I wprowadził ją Izaak do namiotu Sary, matki swojej; i wziął Rebekę, i była mu żoną, i miłował ją. I ucieszył się Izaak po śmierci matki swojej.
Isake analowa naye Rebeka mu tenti ya amayi ake Sara, ndipo anakhala mkazi wake. Isake anamukonda kwambiri Rebeka mkazi wake motero kuti zimenezi zinamutonthoza imfa ya amayi ake.

< Rodzaju 24 >