< Galacjan 1 >

1 Paweł, Apostoł (nie od ludzi, ani przez człowieka, ale przez Jezusa Chrystusa i Boga Ojca, który go wzbudził od umarłych; )
Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
2 I wszyscy bracia, którzy są ze mną, zborom Galackim.
pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
3 Łaska wam i pokój niech będzie od Boga Ojca i Pana naszego, Jezusa Chrystusa.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
4 Który wydał samego siebie za grzechy nasze, aby nas wyrwał z teraźniejszego wieku złego według woli Boga i Ojca naszego; (aiōn g165)
Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn g165)
5 Któremu niech będzie chwała na wieki wieków. Amen. (aiōn g165)
Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
6 Dziwuję się, iż tak prędko dacie się przenosić od tego, który was powołał ku łasce Chrystusowej, do inszej Ewangielii;
Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
7 Która nie jest inszą; tylko niektórzy są, co was turbują i chcą wywrócić Ewangieliję Chrystusową.
umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
8 Ale choćbyśmy i my, albo Anioł z nieba opowiadał wam Ewangieliję mimo tę, którąśmy wam opowiadali, niech będzie przeklęty.
Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
9 Jakośmy przedtem powiedzieli i teraz znowu mówię: Jeźliby wam kto inną Ewangieliję opowiadał mimo tę, którąście przyjęli, niech będzie przeklęty.
Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
10 Albowiem terazże do ludzi was namawiam, czyli do Boga? Albo szukamli, abym się podobał ludziom? Zaiste, jeźlibym się jeszcze ludziom chciał podobać, nie byłbym sługą Chrystusowym.
Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
11 A oznajmuję wam bracia! iż Ewangielija, która jest opowiadana ode mnie, nie jest według człowieka.
Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
12 Albowiem ja anim jej wziął, anim się jej nauczył od człowieka, ale przez objawienie Jezusa Chrystusa.
Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
13 Boście słyszeli o mojem obcowaniu niekiedy w Żydostwie, żem nader prześladował zbór Boży i burzyłem go;
Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
14 I postępowałem w Żydostwie nad wiele rówieśników moich w narodzie moim, będąc nader gorliwym miłośnikiem ustaw moich ojczystych.
Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
15 Ale gdy się upodobało Bogu, który mię odłączył z żywota matki mojej, i powołał z łaski swojej,
Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
16 Aby objawił Syna swego we mnie, abym go opowiadał między poganami, wnetże nie radziłem się ciała i krwi;
kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
17 Anim się wrócił do Jeruzalemu, do tych, którzy przede mną byli Apostołami, alem szedł do Arabii i wróciłem się zasię do Damaszku.
Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
18 Potem po trzech latach wstąpiłem do Jeruzalemu, abym się ujrzał z Piotrem; i mieszkałem u niego piętnaście dni.
Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
19 A inszegom z Apostołów nie widział, oprócz Jakóba, brata Pańskiego.
Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
20 A co wam piszę, oto się przed Bogiem oświadczam, żeć nie kłamię.
Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
21 Zatemem przyszedł do krain Syryi i Cylicyi;
Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
22 A byłem nieznajomym z twarzy zborom żydowskim, które są w Chrystusie;
Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
23 Lecz tylko byli usłyszeli, iż ten, który prześladował nas niekiedy, teraz opowiada wiarę, którą przedtem burzył.
Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
24 I chwalili Boga ze mnie.
Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.

< Galacjan 1 >