< Ezechiela 9 >

1 Potem zawołał, gdziem ja słyszał, głosem wielkim, mówiąc: Hetmani, nastąpcie na to miasto, mając każdy broń swoję ku zabijaniu w ręce swej.
Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
2 A oto sześć mężów przyszło drogą ku brami wyższej, która patrzy na północy, i miał każdy broń swoję ku wytraceniu w ręce swej; ale mąż jeden był w pośród nich odziany szatą lnianą, a kałamarz pisarski przy biodrach jego; i przyszedłszy stanęli u ołtarza miedzanego.
Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
3 A chwała Boga Izraelskiego zstąpiła była z Cherubina, na którym była, do progu domu, i zawołała na męża onego odzianego szatą lnianą, przy którego biodrach był kałamarz pisarski.
Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
4 I rzekł Pan do niego: Przejdź przez pośrodek miasta, przez pośrodek Jeruzalemu, a uczyń znak na czołach mężów, którzy wzdychają i narzekają nad wszystkiemi obrzydliwościami, które się dzieją w pośród niego.
ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
5 A onym rzekł, gdziem ja słyszał: Idźcie po mieście za nim; a zabijajcie; niech nie folguje oko wasze, ani się zmiłujcie.
Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
6 Starca, młodzieńca, i pannę, i maluczkich, i niewiasty wybijcie do szczętu; ale do żadnego męża, na którymby był znak, nie przystępujcie, od świątnicy mojej poczniecie. A tak poczęli od onych mężów starszych, którzy byli przed domem Pańskim;
Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
7 (Bo im był rzekł: Splugawcie ten dom, a napełnijcie sieni pobitymi; idźcież.) A wyszedłszy zabijali w miście.
Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
8 A gdy ich pozabijali, a jam pozostał, tedym padł na oblicze moje, i zawołałem a rzekłem: Ach panujący Panie! izali ty wytracisz wszystek ostatek Izraelski, wylewając popędliwość swoję na Jeruzalem?
Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
9 I rzekł do mnie: Nieprawość domu Izraelskiego i Judzkiego nader jest bardzo wielka, i napełniona jest ziemia krwią, a miasto pełne jest przewrotności; bo mówili: Pan tę ziemię opuścił, a Pan nie widzi nas.
Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
10 Przetoż i Ja toż uczynię, nie sfolguje oko moje, ani się zmiłuję, drogę ich na głowę ich obrócę.
Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
11 A oto mąż on odziany szatą lnianą, przy którego biodrach był kałamarz, oznajmił to mówiąc: Uczyniłem tak, jakoś mi rozkazał.
Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”

< Ezechiela 9 >