< Ezechiela 38 >

1 I stało się słowo Pańskie do mnie mówiąc:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Synu człowieczy! obróć twarz swoję przeciw Gogowi w ziemi Magog, książęciu głównemu w Mesech i Tubal, a prorokuj przeciw niemu.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 I rzecz: Tak mówi panujący Pan: Otom Ja przeciw tobie, o Gogu, księciu główny w Mesechu i w Tubalu!
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 Bo cię zawrócę, i włożę wędzidło w czeluści twoje, i wywiodę cię, i wszystko wojsko twoje, konie i jezdnych wszystkich poubieranych w zupełny kirys, hufy wielkie z tarczami i z przyłbicami, wszystkich tych, którzy władają mieczem.
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Persów, Murzynów i Putejczyków z nimi, tych wszystkich z tarczami i z przyłbicami;
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gomer i wszystkie hufy jego, dom Togormy mieszkającego w stronach północnych, i wszystkie poczty jego, narodów wiele z tobą.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Gotuj się, a wypraw się, ty i wszystkie półki twoje, które się zebrały do ciebie, a bądź stróżem ich.
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 Po wielu dniach nawiedziony będziesz, a w ostatnie lata przyciągniesz na lud uwolniony od miecza, i zebrany z wielu narodów, na góry Izraelskie, które były pustynią ustawiczną, gdyż oni z narodów będąc wywiedzieni, wszyscy bezpiecznie mieszkać będą.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 W tem przyciągniesz i przyjdziesz jako burza, będziesz jako obłok okrywający ziemię, ty i wszystkie poczty twoje, i wiele narodów z tobą.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 Tak mówi panujący Pan: Dnia onego wstąpią dziwne rzeczy na serce twoje, a będziesz złe zamysły myślał,
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 I rzeczesz: Wtargnę do ziemi, w której są wsi; przypadnę na spokojnych i bezpiecznie mieszkających, na wszystkich, którzy mieszkają bez muru, a zawór i bram nie mają;
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 Abym wziął łupy, a rozchwycił korzyści; abym obrócił rękę swoję na spustoszone miejsca już znowu osadzone, i na lud zgromadzony z narodów, którzy się bydłem i kupiectwem bawią, a mieszkają w pośrodku ziemi.
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Seba, i Dedan, i kupcy morscy, i wszystkie lwięta jego rzekną do ciebie: Izali ty na branie łupów idziesz? Izali na rozchwycenie korzyści zebrałeś półki twoje, abyś wybrał srebro i złoto, i zabrał dobytek i majętności, a żebyś zebrał łup wielki?
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 Przetoż prorokuj, synu człowieczy! a mów do Goga: Tak mówi panujący Pan: Izali się w on dzień, gdy lud mój Izraelski bezpiecznie mieszkać będzie, nie dowiesz?
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 I przyjdziesz z miejsca swego z stron północnych, ty i narodów wiele z tobą, wszyscy wsiadający na konie, lud wielki i wojsko gwałtowne;
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 I przypadniesz na lud mój Izraelski jako obłok, abyś okrył tę ziemię. W ostatnie dni przywiodę cię do ziemi mojej, aby mię poznały narody, gdy będę poświęcony w tobie, przed oczyma ich, o Gogu!
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 Tak mówi panujący Pan: Azażeś ty nie jest on, o którymem powiedział za dni dawnych przez sług moich, proroków Izraelskich, którzy prorokowali za dni onych lat, żem cię miał przywieść na nich?
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 Wszakże w on dzień, w dzień, którego przyciągnie Gog na ziemię Izraelską, mówi panujący Pan, wzruszy się gniew mój w popędliwości mojej;
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 A w gorliwości mojej, i w ogniu gniewu mego mówić będę, że dnia onego będzie wielki rozruch w ziemi Izraelskiej;
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 I zadrżą od obliczności mojej ryby morskie, i ptastwo niebieskie, i zwierz polny, i wszelka gadzina płazająca się po ziemi, i wszyscy ludzie, którzy są na obliczu ziemi; i porozwalają się góry, i upadną wysokie wieże, i każdy mur obali się na zie mię.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 Bo przywołam przeciwko niemu po wszystkich górach moich miecz, mówi panujący Pan; miecz każdego obróci się na brata jego.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 I będę się z nim sądził morem i krwią, a deszcz gwałtowny i grad kamienny, ogień i siarkę spuszczę nań, i na wojska jego, i na wiele narodów, które z nim będą.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 I pokażę się wielmożnym, i poświęcę się, i znajomym się uczynię przed oczyma wielu narodów, i dowiedzą się, żem Ja Pan.
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezechiela 38 >