< Ezdrasza 1 >

1 Roku pierwszego Cyrusa, króla Perskiego, aby się wypełniło słowo Pańskie powiedziane przez usta Jeremijaszowe, wzbudził Pan ducha Cyrusa, króla Perskiego, że kazał obwołać i rozpisać po wszystkiem królestwie swojem, mówiąc:
Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
2 Tak mówi Cyrus, król Perski: Wszystkie królestwa ziemi dał mi Pan, Bóg niebieski; i ten mi rozkazał, abym mu zbudował dom w Jeruzalemie, które jest w Judztwie.
Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
3 Kto tedy jest między wami ze wszystkiego ludu jego, z tym niech będzie Bóg jego, a ten niech idzie do Jeruzalemu, które jest w Judztwie, a niech buduje dom Pana, Boga Izraelskiego; onci jest Bóg, który jest w Jeruzalemie.
Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
4 A ktoby został w któremkolwiek miejscu, gdzie jest przychodniem, niech go podpomogą mężowie miejsca onego srebrem i złotem, i majętnością, i bydłem, oprócz dobrowolnej ofiary na dom Boży, który jest w Jeruzalemie.
Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
5 Tedy powstali przedniejsi z domów ojcowskich, z Judy i z Benjamina, i kapłani, i Lewitowie; wszelki, którego ducha pobudził Bóg, aby szli, a budowali dom Pański, który jest w Jeruzalemie;
Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
6 Których wszyscy mieszkający około nich wspomagali naczyniem srebrnem i złotem, majętnością, i bydłem, i rzeczami kosztownemi, oprócz wszystkiego, co dobrowolnie ofiarowano.
Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
7 Król też Cyrus wyniósł naczynia domu Pańskiego (które był zabrał Nabuchodonozor z Jeruzalemu, a oddał je był do domu Boga swego).
Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
8 A wyniósł je Cyrus, król Perski, przez ręce Mitrydatesa podskarbiego, który je pod liczbą oddał Sesbasarowi, książęciu Judzkiemu.
Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
9 A tak jest liczba ich: Miednic złotych trzydzieści, miednic srebrnych tysiąc, nożów dwadzieścia i dziwięć.
Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
10 Kubków złotych trzydzieści, kubków srebrnych podlejszych cztery sta i dziesięć, a naczynia innego tysiącami.
timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
11 Wszystkiego naczynia złotego i srebrnego pięć tysięcy i cztery sta; wszystko to wyniósł Sesbasar, gdy się prowadził lud z niewoli, z Babilonu do Jeruzalemu.
Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.

< Ezdrasza 1 >