< Ezechiela 37 >

1 Była nademną ręka Pańska, i wywiódł mię Pan w duchu, i postawił mię w pośrodku pola, które było pełne kości;
Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
2 I przewiódł mię przez nie w około a w około, a oto było ich bardzo wiele na onem polu, a oto były bardzo suche.
Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
3 I rzekł do mnie: Synu człowieczy! ożyjąli te kości? I rzekłem: Panujący Panie! ty wiesz.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
4 W tem rzekł do mnie: Prorokuj o tych kościach, a mów do nich: Kości suche, słuchajcie słowa Pańskiego!
Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
5 Tak mówi panujący Pan o tych kościach: Oto ja wprowadzę w was ducha, a ożyjecie;
Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
6 A włożę na was żyły, i uczynię, że porośnie na was mięso, i powlekę was skórą, a dam wam ducha, i ożyjecie, i poznacie, żem Ja Pan.
Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
7 Prorokowałem tedy, jako mi rozkazano; i stał się szum, gdym ja prorokował, a oto poruszenie; i przystąpiły kości, kość do kości swojej.
Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
8 I ujrzałem, a oto na nich żyły, i mięso porosło, i powleczone były skórą po wierzchu; ale ducha nie było w nich.
Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
9 I rzekł do mnie: Prorokuj do ducha, prorokuj, synu człowieczy! i rzecz do ducha: Tak mówi panujący Pan: Od czterech wiatrów przyjdź, duchu! i natchnij te pobite, a niech ożyją.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
10 Prorokowałem tedy jako mi był rozkazał, i wstąpił w nie duch, a ożyły, i stanęły na nogach swoich, wojsko nader bardzo wielkie.
Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
11 I rzekł do mnie: Synu człowieczy! te kości są wszystek dom Izraelski. Oto mówią: Wyschły kości nasze, i zginęła nadzieja nasza, wygładzeni jesteśmy.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
12 Dlategoż prorokuj, a mów do nich: Tak mówi panujący Pan: Oto Ja otworzę groby wasze, i wywiodę was z grobów waszych, ludu mój! i przywiodę was do ziemi Izraelskiej!
Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
13 I dowiecie się, żem Ja Pan, gdy Ja otworzę groby wasze, a wywiodę was z grobów waszych, ludu mój!
Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
14 I dam w was ducha mego, a ożyjecie, i dam wam odpocząć w ziemi waszej; i dowiecie się, że Ja Pan mówię to i uczynię, mówi Pan.
Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
15 I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anandiyankhula kuti:
16 A ty, synu człowieczy! weźmij sobie jedno drewno, i napisz na niem: Judzie i synom Izraelskim, towarzyszom jego. Weźmij też i drugie drewno, a napisz na niem: Józefowi drewnu Efraimowemu, i wszystkiemu domowi Izraelskiemu, towarzyszom jego!
“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
17 I złóż je sobie jedno do drugiego w jedno drewno, aby były jako jedno w ręce twojej.
Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
18 A gdy rzekną do ciebie synowie ludu twego, mówiąc: Izali nam nie oznajmisz, co przez to rozumiesz?
“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
19 Rzeczesz im: Tak mówi panujący Pan: Oto Ja wezmę drewno Józefowe, które jest w ręce Efraimowej i pokolenia Izraelskie, towarzyszów jego, i przyłożę je z nim do drewna Judowego, i uczynię je jednem drewnem, a będą jednem w ręce mojej.
iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
20 A gdy będą one drewna, na których napiszesz, w ręce twojej przed oczyma ich,
Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
21 Tedy rzecz do nich: Tak mówi panujący Pan: Oto Ja wezmę synów Izraelskich z pośrodku tych narodów, do których byli zaszli, i zgromadzę ich zewsząd, a przywiodę ich do ziemi ich;
udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
22 I uczynię ich narodem jednym w ziemi, na górach Izraelskich, i będzie król jeden nad onymi wszystkimi za króla; a nie będą więcej dwa narody, nie rozdzielą się nigdy więcej na dwoje królestw;
Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
23 Nie splugwią się więcej plugawemi bałwanami swemi, i obrzydliwościami swemi, ani jakiemi przestępstwy swemi; i wybawię ich z każdego mieszkania ich, gdzie zgrzeszyli, i oczyszczę ich, i będą ludem moim, a Ja będę Bogiem ich.
Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
24 A sługa mój Dawid będzie królem nad nimi, i pasterza jednego wszyscy mieć będą, aby w sądach moich chodzili, i ustaw moich przestrzegali, i czynili je.
“‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
25 I będą mieszkać w onej ziemi, którąm był dał słudze memu Jakóbowi, w której mieszkali ojcowie wasi; będą, mówię, w niej mieszkali oni i synowie ich, i synowie synów ich aż na wieki, a Dawid, sługa mój, będzie książęciem ich na wieki.
Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
26 I uczynię też z nimi przymierze pokoju, a przymierze wieczne będzie z nimi; i osadzę ich i rozmnożę ich, i założę świątnicę moję w pośrodku ich na wieki.
Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
27 I będzie przybytek mój między nimi, i będę Bogiem ich, a oni będą ludem moim.
Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
28 I dowiedzą się narody, żem Ja Pan, który poświęcam Izraela, gdy będzie świątnica moja w pośrodku ich na wieki.
Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”

< Ezechiela 37 >