< Rodzaju 2 >

1 Dokończone tedy są niebiosa i ziemia, i wszystko wojsko ich.
Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.
2 I dokończył Bóg dnia siódmego dzieła swego, które uczynił; i odpoczął w dzień siódmy od wszelkiego dzieła swego, które uczynił.
Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse.
3 I błogosławił Bóg dniowi siódmemu, i poświęcił go; iż weń odpoczął od wszelkiego dzieła swego, które był stworzył Bóg, aby uczynione było.
Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
4 Teć są zrodzenia niebios, i ziemi, gdy były stworzone, dnia, którego uczynił Pan Bóg ziemię i niebo.
Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,
5 Wszelką różdżkę polną, przedtem niż była na ziemi; i wszelkie ziele polne, pierwej niż weszło; albowiem nie spuścił jeszcze był dżdżu Pan Bóg na ziemię; i człowieka nie było, któryby sprawował ziemię.
zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka,
6 Ale para wychodziła z ziemi, która odwilżała wszystek wierzch ziemi.
koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse.
7 Stworzył tedy Pan Bóg człowieka z prochu ziemi, i natchnął w oblicze jego dech żywota. I stał się człowiek duszą żywiącą.
Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
8 Nasadził też był Pan Bóg sad w Eden, na wschód słońca, i postawił tam człowieka, którego był stworzył.
Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja.
9 I wywiódł Pan Bóg z ziemi wszelkie drzewo wdzięczne na wejrzeniu, i smaczne ku jedzeniu: i drzewo żywota w pośrodku sadu; i drzewo wiadomości dobrego i złego.
Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.
10 A rzeka wychodziła z Eden dla odwilżenia sadu; i stamtąd dzieliła się na cztery główne rzeki;
Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi.
11 Imię jednej Fyson; ta okrąża wszystką ziemię Hewila, gdzie się rodzi złoto.
Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide.
12 A złoto ziemi onej jest wyborne. Tamże jest Bdellion, i kamień Onychyn.
(Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi).
13 A imię rzeki drugiej Gihon; ta okrąża wszystkę ziemię Murzyńską.
Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi.
14 Imię zaś rzeki trzeciej Chydekel, ta płynie na wschód słońca ku Asyryi. A rzeka czwarta jest Eufrates.
Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.
15 Wziął tedy Pan Bóg człowieka, i postawił go w sadzie Eden, aby go sprawował, i aby go strzegł.
Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira.
16 Tedy rozkazał Pan Bóg człowiekowi, mówiąc: Z każdego drzewa sadu jeść będziesz.
Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu;
17 Ale z drzewa wiadomości dobrego i złego, jeść z niego nie będziesz; albowiem dnia, którego jeść będziesz z niego, śmiercią umrzesz.
koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”
18 Rzekł też Pan Bóg: Nie dobrze być człowiekowi samemu; uczynię mu pomoc, która by była przy nim.
Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
19 A gdy stworzył Pan Bóg z ziemi wszelki zwierz polny, i wszelkie ptactwo niebieskie, tedy je przywiódł do Adama, aby obaczył jakoby je nazwać miał; a jakoby nazwał Adam każdą duszę żywiącą, tak aby było imię jej.
Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake.
20 Tedy dał Adam imiona wszystkiemu bydłu, i ptactwu niebieskiemu, i wszelkiemu zwierzowi polnemu. Lecz Adamowi nie była znaleziona pomoc, która by przy nim była.
Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse. Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza.
21 Tedy przypuścił Pan Bóg twardy sen na Adama, i zasnął; i wyjął jedno żebro jego, i napełnił ciałem miasto niego.
Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu.
22 I zbudował Pan Bóg z żebra onego, które wyjął z Adama, niewiastę, i przywiódł ją do Adama.
Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.
23 I rzekł Adam: Toć teraz jest kość z kości moich, i ciało z ciała mego; dla tegoż będzie nazwana mężatką, bo ona z męża wzięta jest.
Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
24 Przetoż opuści człowiek ojca swego i matkę swoję, a przyłączy się do żony swojej, i będą jednem ciałem.
Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
25 A byli oboje nadzy, Adam i żona jego; a nie wstydzili się.
Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.

< Rodzaju 2 >